Maliro 2 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 2:1-22

1Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni

ndi mtambo wa mkwiyo wake!

Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli

kuchoka kumwamba.

Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso

popondapo mapazi ake.

2Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;

mu mkwiyo wake anagwetsa

malinga a mwana wamkazi wa Yuda.

Anagwetsa pansi mochititsa manyazi

maufumu ndi akalonga ake.

3Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola

nyanga iliyonse ya Israeli.

Anabweza dzanja lake lamanja

pamene mdani anamuyandikira.

Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa

umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.

4Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;

wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,

ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.

Ukali wake ukuyaka ngati moto

pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.

5Ambuye ali ngati mdani;

wawonongeratu Israeli;

wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu

ndipo wawononga malinga ake.

Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira

kwa mwana wamkazi wa Yuda.

6Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;

wawononga malo ake a msonkhano.

Yehova wayiwalitsa Ziyoni

maphwando ake oyikika ndi masabata ake.

Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza

mfumu ndi wansembe.

7Ambuye wakana guwa lake la nsembe

ndipo wasiya malo ake opatulika.

Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu

kwa mdani wake;

adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova

ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.

8Yehova anatsimikiza kugwetsa

makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.

Anawayesa ndi chingwe

ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.

Analiritsa malinga ndi makoma;

onse anawonongeka pamodzi.

9Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;

wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.

Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,

palibenso lamulo,

ndipo aneneri ake sakupeza

masomphenya kuchokera kwa Yehova.

10Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni

akhala chete pansi;

awaza fumbi pa mitu yawo

ndipo avala ziguduli.

Anamwali a Yerusalemu

aweramitsa mitu yawo pansi.

11Maso anga atopa ndi kulira,

ndazunzika mʼmoyo mwanga,

mtima wanga wadzaza ndi chisoni

chifukwa anthu anga akuwonongeka,

chifukwa ana ndi makanda akukomoka

mʼmisewu ya mu mzinda.

12Anawo akufunsa amayi awo kuti,

“Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”

pamene akukomoka ngati anthu olasidwa

mʼmisewu ya mʼmizinda,

pamene miyoyo yawo ikufowoka

mʼmanja mwa amayi awo.

13Ndinganene chiyani za iwe?

Ndingakufanizire ndi chiyani,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?

Kodi ndingakufanizire ndi yani

kuti ndikutonthoze,

iwe namwali wa Ziyoni?

Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,

kodi ndani angakuchiritse?

14Masomphenya a aneneri ako

anali abodza ndi achabechabe.

Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo

poyika poyera mphulupulu zako.

Mauthenga amene anakupatsa

anali achabechabe ndi osocheretsa.

15Onse oyenda mʼnjira yako

akukuwombera mʼmanja;

akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:

“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa

wokongola kotheratu,

chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”

16Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;

iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,

ndipo akuti, “Tamumeza.

Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;

tili ndi moyo kuti tilione.”

17Yehova wachita chimene anakonzeratu;

wakwaniritsa mawu ake,

amene anatsimikiza kale lomwe.

Wakuwononga mopanda chifundo,

walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,

wakweza mphamvu za adani ako.

18Mitima ya anthu

ikufuwulira Ambuye.

Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,

misozi yako itsike ngati mtsinje

usana ndi usiku;

usadzipatse wekha mpumulo,

maso ako asaleke kukhetsa misozi.

19Dzuka, fuwula usiku,

pamene alonda ayamba kulondera;

khuthula mtima wako ngati madzi

pamaso pa Ambuye.

Kweza manja ako kwa Iye

chifukwa cha miyoyo ya ana ako,

amene akukomoka ndi njala

mʼmisewu yonse ya mu mzinda.

20Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:

kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?

Kodi amayi adye ana awo,

amene amawasamalira?

Kodi ansembe ndi aneneri awaphere

mʼmalo opatulika a Ambuye?

21Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi

pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;

anyamata anga ndi anamwali anga

aphedwa ndi lupanga.

Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;

mwawapha mopanda chifundo.

22Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,

chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.

Pa tsiku limene Yehova wakwiya

palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;

mdani wanga wawononga

onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.

