Marko 7 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 7:1-37

Miyambo ya Makolo ya Ayuda

1Afarisi ndi ena mwa aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anasonkhana momuzungulira Yesu ndipo 2iwo anaona ophunzira ake akudya chakudya ndi mʼmanja mwakuda kapena kuti mʼmanja mosasamba. 3(Afarisi ndi Ayuda onse sadya pokhapokha atasamba mʼmanja, kusunga mwambo wa makolo awo. 4Akabwera kuchokera ku msika samadya pokhapokha atasamba. Ndipo amasunga miyambo ina yambiri monga, kutsuka zikho, mitsuko ndi maketulo).

5Choncho Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anafunsa Yesu kuti, “Nʼchifukwa chiyani ophunzira anu satsatira mwambo wa makolo, mʼmalo mwake amangodya chakudya ndi mʼmanja mwakuda?”

6Iye anayankha kuti, “Yesaya ananena zoona pamene ananenera za inu achiphamaso; monga kunalembedwa kuti:

“Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

7Amandilambira Ine kwachabe;

ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.

8Mwasiya malamulo a Mulungu ndipo mwagwiritsitsa miyambo ya anthu.”

9Ndipo anawawuzanso kuti, “Inu muli ndi njira yabwino yokankhira kumbali malamulo a Mulungu kuti mukatsatire miyambo yanuyo! 10Pakuti Mose anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako,’ ndipo, ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’ 11Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukanayenera kulandira kuchokera kwa ine ndi Korobani’ (kutanthauza kuti, mphatso yoperekedwa kwa Mulungu), 12pamenepo inu simumalola kuti achitire kanthu kalikonse abambo kapena amayi ake. 13Potero mumachepetsa mawu a Mulungu kukhala wopanda mphamvu ndi miyambo yanu imene mumapatsirana. Ndipo mumachita zinthu zina zambiri monga zimenezi.”

14Yesu anayitananso gulu la anthu ndipo anati, “Tandimverani nonsenu, ndipo zindikirani izi. 15Palibe kanthu kunja kwa munthu kamene kakalowa mwa iye kangamusandutse wodetsedwa. Koma zimene zituluka mwa munthu ndizo zimupanga kukhala wodetsedwa.” 16(Ngati wina ali ndi makutu akumva amve).

17Atalisiya gulu la anthu ndi kulowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa za fanizoli 18Iye anawafunsa kuti, “Kodi nanunso simumvetsetsa? Kodi simukuona kuti palibe kanthu kamene kakalowa mwa munthu kochokera kunja kakhoza kumudetsa? 19Pakuti sikalowa mu mtima wake koma mʼmimba mwake, ndipo kenaka kamatuluka kunja.” (Ndi mawu amenewa, Yesu anayeretsa zakudya zonse).

20Anapitiriza kuti, “Chimene chichokera mwa munthu ndi chomwe chimamudetsa. 21Pakuti kuchokera mʼkati mwa mitima ya anthu, mumatuluka maganizo oyipa, chiwerewere, kuba, kupha, chigololo, 22dyera, nkhwidzi, chinyengo, machitidwe onyansa, kaduka, chipongwe, kudzikuza ndi kupusa. 23Zoyipa zonsezi zimatuluka mʼkati ndipo zimadetsa munthu.”

Chikhulupiriro cha Mayi wa ku Siriya Fonisia

24Yesu anachoka kumalo amenewo napita ku madera a Turo. Iye analowa mʼnyumba ndipo sanafune wina kuti adziwe zimenezi; komabe sanathe kudzibisa. 25Kunena zoona, amayi amene kamwana kawo kakakazi kanali kogwidwa ndi mzimu woyipa, atangomva za Iye, anabwera nagwada pa mapazi ake. 26Mayiyu anali Mhelene, wobadwira ku Fonisia wa ku Siriya. Anamupempha Yesu kuti atulutse chiwanda mwa mwana wake.

27Iye anamuwuza kuti, “Choyamba asiye ana adye zimene akuzifuna, pakuti si kwabwino kutenga buledi wa ana ndi kuponyera agalu awo.”

28Mayiyo anayankha kuti, “Inde Ambuye, koma ngakhale agalu amadya zomwe zimagwa pansi kuchokera pa tebulo la ana.”

29Ndipo Iye anamuwuza kuti, “Chifukwa cha yankholi, ukhoza kupita; chiwanda chachoka mwa mwana wako wamkazi.”

30Atapita kwawo anakapeza mwana wake aligone pa bedi, chiwanda chitatuluka.

Kuchiritsidwa kwa Munthu Wosamva ndi Wosayankhula

31Ndipo Yesu anachoka ku dera la Turo nadutsa pakati pa Sidoni, kutsikira ku nyanja ya Galileya kupita ku dera la Dekapoli. 32Kumeneko anthu ena anabweretsa kwa Iye munthu amene anali wosamva ndi wosayankhula, ndipo anamupempha kuti asanjike dzanja pa iye.

