Maliro 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 3:1-66

1Ine ndine munthu amene ndaona masautso

ndi ndodo ya ukali wake.

2Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa

mu mdima osati mʼkuwala;

3zoonadi anandikantha ndi dzanja lake

mobwerezabwereza tsiku lonse.

4Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga,

ndipo waphwanya mafupa anga.

5Wandizinga ndi kundizungulira

ndi zowawa ndi zolemetsa.

6Wandikhazika mu mdima

ngati amene anafa kale.

7Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe,

wandimanga ndi maunyolo.

8Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo,

amakana pemphero langa.

9Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema;

ndipo wakhotetsa tinjira tanga.

10Wandidikirira ngati chimbalangondo,

wandibisalira ngati mkango.

11Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba,

ndipo wandisiya wopanda thandizo.

12Wakoka uta wake

ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.

13Walasa mtima wanga

ndi mivi ya mʼphodo mwake.

14Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse;

amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.

15Wandidyetsa zowawa

ndipo wandimwetsa ndulu.

16Wathyola mano anga ndi miyala;

wandiviviniza mʼfumbi;

17Wandichotsera mtendere;

ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.

18Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka

ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”

19Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala,

zili ngati zowawa ndi ndulu.

20Ine ndikuzikumbukira bwino izi,

ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.

21Komabe ndimakumbukira zimenezi,

nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.

22Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu,

ndi chifundo chake ndi chosatha.

23Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse;

kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.

24Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse;

motero ndimamuyembekezera.”

25Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye,

kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;

26nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha

Yehova modekha.

27Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli

pamene ali wamngʼono.

28Akhale chete pa yekha,

chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.

29Abise nkhope yake mʼfumbi

mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.

30Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye,

ndipo amuchititse manyazi.

31Chifukwa Ambuye satayiratu

anthu nthawi zonse.

32Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo,

chifukwa chikondi chake ndi chosatha.

33Pakuti sabweretsa masautso mwadala,

kapena zowawa kwa ana a anthu.

34Kuphwanya ndi phazi

a mʼndende onse a mʼdziko,

35kukaniza munthu ufulu wake

pamaso pa Wammwambamwamba,

36kumana munthu chiweruzo cholungama—

kodi Ambuye saona zonsezi?

37Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika

ngati Ambuye sanavomereze?

38Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka

mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?

39Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula

akalangidwa chifukwa cha machimo ake?

40Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu,

ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.

41Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu

kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:

42“Ife tachimwa ndi kuwukira

ndipo inu simunakhululuke.

43“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo

mwatitha mopanda chifundo.

44Mwadzikuta mu mtambo

kotero mapemphero athu sakukufikani.

45Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala

pakati pa mitundu ya anthu.

46“Adani anthu atitsekulira pakamwa.

47Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje,

tapasuka ndi kuwonongedwa.”

48Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe

chifukwa anthu anga akuwonongedwa.

49Misozi idzatsika kosalekeza,

ndipo sidzasiya,

50mpaka Yehova ayangʼane pansi

kuchokera kumwamba ndi kuona.

51Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi

chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.

52Akundisaka ngati mbalame,

amene anali adani anga, popanda chifukwa.

53Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje

ndi kundiponya miyala;

54madzi anamiza mutu wanga

ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.

55Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova,

kuchokera mʼdzenje lozama.

56Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere

kulira kwanga kopempha thandizo.”

57Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani,

ndipo munati, “Usaope.”

58Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga;

munapulumutsa moyo wanga.

59Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira.

Mundiweruzire ndinu!

60Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo,

chiwembu chawo chonse pa ine.

61Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo,

chiwembu chawo chonse pa ine,

62manongʼonongʼo a adani anga

ondiwukira ine tsiku lonse.

63Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira,

akundinyoza mu nyimbo zawo.

64Inu Yehova, muwabwezere chowayenera,

chifukwa cha zimene manja awo achita.

65Phimbani mitima yawo,

ndipo matemberero anu akhale pa iwo!

66Muwalondole mwaukali ndipo

muwawonongeretu pa dziko lapansi.

New International Reader’s Version

Lamentations 3:1-66

1I am a man who has suffered greatly.

The Lord has used the Babylonians

to punish my people.

2He has driven me away. He has made me walk

in darkness instead of light.

3He has turned his powerful hand against me.

He has done it again and again, all day long.

4He has worn out my body.

He has broken my bones.

5He has surrounded me and attacked me.

