Masalimo 106 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 106:1-48

Salimo 106

1Tamandani Yehova.

Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

2Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova

kapena kumutamanda mokwanira?

3Odala ndi amene amasunga chilungamo,

amene amachita zolungama nthawi zonse.

4Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu,

bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,

5kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika,

kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu

ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.

6Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu;

tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.

7Pamene makolo athu anali mu Igupto,

sanalingalire za zozizwitsa zanu;

iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka,

ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.

8Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake,

kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.

9Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma;

anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.

10Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo;

anawawombola mʼdzanja la mdani.

11Madzi anamiza adani awo,

palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.

12Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake

ndi kuyimba nyimbo zamatamando.

13Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita,

ndipo sanayembekezere uphungu wake.

14Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo;

mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.

15Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha,

koma anatumiza nthenda yowondetsa.

16Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni,

amene Yehova anadzipatulira.

17Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani;

inakwirira gulu la Abiramu.

18Moto unayaka pakati pa otsatira awo;

lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.

19Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu

ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.

20Anasinthanitsa ulemerero wawo

ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.

21Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa,

amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,

22zozizwitsa mʼdziko la Hamu

ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.

23Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga,

pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa,

kuyima pamaso pake,

ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.

24Motero iwo ananyoza dziko lokoma;

sanakhulupirire malonjezo ake.

25Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo

ndipo sanamvere Yehova.

26Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake,

kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,

27kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina

ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.

28Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori

ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;

29anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa,

ndipo mliri unabuka pakati pawo.

30Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo,

ndipo mliri unaleka.

31Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake,

kwa mibado yosatha imene ikubwera.

32Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova

ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,

33pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu,

ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.

34Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu

monga momwe Yehova anawalamulira.

35Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo

ndi kuphunzira miyambo yawo.

36Ndipo anapembedza mafano awo,

amene anakhala msampha kwa iwowo.

37Anapereka nsembe ana awo aamuna

ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.

38Anakhetsa magazi a anthu osalakwa,

magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi,

amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani,

ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.

39Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita;

ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.

40Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake

ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.

41Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina,

ndipo adani awo anawalamulira.

42Adani awo anawazunza

ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.

43Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri,

koma iwo ankatsimikiza za kuwukira

ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.

44Koma Iye anaona kuzunzika kwawo

pamene anamva kulira kwawo;

45Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake

ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.

46Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo

awamvere chisoni.

47Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu,

ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina

kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera

ndi kunyadira mʼmatamando anu.

48Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli,

Kuyambira muyaya mpaka muyaya.

Anthu onse anene kuti, “Ameni!”

Tamandani Yehova.

Hoffnung für Alle

Psalm 106:1-48

Wir haben schwere Schuld auf uns geladen!

1Halleluja – lobt den Herrn!

Dankt dem Herrn, denn er ist gut,

und seine Gnade hört niemals auf!

2Wer könnte seine mächtigen Taten alle aufzählen?

Wer könnte ihn jemals genug loben?

3Glücklich sind alle, die sich an seine Ordnungen halten

und immer das tun, was in Gottes Augen recht ist!

4Herr, denke auch an mich, wenn du deinem Volk hilfst;

komm auch zu mir und rette mich!

5Lass mich mit eigenen Augen sehen,

wie du dein auserwähltes Volk beschenkst!

Ich will mich gemeinsam mit ihnen freuen

und mit denen jubeln, die zu dir gehören.

6Wir haben schwere Schuld auf uns geladen – wie schon unsere Vorfahren.

Wir haben Unrecht begangen und dich missachtet!

7Schon unsere Väter in Ägypten

wollten nicht aus deinen Wundern lernen.

Schnell vergaßen sie, wie oft du ihnen deine Liebe gezeigt hattest.

Am Ufer des Schilfmeers lehnten sie sich gegen dich auf.

8Trotzdem befreite sie der Herr, um seinem Namen Ehre zu machen

und ihnen seine große Macht zu beweisen.

9Er befahl dem Schilfmeer, sich zu teilen,

und schon türmten die Fluten sich auf.

Er führte sein Volk mitten hindurch, als wäre es trockenes Land.

10-11Das Wasser schlug über den Verfolgern zusammen,

und nicht einer kam mit dem Leben davon.

So rettete er sie aus der Gewalt ihrer Feinde,

unter deren Hass sie so lange gelitten hatten.

12Da endlich glaubten sie seinen Worten

und lobten ihn mit ihren Liedern.

13Doch schon bald vergaßen sie, was er für sie getan hatte.

Sie wollten nicht darauf warten, dass sein Plan sich erfüllte.

