Salimo 124
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5madzi a mkokomo
akanatikokolola.
6Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Песнь 124
Песнь восхождения.
1Те, кто надеется на Вечного, – как гора Сион:
не поколеблются, пребудут вовеки.
2Как горы окружают Иерусалим,
так Вечный окружает Свой народ
отныне и вовеки.
3Не вечно власти нечестивых
быть на земле, принадлежащей праведным,
иначе праведные, по их примеру,
сами станут творить беззаконие.
4Будь добр, Вечный, к добрым
и правым в сердцах своих.
5Но тех, кто следует кривыми путями,
да отвергнет Вечный вместе со злодеями.
Мир Исроилу!