Masalimo 111 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 111:1-10

Salimo 111

1Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse

mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;

onse amene amakondwera nazo amazilingalira.

3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.

5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;

amakumbukira pangano lake kwamuyaya.

6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.

7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;

malangizo ake onse ndi odalirika.

8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,

ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.

9Iyeyo amawombola anthu ake;

anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya

dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;

onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.

Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

Hoffnung für Alle

Psalm 111:1-10

Was Gott tut, ist einzigartig!

1Halleluja – lobt den Herrn!

Von ganzem Herzen will ich dem Herrn danken

vor allen, die aufrichtig mit ihm leben – ja, vor der ganzen Gemeinde!

2Wie gewaltig ist alles, was der Herr vollbracht hat!

Wer sich über seine Taten freut, denkt immer wieder darüber nach.

3Was Gott tut, ist eindrucksvoll und einzigartig;

auf seine Gerechtigkeit ist für immer Verlass.

4Er selbst hat alles dafür getan,

dass seine Wunder nicht in Vergessenheit geraten.

Gnädig und barmherzig ist der Herr!

5Denen, die ihn achteten, gab er immer genug zu essen.

Niemals vergisst er den Bund, den er mit Israel geschlossen hat.

6Er bewies ihnen seine große Macht:

Die Länder anderer Völker gab er ihnen zum Besitz.

7Er ist zuverlässig und gerecht in allem, was er tut;

seinen Geboten kann man völlig vertrauen.

8Niemals verlieren sie ihre Gültigkeit,

von Anfang bis Ende bezeugen sie seine Wahrhaftigkeit und Treue.

9Der Herr hat sein Volk erlöst

und einen ewigen Bund mit ihnen geschlossen.

Heilig und furchterregend ist sein Name!

10Alle Weisheit fängt damit an,

dass man Ehrfurcht vor dem Herrn hat.

Ja, klug ist, wer sein Leben nach Gottes Geboten ausrichtet.

Nie wird das Lob des Herrn verstummen!