Masalimo 105 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 105:1-45

Salimo 105

1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.

2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;

fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.

3Munyadire dzina lake loyera;

mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.

4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

funafunani nkhope yake nthawi yonse.

5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,

zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,

6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.

8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,

mawu amene analamula kwa mibado yonse,

9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,

lumbiro limene analumbira kwa Isake.

10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,

kwa Israeli monga pangano lamuyaya:

11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani

ngati gawo la cholowa chako.”

12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,

ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,

13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,

kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.

14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;

anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:

15“Musakhudze odzozedwa anga;

musachitire choyipa aneneri anga.”

16Iye anabweretsa njala pa dziko

ndipo anawononga chakudya chonse;

17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,

Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.

18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,

khosi lake analiyika mʼzitsulo,

19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,

mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.

20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,

wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.

21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,

wolamulira zonse zimene iye anali nazo,

22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira

ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.

23Tsono Israeli analowa mu Igupto;

Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.

24Yehova anachulukitsa anthu ake;

ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;

25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,

kukonzera chiwembu atumiki ake.

26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,

ndi Aaroni amene Iye anamusankha.

27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,

zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.

28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.

Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.

29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,

kuchititsa kuti nsomba zawo zife.

30Dziko lawo linadzaza ndi achule

amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.

31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka

ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.

32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,

ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;

33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,

nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.

34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,

ziwala zosawerengeka;

35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,

zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.

36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,

zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.

37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,

ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.

38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,

pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.

39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,

ndi moto owawunikira usiku.

40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri

ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.

41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;

ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.

42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene

linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.

43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,

osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;

44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina

ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,

45kuti iwo asunge malangizo ake

ndi kutsatira malamulo ake.

Tamandani Yehova.

New Serbian Translation

Псалми 105:1-45

Псалам 105

1Хвалите Господа, призивајте му име,

објавите његова дела међу народима.

2Певајте му, славите га песмом,

говорите о свим његовим чудесима.

3Хвалите се светим именом његовим,

нек се радују срца оних који траже Господа.

4Тражите Господа и његову снагу,

тражите свагда лице његово.

5Памтите чудеса која је учинио,

чуда и судове уста његових.

6О, семе Аврахамово, слуго његов,

децо Јаковљева, изабраници његови!

7Он је Господ, Бог наш,

судови су његови по свој земљи.

8Он се сећа увек његовог савеза,

речи што је заповеди за хиљаду нараштаја,

9који је склопио са Аврахамом,

и којим се заклео Исаку,

10за уредбу га је поставио Јакову,

Израиљу за вечни савез,

11говорећи: „Теби ћу дати земљу хананску,

као део вашега наследства.“

12Док их је још било мало,

тек шачица дошљака у земљи,

13лутајући од народа до народа,

од једног царства до другог,

14није дао ником да их тлачи,

ради њих је кажњавао цареве:

15„Не дирајте моје помазанике,

мојим пророцима злобу не чините!“

16Он је глад призвао на земљу,

укинуо свако снабдевање хлебом.

17Човека је послао пред њима,

Јосифа, проданог у робље.

18Ноге су му спутали ланцима,

а врат су му оковали гвожђем;

19све до часа кад се испунила реч о њему,

реч Господња га је прокушала.

20Цар је заповедио да га пусте,

владар народа га је ослободио.

21Поставио га је за господара куће,

за управитеља свих својих добара;

22да по својој вољи води му главаре,

старешине му мудро саветује.

23Тако је Израиљ дошао у Египат;

Јаков, дошљак у Хамовој земљи.

24И он је веома умножио свој народ,

бројнији су били од својих душмана.

25Окренуо им је срце да замрзе његов народ,

да му се на слуге пакосно окоме.

26Послао је Мојсија, свог слугу,

и Арона, свог изабраника.

27И они су пред њима приказали његове знакове

и чудеса по Хамовој земљи.

28Спустио је таму на њу, помрачио је,

и они105,28 Према стиху 26, јасно је да се ради о Мојсију и Арону. нису били непослушни његовој речи.

29Воде им је у крв претворио

и рибе им поморио.

30Земља им је врвела од жаба,

чак и одаје њихових царева.

31Заповедио је, па су обади и комарци

навалили на све њихове крајеве.

32Град им је као кишу дао

и пламене муње по њиховој земљи.

33Лозе им је и смокве сломио,

скршио им стабла по њиховом крају.

34Заповедио је, па су грунули

безбројни скакавци и гусенице.

35Обрстили су све биље њихове земље,

појели им летину са поља.

36Побио је све првенце њихове земље,

први плод све њихове мужевности.

37Извео их је са сребром и златом,

међу његовим племенима није било посрнулих.

38Египат је одахнуо када су изашли,

јер их је од њих спопала страхота.

39Облак је као заклон разастро

и пламен да ноћу светли.

40Молили су га и он им доведе препелице,

хлебом с неба их насити.

41Отворио је стену и воде прокуљаше,

потекле су као поток у земљи сувој.

42Јер се сетио свог светог обећања Аврахаму,

слузи своме.

43Извео је свој народ у радости,

уз клицање своје изабране.

44Дао им је земље туђинске,

запосели су труд народа;

45да би се држали његових прописа

и законе његове слушали.

Славите Господа!