Marko 13 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 13:1-37

Zizindikiro za Kutha kwa Masiku Yomaliza

1Iye atachoka mʼNyumba ya Mulungu, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Aphunzitsi taonani! Miyala ikuluikulu! Nyumba zikongolerenji!”

2Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuziona nyumba zikuluzikuluzi? Palibe mwala ndi umodzi pano umene udzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”

3Yesu atakhala pansi pa phiri la Olivi moyangʼanana ndi Nyumba ya Mulungu, Petro, Yakobo, Yohane ndi Andreya anamufunsa Iye pambali kuti, 4“Tatiwuzani, izi zidzachitika liti? Nanga chizindikiro chakuti zatsala pangʼono kukwaniritsidwa chidzakhala chiyani?”

5Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani kuti wina asakunyengeni. 6Anthu ambiri adzabwera mʼdzina langa, nadzati, ‘Ine ndi Iyeyo,’ ndipo adzanamiza anthu ambiri. 7Pamene mudzamva zankhondo ndi mbiri zankhondo, musadzadzidzimuke. Zinthu zotere ziyenera kuchitika, koma sikuti chimaliziro chafika kale ayi. 8Mtundu udzawukira mtundu unzake, ndi ufumu kuwukira ufumu unzake. Kudzakhala zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana, ndi njala. Izi ndi chiyambi chabe cha zowawa monga mayi pobereka.

9“Muyenera kukhala tcheru. Mudzaperekedwa ku mabwalo oweruza ndi kukwapulidwa mwankhanza mʼmasunagoge. Mudzayima pamaso pa abwanamkubwa ndi mafumu monga mboni kwa iwo chifukwa cha Ine. 10Ndipo Uthenga Wabwino uyenera kuyamba walalikidwa kwa anthu a mitundu yonse. 11Nthawi iliyonse pamene mwamangidwa ndi kuyimbidwa mlandu, musadandaule za zimene mudzanena. Zimene mudzapatsidwe pa nthawiyo yankhulani; pakuti sindinu amene mudzayankhula, koma Mzimu Woyera.

12“Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe, ndipo abambo adzapereka mwana wawo. Ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe. 13Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine, koma amene adzalimbika mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.

14“Mukadzaona ‘chinthu chonyansa chosakaza’ chitayima pa malo amene si ake, owerenga azindikire. Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire kumapiri. 15Aliyense amene ali pa denga la nyumba yake asatsike kapena kulowa mʼnyumba kukatenga kanthu kalikonse. 16Aliyense amene ali ku munda asabwerere kukatenga mkanjo wake. 17Kudzakhala koopsa mʼmasiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! 18Pempherani kuti zimenezi zisadzachitike nthawi yozizira, 19chifukwa masiku amenewo adzakhala owawitsa osafanana ndi ena kuyambira pachiyambi, pamene Mulungu analenga dziko, kufikira lero ndipo sadzafanananso ndi ena. 20Ambuye akanapanda kufupikitsa masikuwo, palibe amene akanapulumuka. Koma chifukwa cha osankhidwiratu, amene anawasankha, Iye anawafupikitsa. 21Pa nthawi imeneyo, ngati wina adzati kwa inu, ‘Taonani, Khristu ali kuno, kapena, Taonani, uyo ali apoyo!’ musakhulupirire. 22Pakuti akhristu onama ndi aneneri onama adzaonekera ndipo adzachita zizindikiro ndi zodabwitsa kuti anyenge osankhidwiratu ngati kutakhala kotheka kutero. 23Choncho khalani tcheru; ndakuwuzani zonse nthawi isanafike.

24“Koma masiku amenewo, masautsowo atatha,

“ ‘dzuwa lidzada,

ndipo mwezi sudzawala;

25nyenyezi zidzagwa kuchokera ku thambo,

ndipo mayiko mumlengalenga adzagwedezeka!’

26“Nthawi imeneyo anthu adzaona Mwana wa Munthu akubwera mʼmitambo ndi mphamvu yayikulu ndi ulemerero. 27Ndipo adzatuma angelo ake kukasonkhanitsa osankhidwiratu ake ku mphepo zinayi, kuyambira kumalekezero a dziko lapansi mpaka ku malekezero ake enanso.

28“Tsopano phunzirani phunziro ili kuchokera ku mtengo wamkuyu. Pamene msonga za nthambi zake zikhala za nthete ndipo masamba ake ayamba kuphukira, mumadziwa kuti dzinja layandikira. 29Momwenso pamene muona zinthu izi zikuchitika, dziwani kuti wayandikira, ali pa khomo. 30Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika. 31Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”

Tsiku ndi Ora Sizikudziwika

32“Palibe amene akudziwa za tsikulo kapena nthawi, ngakhale angelo akumwamba, kapena Mwana, koma Atate wokha. 33Khalani maso! Khalani tcheru! Simudziwa pamene nthawi imeneyo idzafike. 34Zili ngati munthu amene akuchokapo. Amasiyira nyumba yake antchito ake, aliyense ndi ntchito yake; ndi kumuwuza wa pa khomo kuti azikhala maso.

