Salimo 112
1Tamandani Yehova.
Wodala munthu amene amaopa Yehova,
amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6Ndithu sadzagwedezeka;
munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;
nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;
adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.
Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Le bonheur des fidèles112 Psaume alphabétique (cf. note 9.1) qui répond au Ps 111.
1Louez l’Eternel112.1 Voir 111.1. !
Heureux est l’homme qui craint l’Eternel
et trouve un grand plaisir ╵à ses commandements !
2Sa postérité sera forte ╵dans le pays
et la génération du juste ╵sera bénie.
3Abondance et richesse ╵règnent dans sa maison,
et sa conduite juste ╵sera pour toujours prise en compte112.3 En hébreu, la formulation est identique à celle de Ps 111.3b, mais le contexte implique un sens différent..
4Une lumière luit ╵dans les ténèbres, ╵pour les gens droits,
ceux qui font grâce, ╵qui sont compatissants et justes112.4 Voir 111.4..
5Il est bon qu’un homme ait de l’empathie ╵et qu’il prête à autrui,
et qu’avec équité, ╵il gère ses affaires ;
6ainsi ne trébuchera-t-il jamais,
et l’on se souviendra ╵du juste pour toujours.
7Il ne craint pas ╵de mauvaises nouvelles,
il a le cœur tranquille, ╵confiant en l’Eternel.
8Plein d’assurance, ╵il est sans crainte,
dans l’attente de voir ╵le sort réservé à ses ennemis.
9Il donne aux pauvres ╵avec largesse,
et sa conduite juste ╵sera pour toujours prise en compte112.9 Voir note v. 3. Cité en 2 Co 9.9 d’après l’ancienne version grecque..
Il peut garder la tête haute ╵et il est honoré.
10Le méchant le constate ╵et s’en irrite,
grince des dents ╵et se démoralise.
Le désir des méchants ╵n’aboutira à rien.