Masalimo 116 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 116:1-19

Salimo 116

1Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga;

Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.

2Pakuti ananditchera khutu,

ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.

3Zingwe za imfa zinandizinga,

zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera;

ndinapeza mavuto ndi chisoni.

4Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova:

“Inu Yehova, pulumutseni!”

5Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama

Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.

6Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima;

pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.

7Pumula iwe moyo wanga,

pakuti Yehova wakuchitira zokoma.

8Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa,

maso anga ku misozi,

mapazi anga kuti angapunthwe,

9kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

10Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati,

“Ndasautsidwa kwambiri.”

11Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati,

“Anthu onse ndi abodza.”

12Ndingamubwezere chiyani Yehova,

chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?

13Ndidzakweza chikho cha chipulumutso

ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.

14Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova

pamaso pa anthu ake onse.

15Imfa ya anthu oyera mtima

ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.

16Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu:

ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu;

Inu mwamasula maunyolo anga.

17Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu

ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.

18Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova

pamaso pa anthu ake onse,

19mʼmabwalo a nyumba ya Yehova,

mʼkati mwako iwe Yerusalemu.

Tamandani Yehova.

New International Version – UK

Psalms 116:1-19

Psalm 116

1I love the Lord, for he heard my voice;

he heard my cry for mercy.

2Because he turned his ear to me,

I will call on him as long as I live.

3The cords of death entangled me,

the anguish of the grave came over me;

I was overcome by distress and sorrow.

4Then I called on the name of the Lord:

Lord, save me!’

5The Lord is gracious and righteous;

our God is full of compassion.

6The Lord protects the unwary;

when I was brought low, he saved me.

7Return to your rest, my soul,

for the Lord has been good to you.

8For you, Lord, have delivered me from death,

my eyes from tears,

my feet from stumbling,

9that I may walk before the Lord

in the land of the living.

10I trusted in the Lord when I said,

‘I am greatly afflicted’;

11in my alarm I said,

‘Everyone is a liar.’

12What shall I return to the Lord

for all his goodness to me?

13I will lift up the cup of salvation

and call on the name of the Lord.

14I will fulfil my vows to the Lord

in the presence of all his people.

15Precious in the sight of the Lord

is the death of his faithful servants.

16Truly I am your servant, Lord;

I serve you just as my mother did;

you have freed me from my chains.

17I will sacrifice a thank-offering to you

and call on the name of the Lord.

18I will fulfil my vows to the Lord

in the presence of all his people,

19in the courts of the house of the Lord

in your midst, Jerusalem.

Praise the Lord.116:19 Hebrew Hallelu Yah