Marko 9 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 9:1-50

1Ndipo anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ena amene ayimirira pano sadzafa asanaone ufumu wa Mulungu ukubwera mwa mphamvu.”

Maonekedwe a Ulemerero wa Yesu pa Phiri

2Patatha masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane nawatsogolera kupita ku phiri lalitali, kumene anali okhaokha. Kumeneko maonekedwe ake anasinthika pamaso pawo. 3Zovala zake zinawala monyezimira kwambiri, kotero kuti palibe sopo wina aliyense amene angaziyeretse monyezimira chotere pa dziko la pansi. 4Ndipo anaonekera Eliya ndi Mose pamaso pawo, amene ankayankhulana ndi Yesu.

5Petro anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, ndi kwabwino kuti ife tili pano. Tiyeni timange misasa itatu; umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.” 6(Iye sanadziwe choti anene, anali ndi mantha akulu).

7Pamenepo mtambo unaoneka ndi kuwaphimba, ndipo mawu anamveka kuchokera mu mtambo kuti, “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa. Mvereni Iye!”

8Mwadzidzidzi, atayangʼanayangʼana, sanaonenso wina aliyense ali ndi iwo kupatula Yesu.

9Pamene ankatsika kuchokera ku phiri, Yesu anawalamulira kuti asawuze aliyense zimene anaona mpaka Mwana wa Munthu atauka kwa akufa. 10Iwo anayisunga nkhaniyo nakambirana za tanthauzo lake la “Kuuka kwa akufa.”

11Ndipo anamufunsa Iye kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kuyamba wabwera?”

12Yesu anayankha kuti, “Kunena motsimikiza, Eliya ayeneradi kuyamba kubwera kudzakonzanso zinthu zonse. Nʼchifukwa chiyani tsono zinalembedwa, kuti Mwana wa Munthu ayenera kuvutika kwambiri ndi kukanidwa? 13Koma ndikuwuzani, kuti Eliya wabweradi, ndipo amuchitira iye zonse zimene iwo anafuna, monga momwe zalembedwera za iye.”

Kuchiritsidwa kwa Mnyamata Wogwidwa ndi Mzimu Woyipa

14Atafika kwa ophunzira ena aja, anaona gulu lalikulu la anthu litawazungulira ndi aphunzitsi amalamulo akutsutsana nawo. 15Nthawi yomweyo anthu onse atamuona, anadabwa kwambiri ndipo anathamanga kukamulonjera.

16Iye anafunsa kuti, “Mukukangana nawo chiyani iwowa?”

17Munthu wina mʼgululo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndinakubweretserani mwana wanga wamwamuna, amene ndi ogwidwa ndi mzimu umene umamulepheretsa kuyankhula. 18Nthawi iliyonse ukamugwira umamugwetsa pansi. Amatuluka thovu kukamwa, amakukuta mano ake ndipo amawuma. Ndinapempha ophunzira anu kuti awutulutse mzimuwo, koma sanathe.”

19Yesu anayankha kuti, “Haa! Mʼbado osakhulupirira, kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Mubweretseni kwa Ine mnyamatayo.”

20Ndipo anamubweretsa kwa Iye. Mzimu woyipawo utaona Yesu, nthawi yomweyo unamukomola mnyamatayo. Anagwa pansi ndi kumagubuduka, ndi kuchita thovu kukamwa.

21Yesu anafunsa abambo a mnyamatayo kuti, “Kodi wakhala chotere nthawi yayitali bwanji?”

Iye anayankha kuti, “Kuyambira ali wamngʼono, 22wakhala ukumuponya pa moto kapena mʼmadzi kuti umuphe. Koma ngati mungathe kuchita kanthu, tichitireni chifundo ndipo mutithandize.”

23Yesu anati, “ ‘Ngati mungathe!’ Zinthu zonse ndi zotheka kwa iye amene akhulupirira.”

24Nthawi yomweyo abambo a mwanayo anafuwula kuti, “Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga!”

25Yesu ataona kuti gulu la anthu likuthamangira kumalowo, anadzudzula mzimu woyipawo kuti, “Iwe mzimu wolepheretsa kuyankhula ndi kumva, ndikulamulira tuluka mwa iye ndipo usadzalowenso.”

26Mzimuwo unafuwula ndi kumugubuduza kwambiri ndipo unatuluka. Mnyamatayo anaoneka ngati mtembo ndipo ambiri anati, “Wafa.” 27Koma Yesu anamugwira dzanja ndipo anamuyimiritsa, ndipo anayimirira.

28Yesu atalowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa ali pa okha kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani ife sitinathe kutulutsa chiwandacho?”

29Iye anayankha kuti, “Mtundu uwu umatuluka pokhapokha mwapemphera ndi kusala kudya.”

Yesu aneneratu za Imfa yake Kachiwiri

30Anachoka malo amenewo nadutsa ku Galileya. Yesu sanafune kuti wina aliyense adziwe kumene anali, 31chifukwa amaphunzitsa ophunzira ake. Anati kwa iwo, “Mwana wa Munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu. Adzamupha, ndipo patatha masiku atatu adzauka.” 32Koma sanazindikire chimene amatanthauza, ndipo anachita mantha kuti amufunse.

