Masalimo 100 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 100:1-5

Salimo 100

Salimo. Nyimbo yothokoza.

1Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.

2Mulambireni Yehova mosangalala;

bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.

3Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.

Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;

ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.

4Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko

ndi ku mabwalo ake ndi matamando;

muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.

5Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;

kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.

New International Version – UK

Psalms 100:1-5

Psalm 100

A psalm. For giving grateful praise.

1Shout for joy to the Lord, all the earth.

2Worship the Lord with gladness;

come before him with joyful songs.

3Know that the Lord is God.

It is he who made us, and we are his100:3 Or and not we ourselves;

we are his people, the sheep of his pasture.

4Enter his gates with thanksgiving

and his courts with praise;

give thanks to him and praise his name.

5For the Lord is good and his love endures for ever;

his faithfulness continues through all generations.