33Atamutengera iye pambali, patali ndi gulu la anthu, Yesu analowetsa zala zake mʼmakutu a munthuyo. Kenaka anapaka malovu pachala ndi kukhudza lilime la munthuyo. 34Iye anayangʼana kumwamba ndipo ndi mawu otsitsa moyo, anati kwa iye, “Efataa!” (Kutanthauza kuti, “Tsekuka!”) 35Atachita izi, makutu a munthuyo anatsekuka komanso lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula momveka bwino.

36Yesu anawalamula kuti asawuze wina aliyense. Koma pamene anapitiriza kuwaletsa, iwo anapitiriza kuyankhula za izi. 37Anthu anadabwa kwambiri. Iwo anati, “Wachita zonse bwino, ngakhale Iyenso atsekula makutu a osamva ndi osayankhula kuti ayankhule.”

New International Version – UK

Mark 7:1-37

That which defiles

1The Pharisees and some of the teachers of the law who had come from Jerusalem gathered round Jesus 2and saw some of his disciples eating food with hands that were defiled, that is, unwashed. 3(The Pharisees and all the Jews do not eat unless they give their hands a ceremonial washing, holding to the tradition of the elders. 4When they come from the market-place they do not eat unless they wash. And they observe many other traditions, such as the washing of cups, pitchers and kettles.7:4 Some early manuscripts pitchers, kettles and dining couches)

5So the Pharisees and teachers of the law asked Jesus, ‘Why don’t your disciples live according to the tradition of the elders instead of eating their food with defiled hands?’

6He replied, ‘Isaiah was right when he prophesied about you hypocrites; as it is written:

‘ “These people honour me with their lips,

but their hearts are far from me.

7They worship me in vain;

their teachings are merely human rules.”7:7 Isaiah 29:13

8You have let go of the commands of God and are holding on to human traditions.’

9And he continued, ‘You have a fine way of setting aside the commands of God in order to observe7:9 Some manuscripts set up your own traditions! 10For Moses said, “Honour your father and mother,”7:10 Exodus 20:12; Deut. 5:16 and, “Anyone who curses their father or mother is to be put to death.”7:10 Exodus 21:17; Lev. 20:9 11But you say that if anyone declares that what might have been used to help their father or mother is Corban (that is, devoted to God) – 12then you no longer let them do anything for their father or mother. 13Thus you nullify the word of God by your tradition that you have handed down. And you do many things like that.’

14Again Jesus called the crowd to him and said, ‘Listen to me, everyone, and understand this. 15Nothing outside a person can defile them by going into them. Rather, it is what comes out of a person that defiles them.’ 167:16 Some manuscripts include here the words of 4:23.

17After he had left the crowd and entered the house, his disciples asked him about this parable. 18‘Are you so dull?’ he asked. ‘Don’t you see that nothing that enters a person from the outside can defile them? 19For it doesn’t go into their heart but into their stomach, and then out of the body.’ (In saying this, Jesus declared all foods clean.)

20He went on: ‘What comes out of a person is what defiles them. 21For it is from within, out of a person’s heart, that evil thoughts come – sexual immorality, theft, murder, 22adultery, greed, malice, deceit, lewdness, envy, slander, arrogance and folly. 23All these evils come from inside and defile a person.’

Jesus honours a Syro-Phoenician woman’s faith

24Jesus left that place and went to the vicinity of Tyre.7:24 Many early manuscripts Tyre and Sidon He entered a house and did not want anyone to know it; yet he could not keep his presence secret. 25In fact, as soon as she heard about him, a woman whose little daughter was possessed by an impure spirit came and fell at his feet. 26The woman was a Greek, born in Syrian Phoenicia. She begged Jesus to drive the demon out of her daughter.

27‘First let the children eat all they want,’ he told her, ‘for it is not right to take the children’s bread and toss it to the dogs.’

28‘Lord,’ she replied, ‘even the dogs under the table eat the children’s crumbs.’

29Then he told her, ‘For such a reply, you may go; the demon has left your daughter.’

30She went home and found her child lying on the bed, and the demon gone.

Jesus heals a deaf and mute man

31Then Jesus left the vicinity of Tyre and went through Sidon, down to the Sea of Galilee and into the region of the Decapolis.7:31 That is, the Ten Cities 32There some people brought to him a man who was deaf and could hardly talk, and they begged Jesus to place his hand on him.

33After he took him aside, away from the crowd, Jesus put his fingers into the man’s ears. Then he spat and touched the man’s tongue. 34He looked up to heaven and with a deep sigh said to him, ‘Ephphatha!’ (which means ‘Be opened!’). 35At this, the man’s ears were opened, his tongue was loosed and he began to speak plainly.

36Jesus commanded them not to tell anyone. But the more he did so, the more they kept talking about it. 37People were overwhelmed with amazement. ‘He has done everything well,’ they said. ‘He even makes the deaf hear and the mute speak.’