Salimo 102
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko.
1Yehova imvani pemphero langa;
kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2Musandibisire nkhope yanu
pamene ndili pa msautso.
Munditcherere khutu;
pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3Pakuti masiku anga akupita ngati utsi;
mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu;
ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula
ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu,
monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7Ndimagona osapeza tulo; ndakhala
ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe;
iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa
ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10chifukwa cha ukali wanu waukulu,
popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo;
Ine ndikufota ngati udzu.
12Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya;
kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni
pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo;
nthawi yoyikika yafika.
14Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu;
fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova,
mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni
ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17Iye adzayankha pemphero la anthu otayika;
sadzanyoza kupempha kwawo.
18Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo,
kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba,
kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende,
kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni
ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22pamene mitundu ya anthu ndi maufumu
adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga;
Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24Choncho Ine ndinati:
“Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga;
zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi
ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo;
zidzatha ngati chovala.
Mudzazisintha ngati chovala
ndipo zidzatayidwa.
27Koma Inu simusintha,
ndipo zaka zanu sizidzatha.
28Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu;
zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
Psalm 102In Hebrew texts 102:1-28 is numbered 102:2-29.
A prayer of an afflicted person who has grown weak and pours out a lament before the Lord.
1Hear my prayer, Lord;
let my cry for help come to you.
2Do not hide your face from me
when I am in distress.
Turn your ear to me;
when I call, answer me quickly.
3For my days vanish like smoke;
my bones burn like glowing embers.
4My heart is blighted and withered like grass;
I forget to eat my food.
5In my distress I groan aloud
and am reduced to skin and bones.
6I am like a desert owl,
like an owl among the ruins.
7I lie awake; I have become
like a bird alone on a roof.
8All day long my enemies taunt me;
those who rail against me use my name as a curse.
9For I eat ashes as my food
and mingle my drink with tears
10because of your great wrath,
for you have taken me up and thrown me aside.
11My days are like the evening shadow;
I wither away like grass.
12But you, Lord, sit enthroned for ever;
your renown endures through all generations.
13You will arise and have compassion on Zion,
for it is time to show favour to her;
the appointed time has come.
14For her stones are dear to your servants;
her very dust moves them to pity.
15The nations will fear the name of the Lord,
all the kings of the earth will revere your glory.
16For the Lord will rebuild Zion
and appear in his glory.
17He will respond to the prayer of the destitute;
he will not despise their plea.
18Let this be written for a future generation,
that a people not yet created may praise the Lord:
19‘The Lord looked down from his sanctuary on high,
from heaven he viewed the earth,
20to hear the groans of the prisoners
and release those condemned to death.’
21So the name of the Lord will be declared in Zion
and his praise in Jerusalem
22when the peoples and the kingdoms
assemble to worship the Lord.
23In the course of my life102:23 Or By his power he broke my strength;
he cut short my days.
24So I said:
‘Do not take me away, my God, in the midst of my days;
your years go on through all generations.
25In the beginning you laid the foundations of the earth,
and the heavens are the work of your hands.
26They will perish, but you remain;
they will all wear out like a garment.
Like clothing you will change them
and they will be discarded.
27But you remain the same,
and your years will never end.
28The children of your servants will live in your presence;
their descendants will be established before you.’