Masalimo 109 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 109:1-31

Salimo 109

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mulungu amene ndimakutamandani,

musakhale chete,

2pakuti anthu oyipa ndi achinyengo

atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane;

iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.

3Andizungulira ndi mawu audani,

amandinena popanda chifukwa.

4Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza,

koma ine ndine munthu wapemphero.

5Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino,

ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.

6Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye;

lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.

7Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa,

ndipo mapemphero ake amutsutse.

8Masiku ake akhale owerengeka;

munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.

9Ana ake akhale amasiye

ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.

10Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha;

apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.

11Wokongoza alande zonse zimene ali nazo;

alendo afunkhe ntchito za manja ake.

12Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima

kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.

13Zidzukulu zake zithe nʼkufa,

mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.

14Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova;

tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.

15Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,

kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.

16Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo,

koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka

ndi osweka mtima.

17Anakonda kutemberera,

matembererowo abwerere kwa iye;

sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena,

choncho madalitso akhale kutali naye.

18Anavala kutemberera ngati chovala;

kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi,

kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.

19Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho,

ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.

20Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga,

kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.

21Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

muchite nane molingana ndi dzina lanu,

chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.

22Pakuti ndine wosauka ndi wosowa,

ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.

23Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo,

ndapirikitsidwa ngati dzombe.

24Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya,

thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.

25Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane;

akandiona, amapukusa mitu yawo.

26Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga;

pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.

27Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu,

kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.

28Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa;

pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi,

koma mtumiki wanu adzasangalala.

29Onditsutsa adzavekedwa mnyozo,

ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.

30Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri;

ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.

31Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo,

kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 109:1-31

Salmo 109

Al director musical. Salmo de David.

1Oh Dios, alabanza mía,

no guardes silencio.

2Pues gente impía y mentirosa

ha declarado en mi contra,

y con lengua engañosa me difaman;

3con expresiones de odio me acosan,

y sin razón alguna me atacan.

4Mi amor me lo pagan con calumnias,

mientras yo me encomiendo a Dios.

5Mi bondad la pagan con maldad;

en vez de amarme, me aborrecen.

6Pon en su contra a un malvado;

que a su derecha esté su acusador.109:6 esté su acusador. Alt. esté Satán.

7Que resulte culpable al ser juzgado,

y que sus propias oraciones lo condenen.

8Que se acorten sus días,

y que otro se haga cargo de su oficio.

9Que se queden huérfanos sus hijos;

que se quede viuda su esposa.

10Que anden sus hijos vagando y mendigando;

que anden rebuscando entre las ruinas.

11Que sus acreedores se apoderen de sus bienes;

que gente extraña saquee sus posesiones.

12Que nadie le extienda su bondad;

que nadie se compadezca de sus huérfanos.

13Que sea exterminada su descendencia;

que desaparezca su nombre en la próxima generación.

14Que recuerde el Señor la iniquidad de su padre,

y no se olvide del pecado de su madre.

15Que no les quite el Señor la vista de encima,

y que borre de la tierra su memoria.

16Por cuanto se olvidó de hacer el bien,

y persiguió hasta la muerte

a pobres, afligidos y menesterosos,

17y porque le encantaba maldecir,

¡que caiga sobre él la maldición!

Por cuanto no se complacía en bendecir,

¡que se aleje de él la bendición!

18Por cuanto se cubrió de maldición

como quien se pone un vestido,

¡que esta se filtre en su cuerpo como el agua!,

¡que penetre en sus huesos como el aceite!

19¡Que lo envuelva como un manto!

¡Que lo apriete en todo tiempo como un cinto!

20¡Que así les pague el Señor a mis acusadores,

a los que me calumnian!

21Pero tú, Señor Soberano,

trátame bien por causa de tu nombre;

líbrame por tu bondad y gran amor.

22Ciertamente soy pobre y estoy necesitado;

profundamente herido está mi corazón.

23Me voy desvaneciendo como sombra vespertina;

se desprenden de mí como de una langosta.

24De tanto ayunar me tiemblan las rodillas;

la piel se me pega a los huesos.

25Soy para ellos motivo de burla;

me ven, y menean la cabeza.

26Señor mi Dios, ¡ayúdame!;

por tu gran amor, ¡sálvame!

27Que sepan que esta es tu mano;

que tú mismo, Señor, lo has hecho.

28¿Qué importa que ellos me maldigan?

¡Bendíceme tú!

Pueden atacarme, pero quedarán avergonzados;

en cambio, este siervo tuyo se alegrará.

29¡Queden mis acusadores cubiertos de deshonra,

envueltos en un manto de vergüenza!

30Por mi parte, daré muchas gracias al Señor;

lo alabaré entre una gran muchedumbre.

31Porque él aboga por el109:31 aboga por el. Lit. está de pie a la diestra del. necesitado

para salvarlo de quienes lo condenan.