14In der Wüste forderten sie Gott heraus,

in ihrer Gier verlangten sie, Fleisch zu essen.

15Da gab er ihnen, wonach sie gierten,

doch hinterher schickte er eine schreckliche Seuche.

16Im Lager sah man voller Neid auf Mose

und auf Aaron, den heiligen Diener des Herrn.

17Da öffnete sich auf einmal die Erde und verschlang die Aufrührer:

Datan, Abiram und ihre Familien wurden in der Tiefe begraben.

18Dann brach ein Feuer aus unter denen, die zu ihnen hielten,

und verbrannte sie, weil sie Gott missachtet hatten.

19Am Berg Horeb goss sich das Volk Israel ein goldenes Kalb

und betete dieses Standbild an.

20Die Herrlichkeit ihres Gottes tauschten sie ein

gegen das Abbild eines Gras fressenden Stiers!

21Sie vergaßen Gott, ihren Retter,

der in Ägypten mächtige Taten vollbracht hatte.

22Sie dachten nicht mehr an seine Wunder,

an sein furchterregendes Handeln am Schilfmeer.

23Schon sprach Gott davon, sie alle zu vernichten,

doch Mose, sein Auserwählter, setzte sich für sie ein.

Er wandte Gottes Zorn von ihnen ab,

so dass sie nicht getötet wurden.

24Dann verschmähten sie das schöne Land,

denn sie glaubten Gottes Zusagen nicht.

25Sie blieben in ihren Zelten und schimpften über den Herrn;

seine Worte nahmen sie längst nicht mehr ernst.

26Da hob er seine Hand zum Schwur und sagte:

»Ich werde sie in der Wüste umkommen lassen

27und ihre Nachkommen unter die Völker zerstreuen,

damit sie dort in der Fremde untergehen!«

28Sie warfen sich Baal an den Hals, dem Gott vom Berg Peor,

und aßen das Fleisch von Opfertieren,

die man doch toten Götzen geweiht hatte.

29Ihr gottloses Treiben reizte den Herrn zum Zorn,

da brach eine schreckliche Seuche unter ihnen aus.

30Pinhas aber griff ein und hielt Gericht,

und die Seuche hörte auf zu wüten.

31So fand er Gottes Anerkennung –

er und seine Nachkommen für alle Zeit.

32Auch bei der Felsenquelle von Meriba

forderten die Israeliten Gottes Zorn heraus,

ihretwegen brach über Mose das Verhängnis herein:

33Sie hatten ihn so wütend gemacht,

dass er sich zu unbedachten Worten hinreißen ließ.

34Sie beachteten nicht den Befehl des Herrn,

die anderen Völker zu vernichten.

35Stattdessen vermischten sie sich mit ihnen

und übernahmen deren schreckliche Bräuche:

36Sie beteten die Götter der Kanaaniter an,

die ihnen schließlich zum Verhängnis wurden.

37Ihre eigenen Söhne und Töchter

opferten sie den Dämonen.

38Sie vergossen unschuldiges Blut

und entweihten das Land,

indem sie ihre Kinder

zu Ehren der Götzen Kanaans schlachteten.

39Durch ihre bösen Taten wurden sie unrein in Gottes Augen –

mit ihrem Treiben brachen sie ihm die Treue.

40Da geriet der Herr in Zorn über Israel

und verabscheute sein eigenes Volk.

41Er gab sie in die Hand fremder Völker;

sie wurden beherrscht von denen, die sie hassten.

42Ihre Feinde unterdrückten sie,

ihrer Gewalt musste Israel sich beugen.

43Immer wieder befreite sie der Herr,

aber sie dachten gar nicht daran, ihm zu gehorchen.

So sanken sie durch ihre Schuld immer tiefer ins Unglück.

44Doch als Gott ihre verzweifelte Lage sah

und ihre Hilfeschreie hörte,

45da dachte er an seinen Bund mit ihnen.

Ja, seine Liebe zu ihnen war stark, darum tat es ihm leid,

dass er sie ihren Feinden ausgeliefert hatte.

46Er ließ sie Erbarmen finden bei denen,

die sie gefangen hielten.

47Rette uns, Herr, unser Gott!

Hol uns heraus aus den Völkern, die dich nicht kennen,

und führe uns wieder zusammen!

Dann werden wir deinen heiligen Namen preisen

und dir voller Freude unseren Dank bringen.

48Gelobt sei der Herr, der Gott Israels,

jetzt und für alle Zeit!

Und das ganze Volk soll antworten: »Amen!

Lobt den Herrn. Halleluja!«