Masalimo 11 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 11:1-7

Salimo 11

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Yehova ine ndimathawiramo.

Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti,

“Thawira ku phiri lako ngati mbalame.

2Pakuti taona oyipa akunga mauta awo;

ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta,

pobisala pawo kuti alase

olungama mtima.

3Tsono ngati maziko awonongeka,

olungama angachite chiyani?”

4Yehova ali mʼNyumba yake yoyera;

Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba.

Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu;

maso ake amawayesa.

5Yehova amayesa olungama,

koma moyo wake umadana ndi oyipa,

amene amakonda zachiwawa.

6Iye adzakhuthulira pa oyipa

makala amoto ndi sulufule woyaka;

mphepo yotentha idzakhala yowayenera.

7Pakuti Yehova ndi wolungama,

Iye amakonda chilungamo;

ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 11:1-7

Tilflugt hos Herren

1Til korlederen: En sang af David.

Jeg stoler på Herren og søger hans hjælp.

Hvorfor siger I: „Flygt op i bjergene som en fugl,

2for de gudløse har spændt deres bue og lagt pilen til rette.

De gemmer sig i mørket for at ramme de retskafne.

3Hvad kan en gudfrygtig gøre, når al lov og ret er borte?”

4Herren sidder i sit hellige tempel.

Han regerer fra sin trone i Himlen.

Han overvåger hvert menneske på jorden.

5Han gennemskuer både de gode og de gudløse.

Han hader dem, som elsker vold.

6Han lader gloende kul regne ned over de onde,

straffer dem med rygende svovl og en brændende vind.

7Herren er god og elsker dem, der adlyder ham,

de, som gør det gode, skal se hans ansigt.