Marko 9 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 9:1-50

1Ndipo anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ena amene ayimirira pano sadzafa asanaone ufumu wa Mulungu ukubwera mwa mphamvu.”

Maonekedwe a Ulemerero wa Yesu pa Phiri

2Patatha masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane nawatsogolera kupita ku phiri lalitali, kumene anali okhaokha. Kumeneko maonekedwe ake anasinthika pamaso pawo. 3Zovala zake zinawala monyezimira kwambiri, kotero kuti palibe sopo wina aliyense amene angaziyeretse monyezimira chotere pa dziko la pansi. 4Ndipo anaonekera Eliya ndi Mose pamaso pawo, amene ankayankhulana ndi Yesu.

5Petro anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, ndi kwabwino kuti ife tili pano. Tiyeni timange misasa itatu; umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.” 6(Iye sanadziwe choti anene, anali ndi mantha akulu).

7Pamenepo mtambo unaoneka ndi kuwaphimba, ndipo mawu anamveka kuchokera mu mtambo kuti, “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa. Mvereni Iye!”

8Mwadzidzidzi, atayangʼanayangʼana, sanaonenso wina aliyense ali ndi iwo kupatula Yesu.

9Pamene ankatsika kuchokera ku phiri, Yesu anawalamulira kuti asawuze aliyense zimene anaona mpaka Mwana wa Munthu atauka kwa akufa. 10Iwo anayisunga nkhaniyo nakambirana za tanthauzo lake la “Kuuka kwa akufa.”

11Ndipo anamufunsa Iye kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kuyamba wabwera?”

12Yesu anayankha kuti, “Kunena motsimikiza, Eliya ayeneradi kuyamba kubwera kudzakonzanso zinthu zonse. Nʼchifukwa chiyani tsono zinalembedwa, kuti Mwana wa Munthu ayenera kuvutika kwambiri ndi kukanidwa? 13Koma ndikuwuzani, kuti Eliya wabweradi, ndipo amuchitira iye zonse zimene iwo anafuna, monga momwe zalembedwera za iye.”

Kuchiritsidwa kwa Mnyamata Wogwidwa ndi Mzimu Woyipa

14Atafika kwa ophunzira ena aja, anaona gulu lalikulu la anthu litawazungulira ndi aphunzitsi amalamulo akutsutsana nawo. 15Nthawi yomweyo anthu onse atamuona, anadabwa kwambiri ndipo anathamanga kukamulonjera.

16Iye anafunsa kuti, “Mukukangana nawo chiyani iwowa?”

17Munthu wina mʼgululo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndinakubweretserani mwana wanga wamwamuna, amene ndi ogwidwa ndi mzimu umene umamulepheretsa kuyankhula. 18Nthawi iliyonse ukamugwira umamugwetsa pansi. Amatuluka thovu kukamwa, amakukuta mano ake ndipo amawuma. Ndinapempha ophunzira anu kuti awutulutse mzimuwo, koma sanathe.”

19Yesu anayankha kuti, “Haa! Mʼbado osakhulupirira, kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Mubweretseni kwa Ine mnyamatayo.”

20Ndipo anamubweretsa kwa Iye. Mzimu woyipawo utaona Yesu, nthawi yomweyo unamukomola mnyamatayo. Anagwa pansi ndi kumagubuduka, ndi kuchita thovu kukamwa.

21Yesu anafunsa abambo a mnyamatayo kuti, “Kodi wakhala chotere nthawi yayitali bwanji?”

Iye anayankha kuti, “Kuyambira ali wamngʼono, 22wakhala ukumuponya pa moto kapena mʼmadzi kuti umuphe. Koma ngati mungathe kuchita kanthu, tichitireni chifundo ndipo mutithandize.”

23Yesu anati, “ ‘Ngati mungathe!’ Zinthu zonse ndi zotheka kwa iye amene akhulupirira.”

24Nthawi yomweyo abambo a mwanayo anafuwula kuti, “Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga!”

25Yesu ataona kuti gulu la anthu likuthamangira kumalowo, anadzudzula mzimu woyipawo kuti, “Iwe mzimu wolepheretsa kuyankhula ndi kumva, ndikulamulira tuluka mwa iye ndipo usadzalowenso.”

