Masalimo 12 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 12:1-8

Salimo 12

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide.

1Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika;

okhulupirika akusowa pakati pa anthu.

2Aliyense amanamiza mʼbale wake;

ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.

3Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo

ndi pakamwa paliponse podzikuza.

4Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu;

pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”

5“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu

ndi kubuwula kwa anthu osowa,

Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova,

“Ndidzawateteza kwa owazunza.”

6Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro

monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi,

oyengedwa kasanu nʼkawiri.

7Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo

mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.

8Oyipa amangoyendayenda ponseponse

anthu akamayamikira zochita zawo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Забур 12:1-6

Песнь 12

1Дирижёру хора. Песнь Довуда.

2Как долго, Вечный? Неужели забыл Ты меня навеки?

Как долго Ты будешь скрывать от меня Своё лицо?

3Как долго будет переживание терзать мою душу

и боль – ежедневно сокрушать моё сердце?

Как долго врагу моему надо мной кичиться?

4Посмотри на меня и ответь, Вечный, мой Бог.

Глаза мои просветли,

чтобы мне не уснуть смертным сном,

5чтобы враг не сказал: «Я его превозмог»,

и когда я паду, не радовались бы недруги мои.

6Я уповаю на Твою милость,

моё сердце возрадуется спасению Твоему.

Вечному буду петь,

потому что Он благ ко мне.