Wamkulu Ndani mu Ufumu wa Mulungu?

33Anafika ku Kaperenawo. Pamene anali mʼnyumba, anawafunsa kuti, “Kodi mumatsutsana chiyani mʼnjira muja?” 34Koma anakhala chete chifukwa ali mʼnjira amatsutsana za kuti wamkulu kuposa onse ndani.

35Atakhala pansi, Yesu anayitana khumi ndi awiriwo nati, “Ngati wina aliyense afuna kukhala woyamba, ayenera kukhala wotsiriza ndi wotumikira onse.”

36Anatenga kamwana nakayimiritsa pakati pawo ndipo anawawuza kuti, 37“Aliyense wolandira mmodzi wa ana angʼono awa mʼdzina langa alandira Ine; ndipo aliyense wolandira Ine salandira Ine koma amene anandituma.”

Wosatsutsana Nafe Athandizana Nafe

38Yohane anati, “Aphunzitsi, tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo ife tinamuwuza kuti aleke, chifukwa sanali mmodzi wa ife.”

39Yesu anati, “Musamuletse, palibe amene amachita chodabwitsa mʼdzina langa ndipo kenaka nanena zoyipa za Ine, 40pakuti aliyense amene satsutsana nafe ali mbali yathu. 41Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene akupatsani chikho cha madzi mʼdzina langa chifukwa ndinu ake a Khristu, sadzataya konse mphotho yake.”

Zochimwitsa Ena

42“Ndipo ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana angʼono awa amene akhulupirira Ine, kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala waukulu mʼkhosi mwake. 43Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. 44(Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima). 45Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. 46(Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima). 47Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, 48kumene

“ ‘mphutsi zake sizifa

ndipo moto wake suzima.’

49Aliyense adzayesedwa ndi moto.

50“Mchere ndi wabwino, koma ngati utasukuluka, mungawukoleretsenso bwanji? Mukhale nawo mchere mwa inu nokha, ndipo mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Марк 9:1-50

1Иса сказал им:

– Говорю вам истину: некоторые из вас, стоящих здесь, не умрут, пока не увидят, что Царство Аллаха проявило себя в силе9:1 Многие толкователи считают, что объяснением этих слов Исы служат следующие семь стихов (см. также Ин. 1:14; 2 Пет. 1:16). Другие думают, что Иса говорил о могущественном воздействии и росте Своего Царства, увеличении количества Его последователей и распространении Радостной Вести после Его воскресения. Существуют и другие толкования..

Преображение Исы аль-Масиха

(Мат. 17:1-13; Лк. 9:28-36)

2Через шесть дней Иса взял с Собой Петира, Якуба и Иохана и привёл их на высокую гору. Они были там совсем одни. И на глазах учеников Его облик изменился. 3Его одежда стала сияющей, ослепительно белой, как ни один белильщик в мире не смог бы отбелить. 4Затем они увидели пророков Ильяса и Мусу, беседующих с Исой. 5Петир сказал Исе:

– Учитель, нам здесь так хорошо! Давай мы сделаем три шалаша: один Тебе, один Мусе и один Ильясу, – 6он и сам не знал, что сказать, потому что они были сильно испуганы. 7Тут появилось облако и накрыло их, и из облака прозвучал голос:

– Это Мой любимый Сын (аль-Масих), слушайте Его!9:7 См. Нач. 22:2; Втор. 18:15; Заб. 2:7. В Исе мы видим исполнение всех этих пророчеств: Он и жертвенный ягнёнок, и обещанный Мусой Пророк, и аль-Масих (Царь Исраила).

8Ученики вдруг оглянулись и уже никого не увидели рядом с собой, кроме Исы. 9Когда они спускались с горы, Иса предупредил их, чтобы они никому не рассказывали о том, что видели, до тех пор, пока Ниспосланный как Человек не воскреснет из мёртвых. 10Они сохранили это в тайне, но между собой рассуждали о том, что же означают слова «воскреснуть из мёртвых». 11А Ису они спросили:

– Почему учители Таурата говорят, что вначале, перед аль-Масихом, должен прийти Ильяс?

12– Верно, – ответил Иса, – Ильяс действительно должен прийти первым и всё приготовить9:12 См. Мал. 4:5-6.. Но почему же о Ниспосланном как Человек в Писании говорится, что Ему придётся перенести много страданий и унижений? 13Но говорю вам, что Ильяс уже пришёл9:13 См. Лк. 1:13-17., и люди поступили с ним по своему произволу, как о нём и было написано9:13 См. 6:14-29, также 3 Цар. 19:1-10..

Исцеление мальчика, одержимого нечистым духом

(Мат. 17:14-19; Лк. 9:37-42)

14Когда они вернулись к остальным ученикам, то увидели, что тех окружила большая толпа и учители Таурата спорят с ними. 15Когда все увидели Ису, они пришли в крайнее изумление и побежали Ему навстречу, чтобы приветствовать Его.