26Mzimuwo unafuwula ndi kumugubuduza kwambiri ndipo unatuluka. Mnyamatayo anaoneka ngati mtembo ndipo ambiri anati, “Wafa.” 27Koma Yesu anamugwira dzanja ndipo anamuyimiritsa, ndipo anayimirira.

28Yesu atalowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa ali pa okha kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani ife sitinathe kutulutsa chiwandacho?”

29Iye anayankha kuti, “Mtundu uwu umatuluka pokhapokha mwapemphera ndi kusala kudya.”

Yesu aneneratu za Imfa yake Kachiwiri

30Anachoka malo amenewo nadutsa ku Galileya. Yesu sanafune kuti wina aliyense adziwe kumene anali, 31chifukwa amaphunzitsa ophunzira ake. Anati kwa iwo, “Mwana wa Munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu. Adzamupha, ndipo patatha masiku atatu adzauka.” 32Koma sanazindikire chimene amatanthauza, ndipo anachita mantha kuti amufunse.

Wamkulu Ndani mu Ufumu wa Mulungu?

33Anafika ku Kaperenawo. Pamene anali mʼnyumba, anawafunsa kuti, “Kodi mumatsutsana chiyani mʼnjira muja?” 34Koma anakhala chete chifukwa ali mʼnjira amatsutsana za kuti wamkulu kuposa onse ndani.

35Atakhala pansi, Yesu anayitana khumi ndi awiriwo nati, “Ngati wina aliyense afuna kukhala woyamba, ayenera kukhala wotsiriza ndi wotumikira onse.”

36Anatenga kamwana nakayimiritsa pakati pawo ndipo anawawuza kuti, 37“Aliyense wolandira mmodzi wa ana angʼono awa mʼdzina langa alandira Ine; ndipo aliyense wolandira Ine salandira Ine koma amene anandituma.”

Wosatsutsana Nafe Athandizana Nafe

38Yohane anati, “Aphunzitsi, tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo ife tinamuwuza kuti aleke, chifukwa sanali mmodzi wa ife.”

39Yesu anati, “Musamuletse, palibe amene amachita chodabwitsa mʼdzina langa ndipo kenaka nanena zoyipa za Ine, 40pakuti aliyense amene satsutsana nafe ali mbali yathu. 41Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene akupatsani chikho cha madzi mʼdzina langa chifukwa ndinu ake a Khristu, sadzataya konse mphotho yake.”

Zochimwitsa Ena

42“Ndipo ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana angʼono awa amene akhulupirira Ine, kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala waukulu mʼkhosi mwake. 43Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. 44(Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima). 45Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. 46(Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima). 47Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, 48kumene

“ ‘mphutsi zake sizifa

ndipo moto wake suzima.’

49Aliyense adzayesedwa ndi moto.

50“Mchere ndi wabwino, koma ngati utasukuluka, mungawukoleretsenso bwanji? Mukhale nawo mchere mwa inu nokha, ndipo mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.”

New International Reader’s Version

Mark 9:1-50

1Jesus said to them, “What I’m about to tell you is true. Some who are standing here will not die before they see that God’s kingdom has come with power.”

Jesus’ Appearance Is Changed

2After six days Jesus took Peter, James and John with him. He led them up a high mountain. They were all alone. There in front of them his appearance was changed. 3His clothes became so white they shone. They were whiter than anyone in the world could bleach them. 4Elijah and Moses appeared in front of Jesus and his disciples. The two of them were talking with Jesus.

5Peter said to Jesus, “Rabbi, it is good for us to be here. Let us put up three shelters. One will be for you, one for Moses, and one for Elijah.” 6Peter didn’t really know what to say, because they were so afraid.

7Then a cloud appeared and covered them. A voice came from the cloud. It said, “This is my Son, and I love him. Listen to him!”

8They looked around. Suddenly they no longer saw anyone with them except Jesus.

9They came down the mountain. On the way down, Jesus ordered them not to tell anyone what they had seen. He told them to wait until the Son of Man had risen from the dead. 10So they kept the matter to themselves. But they asked each other what “rising from the dead” meant.

11Then they asked Jesus, “Why do the teachers of the law say that Elijah has to come first?”

