Salimo 101
Salimo la Davide.
1Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama;
kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.
2Ndidzatsata njira yolungama;
nanga mudzabwera liti kwa ine?
Ndidzayenda mʼnyumba mwanga
ndi mtima wosalakwa.
3Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa
pamaso panga.
Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro;
iwo sadzadziphatika kwa ine.
4Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine;
ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.
5Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri
ameneyo ndidzamuletsa;
aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza,
ameneyo sindidzamulekerera.
6Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko,
kuti akhale pamodzi ndi ine;
iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa
adzanditumikira.
7Aliyense wochita chinyengo
sadzakhala mʼnyumba mwanga.
Aliyense woyankhula mwachinyengo
sadzayima pamaso panga.
8Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu
onse oyipa mʼdziko;
ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa
mu mzinda wa Yehova.
Engagement à lutter contre le mal
1Psaume de David.
Je veux chanter l’amour ╵et la justice,
je te célébrerai ╵par la musique, ╵ô Eternel.
2Je ferai attention ╵de suivre le chemin ╵des gens intègres.
Quand viendras-tu vers moi ?
Je veux marcher ╵avec un cœur intègre
dans ma maison,
3je ne mettrai ╵rien de mauvais ╵devant mes yeux.
Je hais l’acte tordu,
il n’aura sur moi pas de prise.
4Le cœur corrompu restera ╵bien loin de moi,
je ne veux pas ╵être impliqué avec le mal.
5Celui qui calomnie ╵son prochain en secret,
je le réduirai au silence.
Je ne supporte pas
les yeux hautains ╵ni le cœur arrogant.
6Mes yeux se porteront ╵sur les fidèles du pays,
je les ferai siéger auprès de moi.
Et ceux qui suivent le chemin ╵des gens intègres
seront à mon service.
7Il n’y a pas de place ╵dans ma maison
pour qui pratique ╵la tromperie,
et le menteur ╵ne subsistera pas ╵en ma présence.
8Tous les matins101.8 La justice se rendait le matin à la porte de la ville (2 S 15.2 ; Jr 21.12). ╵je fermerai la bouche ╵aux méchants du pays,
pour retrancher ╵de la cité de l’Eternel,
tous ceux qui font le mal.