Marko 3 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 3:1-35

Yesu Achiritsa Wolumala Dzanja

1Nthawi inanso analowa mʼsunagoge, ndipo munthu wa dzanja lolumala anali momwemo. 2Ena a iwo anafunafuna chifukwa chakuti akamuneneze Yesu, potero anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati angamuchiritse tsiku la Sabata. 3Yesu anati kwa munthu wolumala dzanjayo, “Imirira, bwera kuno kutsogolo.”

4Ndipo Yesu anawafunsa kuti, “Kodi chololedwa ndi chiyani pa tsiku la Sabata: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kupha?” Koma iwo anakhala chete.

5Yesu anawayangʼana ndi mkwiyo ndipo powawidwa mtima chifukwa cha mitima yawo yowuma anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye analiwongola, ndipo dzanja lake linachira. 6Kenaka Afarisi anatuluka nayamba kukonza chiwembu ndi Aherode mmene angamuphere Yesu.

Magulu a Anthu Amutsata Yesu

7Yesu anachoka pamodzi ndi ophunzira ake napita ku nyanja, ndipo gulu lalikulu la anthu lochokera ku Galileya linamutsata. 8Atamva zonse zimene amachita, anthu ambiri anabwera kwa Iye kuchokera ku Yudeya, Yerusalemu, Idumeya ndi madera a ku tsidya kwa mtsinje wa Yorodani ndi ozungulira Turo ndi Sidoni. 9Chifukwa cha gulu la anthu, anawuza ophunzira ake kuti apezeretu bwato likhale, kuti anthu angamupanikize. 10Pakuti anachiritsa ambiri, kotero kuti iwo amene anali ndi matenda amakankhana kutsogolo kuti amukhudze. 11Nthawi iliyonse mizimu yoyipa ikamuona, imagwa pansi pamaso pake ndi kufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” 12Koma anayichenjeza mwamphamvu kuti isanene kuti Iye anali ndani.

Yesu Asankha Ophunzira Khumi ndi Awiri

13Yesu anakwera ku phiri ndipo anayitana amene anawafuna, ndipo anabwera kwa Iye. 14Iye anasankha khumi ndi awiri, nawayika akhale atumwi; pokhala ndi Iye aziwatuma kukalalikira 15ndi kuti akhale ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda. 16Awa ndi khumi ndi awiri amene anawasankha: Simoni (amene anapatsidwa dzina lakuti Petro); 17Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi mʼbale wake Yohane (iwowa anawapatsa dzina lakuti Bowanege, ndiye kuti ana a bingu); 18Andreya, Filipo, Bartumeyu, Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Tadeyo, Simoni Zelote, 19ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.

Yesu ndi Belezebabu

20Pambuyo pake Yesu analowa mʼnyumba, ndipo gulu la anthu linasonkhananso, kotero kuti Iye pamodzi ndi ophunzira ake sanapeze mpata kuti adye. 21Anthu a ku banja lake atamva zimenezi, anapita kuti akamutenga, pakuti ankanena kuti, “Wazungulira mutu.”

22Ndipo aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anati, “Iye wagwidwa ndi Belezebabu! Ndi ulamuliro wa mkulu wa ziwanda akutulutsa ziwanda.”

23Pamenepo Yesu anawayitana nawayankhula mʼmafanizo nati: “Kodi Satana angatulutse bwanji Satana? 24Ngati ufumu ugawanikana mwa iwo okha, ufumu umenewo sungakhalitse. 25Ngati nyumba igawanikana mwa iyo yokha, nyumba imeneyo singathe kuyima. 26Ndipo ngati Satana adzitsutsa yekha sangathe kuyima; ulamuliro wake watha. 27Kunena zoona, palibe munthu angalowe mʼnyumba ya munthu wamphamvu ndi kutenga katundu wake pokhapokha atayamba wamumanga munthu wamphamvuyo. Pamenepo akhoza kumubera. 28Ndikukuwuzani zoona kuti machimo onse ndi zamwano zonse za anthu zidzakhululukidwa, 29koma aliyense amene achitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa pakuti wachita tchimo losatha.”

30Ananena izi chifukwa anati, “Ali ndi mzimu woyipa.”

Amayi ndi Abale ake a Yesu

31Pamenepo amayi ndi abale ake a Yesu anafika. Atayima kunja, anatuma wina kuti akamuyitane Iye. 32Gulu la anthu linakhala momuzungulira Iye, ndipo anamuwuza kuti, “Amayi ndi abale anu ali panja akukufunani.”

33Iye anafunsa kuti, “Amayi ndi abale anga ndi ndani?”

34Pamenepo anayangʼana anthu amene anakhala momuzungurira ndipo anati, “Awa ndi amayi anga ndi abale anga! 35Aliyense amene achita chifuniro cha Mulungu ndi mʼbale wanga ndi mlongo wanga ndi amayi anga.”