12Jesus replied, “That’s right. Elijah does come first. He makes all things new again. So why is it written that the Son of Man must suffer much and not be accepted? 13I tell you, Elijah has come. They have done to him everything they wanted to do. They did it just as it is written about him.”

Jesus Heals a Boy Who Is Controlled by an Evil Spirit

14When Jesus and those who were with him came to the other disciples, they saw a large crowd around them. The teachers of the law were arguing with them. 15When all the people saw Jesus, they were filled with wonder. And they ran to greet him.

16“What are you arguing with them about?” Jesus asked.

17A man in the crowd answered. “Teacher,” he said, “I brought you my son. He is controlled by an evil spirit. Because of this, my son can’t speak anymore. 18When the spirit takes hold of him, it throws him to the ground. He foams at the mouth. He grinds his teeth. And his body becomes stiff. I asked your disciples to drive out the spirit. But they couldn’t do it.”

19“You unbelieving people!” Jesus replied. “How long do I have to stay with you? How long do I have to put up with you? Bring the boy to me.”

20So they brought him. As soon as the spirit saw Jesus, it threw the boy into a fit. He fell to the ground. He rolled around and foamed at the mouth.

21Jesus asked the boy’s father, “How long has he been like this?”

“Since he was a child,” he answered. 22“The spirit has often thrown him into fire or water to kill him. But if you can do anything, take pity on us. Please help us.”

23“ ‘If you can’?” said Jesus. “Everything is possible for the one who believes.”

24Right away the boy’s father cried out, “I do believe! Help me overcome my unbelief!”

25Jesus saw that a crowd was running over to see what was happening. Then he ordered the evil spirit to leave the boy. “You spirit that makes him unable to hear and speak!” he said. “I command you, come out of him. Never enter him again.”

26The spirit screamed. It shook the boy wildly. Then it came out of him. The boy looked so lifeless that many people said, “He’s dead.” 27But Jesus took him by the hand. He lifted the boy to his feet, and the boy stood up.

28Jesus went indoors. Then his disciples asked him in private, “Why couldn’t we drive out the evil spirit?”

29He replied, “This kind can come out only by prayer.”

Jesus Speaks a Second Time About His Coming Death

30They left that place and passed through Galilee. Jesus did not want anyone to know where they were. 31That was because he was teaching his disciples. He said to them, “The Son of Man is going to be handed over to men. They will kill him. After three days he will rise from the dead.” 32But they didn’t understand what he meant. And they were afraid to ask him about it.

Who Is the Most Important Person?

33Jesus and his disciples came to a house in Capernaum. There he asked them, “What were you arguing about on the road?” 34But they kept quiet. On the way, they had argued about which one of them was the most important person.

35Jesus sat down and called for the 12 disciples to come to him. Then he said, “Anyone who wants to be first must be the very last. They must be the servant of everyone.”

36Jesus took a little child and had the child stand among them. Then he took the child in his arms. He said to them, 37“Anyone who welcomes one of these little children in my name welcomes me. And anyone who welcomes me also welcomes the one who sent me.”

Anyone Who Is Not Against Us Is for Us

38“Teacher,” said John, “we saw someone driving out demons in your name. We told him to stop, because he was not one of us.”

39“Do not stop him,” Jesus said. “For no one who does a miracle in my name can in the next moment say anything bad about me. 40Anyone who is not against us is for us. 41What I’m about to tell you is true. Suppose someone gives you a cup of water in my name because you belong to the Messiah. That person will certainly not go without a reward.

Leading People to Sin

42“What if someone leads one of these little ones who believe in me to sin? If they do, it would be better if a large millstone were hung around their neck and they were thrown into the sea. 43-44If your hand causes you to sin, cut it off. It would be better for you to enter God’s kingdom with only one hand than to go into hell with two hands. In hell the fire never goes out. 45-46If your foot causes you to sin, cut it off. It would be better to enter God’s kingdom with only one foot than to have two feet and be thrown into hell. 47If your eye causes you to sin, poke it out. It would be better for you to enter God’s kingdom with only one eye than to have two eyes and be thrown into hell. 48In hell,

“ ‘The worms that eat them do not die.

The fire is not put out.’ (Isaiah 66:24)

49Everyone will be salted with fire.

50“Salt is good. But suppose it loses its saltiness. How can you make it salty again? Have salt among yourselves. And be at peace with each other.”