Maliro 4 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 4:1-22

1Haa! Golide wathimbirira,

golide wosalala wasinthikiratu!

Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika

pamphambano ponse pa mzinda.

2Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali

amene kale anali ngati golide,

tsopano ali ngati miphika ya dothi,

ntchito ya owumba mbiya!

3Ngakhale nkhandwe zimapereka bere

kuyamwitsa ana ake,

koma anthu anga asanduka ankhanza

ngati nthiwatiwa mʼchipululu.

4Lilime la mwana lakangamira kukhosi

chifukwa cha ludzu,

ana akupempha chakudya,

koma palibe amene akuwapatsa.

5Iwo amene kale ankadya zonona

akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda.

Iwo amene kale ankavala zokongola

tsopano akugona pa phulusa.

6Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu

kuposa anthu a ku Sodomu,

amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa

popanda owathandiza.

7Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana

ndi oyera kuposa mkaka.

Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi,

maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.

8Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye;

palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda.

Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo;

lawuma gwaa ngati nkhuni.

9Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa

amene anafa ndi njala;

chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda

iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.

10Amayi achifundo afika

pophika ana awo enieni,

ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu

anga anali kuwonongeka.

11Yehova wakwaniritsa ukali wake;

wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa.

Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni

kuti uwononge maziko ake.

12Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire,

kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse,

kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa

pa zipata za Yerusalemu.

13Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake

ndi mphulupulu za ansembe ake,

amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.

14Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda

ngati anthu osaona.

Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi

palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.

15Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!”

“Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!”

Akamathawa ndi kumangoyendayenda,

pakati pa anthu a mitundu yonse amati,

“Asakhalenso ndi ife.”

16Yehova mwini wake wawabalalitsa;

Iye sakuwalabadiranso.

Ansembe sakulandira ulemu,

akuluakulu sakuwachitira chifundo.

17Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana,

chithandizo chosabwera nʼkomwe,

kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu

wa anthu umene sukanatipulumutsa.

18Anthu ankalondola mapazi athu,

choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda.

Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka,

chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.

19Otilondola akuthamanga kwambiri

kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga;

anatithamangitsa mpaka ku mapiri

ndi kutibisalira mʼchipululu.

20Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo,

anakodwa mʼmisampha yawo.

Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake

pakati pa mitundu ya anthu.

21Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu.

Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi.

Koma iwenso chikho chidzakupeza;

udzaledzera mpaka kukhala maliseche.

22Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha;

Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo.

Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu,

ndi kuyika poyera mphulupulu zako.

Korean Living Bible

예레미야애가 4:1-22

함락 후의 예루살렘

1아, 슬프다! 금이 광택을 잃고 순금이 변했으며 성전의 돌들이 거리에 흩어 졌구나!

2시온의 젊은이들이 순금처럼 소중하더니 이제는 흔한 질그릇처럼 되고 말았네.

3여우도 제 새끼에게 젖을 먹이는데 내 백성은 잔인하여 사막의 타조 같구나.

4젖먹이가 목이 말라 그 혀가 입천장에 붙고 아이들이 먹을 것을 구걸하나 주는 자가 없구나.

5맛있는 것만 먹던 자가 이제는 거리에서 처량한 신세가 되었고 좋은 옷만 입고 자라던 자가 이제는 잿더미에 누웠네.

6전에 소돔성이 사람의 손을 대지 않고도 순식간에 무너지더니 이제 내 백성의 죄가 그 소돔 사람들의 죄보다 크구나.

7전에는 귀족들의 몸이 눈보다 더 깨끗하고 우유보다 더 희며 그 혈색이 산호보다 붉고 그 외모가 청옥 같았다.

8그러나 지금은 그 얼굴이 숯보다 검고 그 가죽이 뼈에 붙어 막대기같이 되었으니 아무도 그들을 길거리에서 알아볼 수 없게 되었네.

9칼날에 죽는 자가 굶어서 죽는 자보다 나은 것은 농산물이 부족하여 먹을 것이 없으므로 그들이 점점 시들어 죽어 가기 때문이다.

10내 백성이 멸망할 때 인자한 어머니가 자기 손으로 자식을 삶아 먹었다.

11여호와께서 몹시 화가 나셔서 그의 무서운 분노를 쏟아 시온에 불을 지르고 그 터전까지 태워 버리셨네.

12침략군이 예루살렘 성문으로 들어가리라고는 세상의 그 누구도 믿지 않았다.

13이런 일이 일어나게 된 것은 예언자들의 죄와 제사장들의 죄 때문이니 그들이 죄 없는 자들의 피를 흘렸음이라.

14그들이 맹인처럼 거리를 방황하며 그 옷이 피로 더럽혀졌으니 아무도 만질 수 없게 되었구나.

15사람들이 그들에게 “저리 가거라. 부정하다! 가거라! 가거라! 만지지 말아라!” 하고 외치는구나. 그들이 먼 땅으로 도망하여 이리저리 방황할 때에 그들을 반겨 주는 자가 아무도 없었다.

16여호와께서 그들을 흩어 버리고 다시는 돌보지 않으시니 이방인들이 제사장들을 존경하지 않고 장로들을 대우하지 않는구나.

17우리가 쓸데없는 도움을 바라다가 우리 눈이 쇠약해졌으니 우리를 구원하지 못할 나라에 도움을 기대하였음이라.

18사람들이 우리를 일일이 살피고 있으므로 우리가 거리에 걸어다닐 수 없구나. 우리의 날이 다하고 우리의 종말이 이르렀다.

19우리를 추격하는 자들이 공중의 독수리보다 빨라서 우리가 산으로 도망하여도 그들이 우리를 추격하고 우리가 광야에 숨어도 그들이 거기서 잠복하여 우리를 기다리는구나.

20여호와께서 택하신 자, 곧 우리의 생명과 같은 왕이 그들의 함정에 빠지고 말았네. 그는 우리가 세상의 모든 침략자들로부터 우리를 보호해 줄 것으로 믿었던 자인데 … … .

21우스 땅에 사는 에돔 사람들아, 기뻐하고 즐거워하라. 진노의 잔이 너희에게도 지나갈 것이니 너희가 취하여 벌거벗은 자가 되리라.

22처녀 시온아, 네 죄의 형벌이 끝났다. 주께서 다시는 네가 사로잡혀가지 않게 하시리라. 그러나 에돔아, 주께서 너를 벌하시고 네 죄를 드러내실 것이다.