Masalimo 127 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 127:1-5

Salimo 127

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni.

1Yehova akapanda kumanga nyumba,

omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe.

Yehova akapanda kulondera mzinda,

mlonda akanangolondera pachabe.

2Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa

ndi kusagona msanga madzulo,

kuvutikira chakudya choti mudye,

pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.

3Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova,

ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.

4Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja

mwa munthu wankhondo.

5Wodala munthu

amene motengera mivi mwake mwadzaza.

Iwo sadzachititsidwa manyazi

pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

New International Reader’s Version

Psalm 127:1-5

Psalm 127

A song for those who go up to Jerusalem to worship the Lord. A psalm of Solomon.

1If the Lord doesn’t build a house,

the work of the builders is useless.

If the Lord doesn’t watch over a city,

it’s useless for those on guard duty to stand watch over it.

2It’s useless for you to work from early morning

until late at night

just to get food to eat.

God provides for those he loves even while they sleep.

3Children are a gift from the Lord.

They are a reward from him.

4Children who are born to people when they are young

are like arrows in the hands of a soldier.

5Blessed are those

who have many children.

They won’t be put to shame

when they go up against their enemies in court.