He has made me suffer bitterly.

He has made things hard for me.

6He has made me live in darkness

like those who are dead and gone.

7He has built walls around me, so I can’t escape.

He has put heavy chains on me.

8I call out and cry for help.

But he won’t listen to me when I pray.

9He has put up a stone wall to block my way.

He has made my paths crooked.

10He has been like a bear waiting to attack me.

He has been like a lion hiding in the bushes.

11He has dragged me off the path.

He has torn me to pieces.

And he has left me helpless.

12He has gotten his bow ready to use.

He has shot his arrows at me.

13The arrows from his bag

have gone through my heart.

14My people laugh at me all the time.

They sing and make fun of me all day long.

15The Lord has made my life bitter.

He has made me suffer bitterly.

16He made me chew stones that broke my teeth.

He has walked all over me in the dust.

17I have lost all hope of ever having any peace.

I’ve forgotten what good times are like.

18So I say, “My glory has faded away.

My hope in the Lord is gone.”

19I remember how I suffered and wandered.

I remember how bitter my life was.

20I remember it very well.

My spirit is very sad deep down inside me.

21But here is something else I remember.

And it gives me hope.

22The Lord loves us very much.

So we haven’t been completely destroyed.

His loving concern never fails.

23His great love is new every morning.

Lord, how faithful you are!

24I say to myself, “The Lord is everything I will ever need.

So I will put my hope in him.”

25The Lord is good to those who put their hope in him.

He is good to those who look to him.

26It is good when people wait quietly

for the Lord to save them.

27It is good for a man to carry a heavy load of suffering

while he is young.

28Let him sit alone and not say anything.

The Lord has placed that load on him.

29Let him bury his face in the dust.

There might still be hope for him.

30Let him turn his cheek toward those who would slap him.

Let him be filled with shame.

31The Lord doesn’t turn his back

on people forever.

32He might bring suffering.

But he will also show loving concern.

How great his faithful love is!

33He doesn’t want to bring pain

or suffering to anyone.

34Every time people crush prisoners under their feet,

the Lord knows all about it.

35When people refuse to give someone what they should,

the Most High God knows it.

36When people don’t treat someone fairly,

the Lord knows it.

37Suppose people order something to happen.

It won’t happen unless the Lord has planned it.

38Troubles and good things alike come to people

because the Most High God has commanded them to come.

39A person who is still alive shouldn’t blame God

when God punishes them for their sins.

40Let’s take a good look at the way we’re living.

Let’s return to the Lord.

41Let’s lift up our hands to God in heaven.

Let’s pray to him with all our hearts.

42Let’s say, “We have sinned.

We’ve refused to obey you.

And you haven’t forgiven us.

43“You have covered yourself with the cloud of your anger.

You have chased us.

You have killed us without pity.

44You have covered yourself with the cloud of your anger.

Our prayers can’t get through to you.

45You have made us become like trash and garbage

among the nations.

46“All our enemies have opened their mouths wide

to swallow us up.

47We are terrified and trapped.

We are broken and destroyed.”

48Streams of tears flow from my eyes.

That’s because my people are destroyed.

49Tears will never stop flowing from my eyes.

My eyes can’t get any rest.

50I’ll weep until the Lord looks down from heaven.

I’ll cry until he notices my tears.

51What I see brings pain to my spirit.

All the women of my city are mourning.

52Those who were my enemies for no reason at all

hunted me down as if I were a bird.

53They tried to end my life

by throwing me into a deep pit.

They threw stones down at me.

54The water rose and covered my head.

I thought I was going to die.

55Lord, I called out to you.

I called out from the bottom of the pit.

56I prayed, “Please don’t close your ears

to my cry for help.”

And you heard my appeal.

57You came near when I called out to you.

You said, “Do not be afraid.”

58Lord, you stood up for me in court.

You saved my life and set me free.

59Lord, you have seen the wrong things

people have done to me.

Stand up for me again!

60You have seen how my enemies

have tried to get even with me.

You know all about their plans against me.

61Lord, you have heard them laugh at me.

You know all about their plans against me.

62You have heard my enemies

whispering among themselves.

They speak against me all day long.

63Just look at them sitting and standing there!

They sing and make fun of me.

64Lord, pay them back.

Punish them for what their hands have done.

65Cover their minds with a veil.

Put a curse on them!

66Lord, get angry with them and hunt them down.

Wipe them off the face of the earth.