Salimo 112
1Tamandani Yehova.
Wodala munthu amene amaopa Yehova,
amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6Ndithu sadzagwedezeka;
munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;
nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;
adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.
Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Псалам 112
1Славите Господа!
Благо човеку што се Господа боји
и у заповестима његовим радо ужива.
2Моћно ће му потомство бити по земљи,
нараштај ће праведника благословен бити.
3У кући му благо и иметак,
праведност му постојана вавек.
4Светло и у тами сија праведнима,
милосрднима, милостивима и правичнима.
5Сажаљив је добар човек, позајмљује,
праведно се у послу опходи.
6Тај се никад уздрмати неће,
сећање на праведника трајаће довека.
7Он не стрепи пред лошим вестима,
поузданог срца у Господа се узда.
8Прибраног је срца, не страхује
док не заликује над душманима својим.
9Он нештедимице дели,
даје сиротињи,
праведност његова остаје довека;
рог ће му се у части уздићи.
10Видеће то злотвор, озлоједиће се,
шкрипаће зубима и гришће се;
пропашће жудња злотвора!