Salimo 125
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,
limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2Monga mapiri azungulira Yerusalemu,
momwemonso Yehova azungulira anthu ake
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala
pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,
kuti anthu olungamawo
angachite nawonso zoyipa.
4Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,
amene ndi olungama mtima
5Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,
Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.
Mtendere ukhale pa Israeli.
Psalm 125
A song of ascents.
1Those who trust in the Lord are like Mount Zion,
which cannot be shaken but endures for ever.
2As the mountains surround Jerusalem,
so the Lord surrounds his people
both now and for evermore.
3The sceptre of the wicked will not remain
over the land allotted to the righteous,
for then the righteous might use
their hands to do evil.
4Lord, do good to those who are good,
to those who are upright in heart.
5But those who turn to crooked ways
the Lord will banish with the evildoers.
Peace be on Israel.