Священное Писание

Марк 3:1-35

Исцеление в субботу человека с больной рукой

(Мат. 12:9-14; Лк. 6:6-11)

1Иса снова зашёл в молитвенный дом иудеев. Там был человек с иссохшей рукой. 2Недоброжелатели Исы внимательно наблюдали за Ним, не будет ли Он исцелять этого человека в субботу, потому что искали повод обвинить Его. 3Иса сказал человеку с иссохшей рукой:

– Встань посередине.

4Затем Он спросил их:

– Что позволительно делать в субботу: добро или зло? Спасать жизнь или убивать?

Они молчали. 5Тогда Иса, обведя их гневным взглядом и скорбя о чёрствости их сердец, сказал больному:

– Протяни руку.

Тот протянул, и его рука стала совершенно здоровой.

6Выйдя из молитвенного дома, блюстители Закона немедленно начали совещаться со сторонниками правителя Ирода3:6 Это Ирод Антипа, сын Ирода Великого от самарянки Малфаки. Он правил Галилеей и Переей с 4 г. до н. э. по 39 г. н. э. о том, как им убить Ису.

За Исой Масихом следует множество народа

(Мат. 4:23-25; 12:15-16; Лк. 6:17-19)

7А Иса пошёл с учениками к озеру. За ними следовало великое множество народа из Галилеи, Иудеи, 8Иерусалима, Идумеи, из-за реки Иордан, из окрестностей Тира и Сидона. Эти люди шли к Исе, потому что слышали о делах, которые Он совершал. 9Иса велел ученикам приготовить лодку, чтобы не теснили Его, потому что толпа была весьма многочисленна. 10Он исцелил многих людей, и поэтому все больные проталкивались вперёд, чтобы прикоснуться к Нему. 11А те, в ком были нечистые духи, когда видели Его, падали перед Ним и кричали:

– Ты – Сын Всевышнего (Царственный Спаситель)!

12Но Иса строго запрещал им разглашать о том, кто Он.

Избрание двенадцати посланников Масиха

(Мат. 10:2-4; Лк. 6:14-16; Деян. 1:13)

13Однажды Иса поднялся на гору и позвал к Себе тех, кого Сам пожелал. Они пришли к Нему, 14и из них Он избрал двенадцать человек (которых назвал Своими посланниками), чтобы они всегда были с Ним и чтобы Он мог посылать их возвещать Радостную Весть. 15Он также наделил их властью изгонять демонов. 16Итак, Иса назначил двенадцать человек: Шимона (которому Он дал имя Петир), 17Якуба, сына Завдая, и Иохана, брата Якуба (их Он называл «Бней-регеш», что значит «сыны грома»), 18Андера, Филиппа, Варфоломея, Матая, Фому, Якуба (сына Алфея), Фаддея, Шимона Кананита3:18 Кананит – то же, что и зилот (см. Лк. 6:15), т. е. «ревнитель» – член крайней религиозно-политической группировки, выступавшей против римской оккупации Исраила. 19и Иуду Искариота (который впоследствии и предал Его).

Иса Масих изгоняет демонов силой Всевышнего

(Мат. 12:22-29; Лк. 11:14-23; 12:10)

20Однажды, когда Иса вошёл в дом, опять собралась толпа, так что Ему и Его ученикам даже поесть было некогда. 21Услышав об этом, родственники Исы пришли забрать Его, потому что они говорили:

– Он не в Своём уме.

22А учители Таурата, пришедшие из Иерусалима, утверждали:

– Он одержим Баал-Зевулом (сатаной). Он изгоняет демонов силой повелителя демонов.

23Тогда, подозвав их к Себе, Иса стал объяснять им с помощью притч:

– Как сатана может изгонять сатану? 24Если царство разделится на враждующие части, оно не сможет устоять, 25и если дом будет разделён враждой, то этот дом не сможет устоять. 26Если сатана разделился и враждует против самого себя, то он не может устоять, и конец его близок. 27Ведь никто не может войти в дом сильного человека и разграбить его добро, если сначала не свяжет его, – только тогда можно будет ограбить его дом. 28Говорю вам истину: все грехи и любое кощунство будут прощены людям, 29но кощунство над Святым Духом не простится никогда, вина за этот грех остаётся на человеке навсегда.

30Он сказал это потому, что они говорили, будто в Нём нечистый дух.

Иса Масих говорит о Своей истинной семье

(Мат. 12:46-50; Лк. 8:19-21)

31Пришли Его мать и братья и, стоя снаружи, попросили позвать Его. 32Вокруг Исы было много людей, и Ему передали:

– Твоя мать и Твои братья стоят снаружи и спрашивают Тебя.

33– Кто Мне мать и кто Мне братья? – спросил их в ответ Иса.

34Он обвёл взглядом сидящих вокруг Него людей и сказал:

– Вот Моя мать и Мои братья. 35Кто исполняет волю Всевышнего, тот Мне и брат, и сестра, и мать.