16– О чём у вас спор? – спросил Иса.

17Кто-то из толпы ответил:

– Учитель, я привёл к Тебе сына, в него вселился дух немоты. 18И когда дух схватывает его, то бросает его на землю, и тогда у мальчика идёт пена изо рта, он скрежещет зубами и цепенеет. Я просил Твоих учеников изгнать духа, но они не смогли.

19Иса в ответ сказал:

– О неверующее поколение! Сколько Мне ещё быть с вами? Сколько Мне ещё терпеть вас? Приведите мальчика ко Мне.

20Мальчика привели. Как только дух увидел Ису, он вызвал у мальчика приступ, и тот упал и стал кататься по земле, и изо рта у него пошла пена.

21– Давно с ним так? – спросил Иса у отца.

– С самого детства, – ответил тот. – 22Дух часто бросает его то в огонь, то в воду, чтобы погубить его. Сжалься над нами и помоги, если Ты что-нибудь можешь сделать.

23– Если можешь?! – сказал Иса. – Кто верит, тот может всё.

24И тотчас отец мальчика воскликнул:

– Я верю, но помоги мне победить свои сомнения!

25Иса, увидев, что сбегается толпа, приказал нечистому духу, говоря:

– Дух немоты и глухоты, Я приказываю тебе: выйди из него и больше никогда не входи!

26Вскрикнув и сильно сотрясши мальчика, дух вышел. Мальчик стал как мёртвый, так что многие говорили, что он умер. 27Но Иса, взяв мальчика за руку, поднял его, и тот встал.

28Позже, когда Иса вошёл в дом, ученики спросили Его наедине:

– Почему же мы не смогли изгнать его?

29Иса ответил:

– Этот вид демонов можно изгнать только молитвой9:29 Или: «молитвой и постом»..

Иса аль-Масих вновь говорит о своей смерти и воскресении

(Мат. 17:22-23; Лк. 9:43-45)

30Покинув ту местность, Иса и Его ученики проходили через Галилею, и Иса не хотел, чтобы кто-либо об этом знал, 31потому что Он был занят наставлением Своих учеников.

Он говорил им:

– Ниспосланный как Человек будет предан в руки людей, которые убьют Его, но через три дня Он воскреснет.

32Но они не поняли, что Он имел в виду, а спросить боялись.

Кто важнее?

(Мат. 18:1-5; Лк. 9:46-48)

33Они пришли в Капернаум, и, когда расположились в доме, Иса спросил учеников:

– Скажите, о чём это вы говорили по дороге?

34Но они молчали, потому что по дороге они спорили о том, кто из них важнее. 35Тогда Иса сел, созвал двенадцать учеников и сказал:

– Кто хочет быть первым, тот пусть будет последним из всех и всем слугой.

36Взяв ребёнка, Он поставил его посреди них, обнял его и продолжал:

37– Кто ради Меня принимает такого ребёнка, тот принимает и Меня, а кто принимает Меня, тот принимает не только Меня, но и Пославшего Меня.

Кто не против нас, тот за нас

(Мат. 10:42; Лк. 9:49-50)

38Иохан сказал Ему:

– Учитель! Мы видели человека, который Твоим именем изгонял демонов, и мы пытались запретить ему, потому что он не следовал за нами.

39– Не запрещайте ему, – сказал Иса. – Кто Моим именем совершает чудеса, тот не станет после этого говорить обо Мне плохо. 40Кто не против нас, тот за нас. 41Если кто-либо напоит вас чашей воды за то, что вы носите имя последователей аль-Масиха, то, говорю вам истину, он не останется без награды.

Об искушениях

(Мат. 18:8-9; Лк. 17:1-2)

42Если же кто введёт в грех одного из этих малых, верующих в Меня, то для него было бы лучше, если бы ему надели на шею мельничный жёрнов и бросили в море. 43-44Если твоя рука влечёт тебя ко греху, отсеки её. Лучше тебе оставаться с одной рукой, но войти в рай, чем с двумя руками пойти в ад, в неугасимый огонь!9:43-44 В некоторых рукописях присутствуют слова: «Где черви, грызущие тело, не умирают, и огонь пожирающий не угасает». То же в 9:45-46. 45-46Если твоя нога влечёт тебя ко греху, отсеки её. Лучше тебе остаться с одной ногой, но войти в рай, чем с двумя ногами быть брошенным в ад. 47Если твой глаз влечёт тебя ко греху, вырви его. Лучше тебе с одним глазом войти в Царство Аллаха, чем с двумя глазами быть брошенным в ад, 48где

«черви, грызущие тело, не умирают,

и огонь пожирающий не угасает»9:48 Ис. 66:24..

49Потому что каждый будет очищен огнём, как жертва очищается солью9:49 См. Лев. 2:13; Езек. 43:24.. 50Соль – хорошая вещь, но если она потеряет свой вкус, то что может опять сделать её солёной? Имейте в себе соль и будьте в мире друг с другом.