Salimo 100
Salimo. Nyimbo yothokoza.
1Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
2Mulambireni Yehova mosangalala;
bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
3Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.
Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;
ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
4Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko
ndi ku mabwalo ake ndi matamando;
muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
5Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;
kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
Psalm 100
A psalm. For giving grateful praise.
1Shout for joy to the Lord, all the earth.
2Worship the Lord with gladness;
come before him with joyful songs.
3Know that the Lord is God.
It is he who made us, and we are his100:3 Or and not we ourselves;
we are his people, the sheep of his pasture.
4Enter his gates with thanksgiving
and his courts with praise;
give thanks to him and praise his name.
5For the Lord is good and his love endures for ever;
his faithfulness continues through all generations.