Masalimo 113 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 113:1-9

Salimo 113

1Tamandani Yehova.

Mutamandeni, inu atumiki a Yehova,

tamandani dzina la Yehova.

2Yehova atamandidwe,

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake,

dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.

4Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse,

ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.

5Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu,

Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?

6amene amawerama pansi kuyangʼana

miyamba ndi dziko lapansi?

7Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi

ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;

8amawakhazika pamodzi ndi mafumu,

pamodzi ndi mafumu a anthu ake.

9Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake

monga mayi wa ana wosangalala.

Tamandani Yehova.

Het Boek

Psalmen 113:1-9

1Prijs de Here!

Dienaars van de Here,

loof en prijs zijn naam!

2Laat de naam van de Here

worden geprezen en geëerd,

nu en tot in eeuwigheid.

3Over de hele aarde

moet de naam van de Here worden geprezen.

4De Here staat boven alle mensen en volken.

Hoog boven de hemelen troont zijn heerlijkheid.

5Is iemand te vergelijken met de Here?

Met onze God, die zo onmeetbaar hoog woont?

6Met onze God, die zo heel laag moet neerzien

om te zien wat in de hemel en op aarde gebeurt?

7Hij helpt kleine mensen opstaan uit het stof

en armen tilt Hij op uit de modder.

8Hij laat hen zitten bij de vooraanstaanden uit het volk.

9Onvruchtbare vrouwen verandert Hij in gelukkige moeders.

Prijs de Here!