Salimo 124
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5madzi a mkokomo
akanatikokolola.
6Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Salimo 124
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5madzi a mkokomo
akanatikokolola.
6Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.