35“Inunso muyenera kukhala maso chifukwa simukudziwa nthawi imene mwini nyumba adzabwere, kaya madzulo, kapena pakati pa usiku, kapena tambala akulira, kapena mʼbandakucha. 36Ngati atabwera mwadzidzidzi, asadzakupezeni inu muli mtulo. 37Zimene ndikunena kwa inu, ndikunena kwa aliyense: ‘Khalani tcheru!’ ”

Thai New Contemporary Bible

มาระโก 13:1-37

หมายสำคัญแห่งวาระสิ้นยุค

(มธ.24:1-51; ลก.21:5-36)

1ขณะพระเยซูเสด็จออกจากพระวิหาร สาวกคนหนึ่งทูลพระองค์ว่า “ดูสิ พระอาจารย์! หินก้อนมหึมาทั้งนั้น! ช่างเป็นอาคารที่งามตระการตายิ่งนัก!”

2พระเยซูตรัสตอบว่า “พวกท่านเห็นอาคารใหญ่โตมโหฬารเหล่านี้ใช่ไหม? ศิลาที่นี่จะไม่เหลือซ้อนทับกันสักก้อนเดียว ทุกก้อนจะถูกโยนทิ้งลงมาหมด”

3ขณะพระเยซูประทับอยู่บนภูเขามะกอกเทศตรงข้ามกับพระวิหาร เปโตร ยากอบ ยอห์น และอันดรูว์มาทูลถามพระองค์เป็นการส่วนตัวว่า 4“ขอทรงบอกพวกข้าพระองค์เถิด สิ่งเหล่านี้จะเกิดขึ้นเมื่อใด? และอะไรเป็นหมายสำคัญว่าสิ่งทั้งปวงนั้นกำลังจะสำเร็จ?”

5พระเยซูตรัสกับพวกเขาว่า “จงระวัง อย่าให้ใครมาล่อลวงท่าน 6หลายคนจะมาในนามของเราและอ้างตัวว่า ‘เราคือผู้นั้น’ แล้วล่อลวงคนเป็นอันมาก 7เมื่อท่านได้ยินข่าวสงครามและข่าวลือเรื่องสงคราม อย่าตื่นตกใจ เพราะสิ่งเหล่านั้นต้องเกิดขึ้นแต่ยังไม่ถึงจุดจบ 8ประชาชาติต่อประชาชาติและอาณาจักรต่ออาณาจักรจะสู้รบกัน จะเกิดแผ่นดินไหวและการกันดารอาหารในที่ต่างๆ เหตุการณ์เหล่านี้คือขั้นเริ่มต้นของความเจ็บปวดก่อนคลอดบุตร

9“ท่านต้องเฝ้าระวัง ท่านจะถูกคุมตัวไปยังที่ว่าการในท้องที่และถูกโบยตีในธรรมศาลา ท่านต้องไปยืนอยู่ต่อหน้าผู้ว่าการและกษัตริย์แล้วเป็นพยานแก่พวกเขาเพื่อเรา 10ข่าวประเสริฐต้องประกาศแก่มวลประชาชาติก่อน 11เมื่อใดก็ตามที่ท่านถูกจับกุมและส่งตัวขึ้นศาล อย่าวิตกกังวลไปก่อนว่าจะพูดอะไรดี จงพูดไปตามถ้อยคำที่ประทานแก่ท่านในเวลานั้นเพราะไม่ใช่ตัวท่านเองที่เป็นผู้พูดแต่เป็นพระวิญญาณบริสุทธิ์

12“พี่น้องจะทรยศกันเองถึงตายและพ่อจะทรยศลูก ลูกจะกบฏต่อพ่อแม่และเป็นเหตุให้พวกเขาถึงตาย 13คนทั้งปวงจะเกลียดชังท่านเพราะเรา แต่ผู้ที่ยืนหยัดจนถึงที่สุดจะรอด

