Masalimo 112 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 112:1-10

Salimo 112

1Tamandani Yehova.

Wodala munthu amene amaopa Yehova,

amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.

2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;

mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.

3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;

wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.

5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,

amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

6Ndithu sadzagwedezeka;

munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.

7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;

mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.

8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;

potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.

9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,

chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;

nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.

10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;

adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.

Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

New Serbian Translation

Псалми 112:1-10

Псалам 112

1Славите Господа!

Благо човеку што се Господа боји

и у заповестима његовим радо ужива.

2Моћно ће му потомство бити по земљи,

нараштај ће праведника благословен бити.

3У кући му благо и иметак,

праведност му постојана вавек.

4Светло и у тами сија праведнима,

милосрднима, милостивима и правичнима.

5Сажаљив је добар човек, позајмљује,

праведно се у послу опходи.

6Тај се никад уздрмати неће,

сећање на праведника трајаће довека.

7Он не стрепи пред лошим вестима,

поузданог срца у Господа се узда.

8Прибраног је срца, не страхује

док не заликује над душманима својим.

9Он нештедимице дели,

даје сиротињи,

праведност његова остаје довека;

рог ће му се у части уздићи.

10Видеће то злотвор, озлоједиће се,

шкрипаће зубима и гришће се;

пропашће жудња злотвора!