Masalimo 104 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 104:1-35

Salimo 104

1Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri;

mwavala ulemerero ndi ufumu.

2Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala;

watambasula miyamba ngati tenti

3ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake.

Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake,

ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.

4Amapanga mphepo kukhala amithenga ake,

malawi amoto kukhala atumiki ake.

5Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake;

silingasunthike.

6Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala;

madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.

7Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa,

pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;

8Inu munamiza mapiri,

iwo anatsikira ku zigwa

kumalo kumene munawakonzera.

9Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa,

iwo sadzamizanso dziko lapansi.

10Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa;

madziwo amayenda pakati pa mapiri.

11Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo;

abulu akuthengo amapha ludzu lawo.

12Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi;

zimayimba pakati pa thambo.

13Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba;

dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.

14Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye,

ndi zomera, kuti munthu azilima

kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:

15vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu,

mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala,

ndi buledi amene amapereka mphamvu.

16Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino,

mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.

17Mbalame zimamanga zisa zawo;

kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.

18Mapiri ataliatali ndi a mbalale;

mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.

19Mwezi umasiyanitsa nyengo

ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.

20Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku,

ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.

21Mikango imabangula kufuna nyama,

ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.

22Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala;

imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.

23Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake,

kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.

24Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova!

Munazipanga zonse mwanzeru,

dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

25Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala,

yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka,

zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.

26Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku,

ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.

27Zonsezi zimayangʼana kwa Inu

kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.

28Mukazipatsa,

zimachisonkhanitsa pamodzi;

mukatsekula dzanja lanu,

izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.

29Mukabisa nkhope yanu,

izo zimachita mantha aakulu;

mukachotsa mpweya wawo,

zimafa ndi kubwerera ku fumbi.

30Mukatumiza mzimu wanu,

izo zimalengedwa

ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.

31Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya;

Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;

32Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera,

amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.

33Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse;

ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.

34Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye,

pamene ndikusangalala mwa Yehova.

35Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi

ndipo anthu oyipa asapezekenso.

Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga.

Tamandani Yehova.

Hoffnung für Alle

Psalm 104:1-35

Freude an Gottes Schöpfung

1Ich will den Herrn preisen von ganzem Herzen.

Herr, mein Gott, wie groß bist du!

Majestätische Pracht ist dein Festgewand,

2helles Licht umhüllt dich wie ein Mantel.

Du spanntest den Himmel aus wie ein Zeltdach,

3über den Wolken104,3 Wörtlich: in den Wassern. – Vgl. 1. Mose 1,6‒8. hast du deine Wohnung errichtet.

Ja, die Wolken sind dein Wagen,

du fährst auf den Flügeln des Windes dahin.

4Wind und Wetter sind deine Boten,

und feurige Flammen sind deine Diener.

5Die Erde stelltest du auf ein festes Fundament,

niemals gerät sie ins Wanken.

6Wie ein Kleid bedeckte die Urflut ihre Kontinente,

die Wassermassen standen noch über den Bergen.

7Doch vor deinem lauten Ruf wichen sie zurück,

vor deinem Donnergrollen flohen sie.

8Die Berge erhoben sich,

und die Täler senkten sich an den Ort,

den du für sie bestimmt hattest.

9Du hast dem Wasser eine Grenze gesetzt,

die es nicht überschreiten darf,

nie wieder soll es die ganze Erde überschwemmen.

10Du lässt Quellen sprudeln und als Bäche in die Täler fließen,

zwischen den Bergen finden sie ihren Weg.

11Die Tiere der Steppe trinken davon,

Wildesel stillen ihren Durst.

12An ihren Ufern nisten die Vögel,

in dichtem Laub singen sie ihre Lieder.

13Vom Himmel lässt du Regen auf die Berge niedergehen,

die Erde versorgst du und schenkst reiche Frucht.

14Du lässt Gras wachsen für das Vieh

und Pflanzen, die der Mensch anbauen und ernten kann.

15So hat er Wein, der ihn erfreut,

Öl, das seinen Körper pflegt, und Brot, das ihn stärkt.

16Du, Herr, hast die riesigen Zedern

auf dem Libanongebirge gepflanzt und gibst ihnen genügend Regen.

17In ihren Zweigen bauen die Vögel ihre Nester,

und Störche haben in den Zypressen ihren Brutplatz.

18In den hohen Bergen hat der Steinbock sein Revier,

und das Murmeltier104,18 Wörtlich: der Klippdachs. – Der Klippdachs war ein murmeltierähnlicher Pflanzenfresser von gelb-brauner Farbe. Vgl. 3. Mose 11,5; 5. Mose 14,7. findet in den Felsen Zuflucht.

19Du hast den Mond gemacht, um die Monate zu bestimmen,

und die Sonne weiß, wann sie untergehen soll.

20Du lässt die Dunkelheit hereinbrechen, und es wird Nacht –

dann regen sich die Tiere im Dickicht des Waldes.

21Die jungen Löwen brüllen nach Beute;

von dir, o Gott, erwarten sie ihre Nahrung.

22Sobald aber die Sonne aufgeht,

schleichen sie zurück in ihre Schlupfwinkel

und legen sich dort nieder.

23Dann steht der Mensch auf und geht an seine Arbeit,

er hat zu tun, bis es wieder Abend wird.

24O Herr, welch unermessliche Vielfalt zeigen deine Werke!

Sie alle sind Zeugen deiner Weisheit,

die ganze Erde ist voll von deinen Geschöpfen.

25Da ist das Meer – so unendlich groß und weit,

unzählbar sind die Tiere darin, große wie kleine.

26Schiffe ziehen dort vorüber und auch die Seeungeheuer,

die du geschaffen hast, um mit ihnen zu spielen.

27Alle deine Geschöpfe warten auf dich,

dass du ihnen zur rechten Zeit zu essen gibst.

28Sie holen sich die Nahrung, die du ihnen zuteilst.

Du öffnest deine Hand, und sie werden reichlich satt.

29Doch wenn du dich von ihnen abwendest,

müssen sie zu Tode erschrecken.

Ja, sie sterben und werden zu Staub,

wenn du ihnen den Lebensatem nimmst.

30Doch wenn du deinen Geist schickst, wird neues Leben geschaffen,

und die Erde kann sich wieder entfalten.

31Die Herrlichkeit des Herrn möge ewig bestehen!

Er freue sich an dem, was er geschaffen hat!

32Er braucht die Erde nur anzusehen – schon fängt sie an zu beben;

und wenn er die Berge berührt, dann stoßen sie Rauch aus.

33Singen will ich für den Herrn, solange ich bin,

für meinen Gott will ich musizieren mein Leben lang.

34Wie freue ich mich über den Herrn

möge ihm mein Lied gefallen!

35Doch wer sich ihm widersetzt, soll nicht mehr weiterleben,

ja, die Gottlosen sollen vom Erdboden verschwinden.

Ich will den Herrn preisen von ganzem Herzen.

Halleluja – lobt den Herrn!