Masalimo 100 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 100:1-5

Salimo 100

Salimo. Nyimbo yothokoza.

1Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.

2Mulambireni Yehova mosangalala;

bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.

3Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.

Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;

ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.

4Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko

ndi ku mabwalo ake ndi matamando;

muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.

5Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;

kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.

New International Reader’s Version

Psalm 100:1-5

Psalm 100

A psalm for giving grateful praise.

1Shout for joy to the Lord, everyone on earth.

2Worship the Lord with gladness.

Come to him with songs of joy.

3Know that the Lord is God.

He made us, and we belong to him.

We are his people.

We are the sheep belonging to his flock.

4Give thanks as you enter the gates of his temple.

Give praise as you enter its courtyards.

Give thanks to him and praise his name.

5The Lord is good. His faithful love continues forever.

It will last for all time to come.