Masalimo 1 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 1:1-6

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Salimo 1

1Wodala munthu

amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,

kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,

kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.

2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova

ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.

3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake

ndipo masamba ake safota.

Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.

4Sizitero ndi anthu oyipa!

Iwo ali ngati mungu

umene umawuluzidwa ndi mphepo.

5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,

kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,

koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 1:1-6

LIBRO I

Salmos 1–41

Salmo 1

1Dichoso el hombre

que no sigue el consejo de los malvados,

ni se detiene en la senda de los pecadores

ni cultiva la amistad de los blasfemos,

2sino que en la ley del Señor se deleita,

y día y noche medita en ella.

3Es como el árbol

plantado a la orilla de un río

que, cuando llega su tiempo, da fruto

y sus hojas jamás se marchitan.

¡Todo cuanto hace prospera!

4En cambio, los malvados

son como paja arrastrada por el viento.

5Por eso no se sostendrán los malvados en el juicio,

ni los pecadores en la asamblea de los justos.

6Porque el Señor cuida el camino de los justos,

mas la senda de los malos lleva a la perdición.