14“เมื่อใดที่ท่านเห็น ‘สิ่งที่น่าสะอิดสะเอียนอันเป็นต้นเหตุของวิบัติ’13:14 ดนล. 9:27; 11:31; 12:11 ตั้งอยู่ในที่ซึ่งไม่ใช่ที่ของมัน13:14 หรือเขาเช่นเดียวกับข้อ 29 (ให้ผู้อ่านทำความเข้าใจเอาเถิด) เมื่อนั้นให้ผู้ที่อยู่ในยูเดียหนีไปที่ภูเขา 15ผู้ที่อยู่บนดาดฟ้าหลังคาบ้านอย่าลงมาหรือเข้าบ้านมาหยิบสิ่งใดออกไป 16ผู้ที่อยู่ตามทุ่งนาก็อย่ากลับไปเอาเสื้อคลุมของท่าน 17วันเหล่านั้นน่าหวาดกลัวยิ่งนักสำหรับหญิงมีครรภ์หรือแม่ลูกอ่อน 18จงอธิษฐานให้เหตุการณ์นี้ไม่เกิดในฤดูหนาว 19เพราะเวลานั้นจะเป็นวาระแห่งความทุกข์ลำเค็ญอย่างที่ไม่มีครั้งใดเทียบเท่าตั้งแต่เริ่มแรกเมื่อพระเจ้าทรงสร้างโลกจนถึงบัดนี้ และจะไม่มีครั้งใดเทียบเท่าอีก 20หากองค์พระผู้เป็นเจ้าไม่ทรงร่นวันเหล่านั้นให้สั้นเข้าก็จะไม่มีใครเหลือรอดเลย แต่เพราะเห็นแก่ผู้ที่ทรงเลือกสรรไว้พระองค์จึงทรงทำให้วันเหล่านั้นสั้นลง 21เมื่อเวลานั้นมาถึงหากมีใครมาบอกท่านว่า ‘ดูเถิด พระคริสต์13:21 หรือพระเมสสิยาห์อยู่ที่นี่!’ หรือ ‘ดูเถิด พระองค์อยู่ที่นั่น!’ อย่าไปเชื่อเลย 22เพราะจะมีพระคริสต์ปลอมและผู้เผยพระวจนะเท็จปรากฏขึ้น พวกเขาจะแสดงหมายสำคัญและการอัศจรรย์ต่างๆ เพื่อลวงผู้ที่ทรงเลือกสรรไว้หากเป็นไปได้ 23ฉะนั้นจงระวัง เราบอกทุกอย่างแก่ท่านไว้ล่วงหน้าแล้ว

24“แต่ในวาระนั้นหลังจากความทุกข์เข็ญ

“ ‘ดวงอาทิตย์จะถูกดับ

ดวงจันทร์จะไม่ทอแสง

25ดวงดาวทั้งหลายจะร่วงจากท้องฟ้า

และฟ้าสวรรค์จะถูกเขย่า’13:25 อสย.13:10; 34:4

26“เมื่อนั้นคนทั้งหลายจะเห็นบุตรมนุษย์เสด็จมาในหมู่เมฆด้วยเดชานุภาพและพระเกียรติสิริอันยิ่งใหญ่ 27พระองค์จะทรงส่งทูตสวรรค์ของพระองค์มารวบรวมผู้ที่ทรงเลือกสรรไว้จากทั้งสี่ทิศ จากปลายแผ่นดินโลกถึงสุดขอบฟ้าสวรรค์

28“จงเรียนรู้บทเรียนนี้จากต้นมะเดื่อ คือทันทีที่มันแตกกิ่งและผลิใบท่านก็รู้ว่าฤดูร้อนใกล้เข้ามาแล้ว 29เช่นเดียวกันเมื่อท่านเห็นสิ่งเหล่านี้เกิดขึ้น ท่านก็รู้ว่าสิ่งนี้13:29 หรือเขาหรือพระองค์ใกล้เข้ามาแล้ว อยู่ที่ประตูนี่เอง 30เราบอกความจริงแก่ท่านว่าคนในยุคนี้13:30 หรือชาติพันธุ์นี้ยังไม่ทันล่วงลับไป สิ่งทั้งปวงเหล่านี้ก็เกิดขึ้นแล้วอย่างแน่นอน 31ฟ้าและดินจะสูญสิ้นไปแต่ถ้อยคำของเราจะไม่มีวันสูญสิ้น

วันเวลาที่ไม่มีใครรู้

32“ไม่มีใครรู้วันเวลาที่เหตุการณ์นั้นจะเกิดขึ้น แม้แต่ทูตสวรรค์หรือพระบุตรก็ไม่รู้ พระบิดาเท่านั้นที่ทรงทราบ 33จงระวัง! จงตื่นตัว!13:33 สำเนาต้นฉบับ บางสำเนาว่าตื่นตัวและอธิษฐาน ท่านไม่รู้ว่าเวลานั้นจะมาถึงเมื่อใด 34ก็เหมือนชายคนหนึ่งออกจากบ้านไป เขาตั้งคนรับใช้ให้รับผิดชอบหน้าที่ต่างๆ ตามที่แต่ละคนได้รับมอบหมายและบอกคนเฝ้าประตูให้เฝ้าระวังไว้

35“ฉะนั้นจงเฝ้าระวังอยู่เพราะท่านไม่รู้ว่าเจ้าของบ้านจะกลับมาเมื่อใด อาจจะกลับมาเวลาค่ำหรือเวลาเที่ยงคืน เวลาไก่ขัน หรือเวลารุ่งสาง 36ถ้าเขากลับมากระทันหันก็อย่าให้เขาพบว่าท่านกำลังหลับอยู่ 37สิ่งที่เราบอกกับท่านเราก็บอกกับทุกๆ คนว่า ‘จงเฝ้าระวัง!’”