Asante Twi Contemporary Bible

Kwadwom 2:1-22

1Sɛdeɛ Awurade de nʼabufuhyeɛ omununkum

akata Ɔbabaa Sion so nie?

Wato Israel animuonyam

firi soro abɛhwe fam;

wankae ne nan ntiasoɔ

wɔ nʼabufuo da no.

2Awurade annya ahummɔborɔ

na wamene Yakob atenaeɛ nyinaa;

nʼabufuhyeɛ mu, wadwiri

Yuda Ɔbabaa aban denden no agu fam.

Wagu nʼahennie ne ne mmapɔmma

ho fi.

3Ɔde abufuhyeɛ atwitwa

Israel mmɛn nyinaa.

Wayi ne banbɔ

wɔ ɛberɛ a atamfoɔ no reba.

Wasɔ wɔ Yakob mu sɛ ogyadɛreɛ

a ɛhye biribiara a atwa ho ahyia.

4Wapoma ne bɛmma te sɛ ɔtamfoɔ;

ne nsa nifa ayɛ krado.

Sɛdeɛ ɔtamfoɔ yɛ no, wakunkum

wɔn a wɔyɛ fɛ wɔ anisoɔ nyinaa;

wahwie nʼabufuhyeɛ sɛ ogya

agu Ɔbabaa Sion ntomadan so.

5Awurade ayɛ sɛ ɔtamfoɔ;

wamene Israel.

Wamene nʼahemfie nyinaa

asɛe nʼabandenden.

Wama awerɛhoɔdie ne agyaadwotwa adɔɔso

ama Yuda Ɔbabaa.

6Wama nʼatenaeɛ ada mpan sɛ turo;

wasɛe ne dwabirem.

Awurade ama Sion werɛ afiri

nʼafahyɛ ne home nna;

wɔ nʼabufuhyeɛ mu no

wabu ɔhene ne ɔsɔfoɔ animtia.

7Awurade apo nʼafɔrebukyia

na wagyae ne kronkronbea mu.

Ɔde nʼahemfie afasuo

ahyɛ nʼatamfoɔ nsa.

Wɔteam wɔ Awurade efie

te sɛ afahyɛ da.

8Awurade sii nʼadwene pi sɛ ɔbɛsɛe

Ɔbabaa Sion ɔfasuo a atwa ne ho ahyia no.

Ɔde susuhoma too ho

na wannyae ɔsɛeɛ no.

Ɔmaa apie ne afasuo dii abooboo;

wɔn nyinaa sɛeɛ.

9Nʼapono amem fam;

wɔn adaban nso, wabubu mu asɛe no.

Ne ɔhene ne ne mmapɔmma, watwa wɔn asuo kɔ amanaman no mu,

mmara nni hɔ bio,

na nʼadiyifoɔ nnnya anisoadehunu a

ɛfiri Awurade hɔ bio.

10Ɔbabaa Sion mpanimfoɔ

tete fam ayɛ komm;

wɔde mfuturo agu wɔn tirim

afirafira ayitoma.

Yerusalem mmabaawa

asisi wɔn tiri ase.

11Mʼani rentumi nnyae nisuteɛ,

me yafunu mu retwa me,

mʼakoma rete atɔ fam,

ɛfiri sɛ wɔasɛe me nkurɔfoɔ,

ɛfiri sɛ mmɔfra ne mmotafowa totɔ piti

wɔ kuropɔn no mmɔntene so.

12Wɔbisa wɔn maamenom sɛ,

“Ɛhe na aduane ne nsã wɔ?”

Ɛberɛ a wɔtotɔ piti sɛ apirafoɔ

wɔ kuropɔn no mmɔntene so,

ɛberɛ a wɔn nkwa resa

wɔ wɔn maamenom abasa so.

13Ɛdeɛn na mɛtumi aka ama woɔ?

Ɛdeɛn ho na mɛtumi de wo atoto,

Ao, Yerusalem Ɔbabaa?

Ɛdeɛn na mɛtumi de asusu woɔ,

de akyekyere wo werɛ,

Ao, Sion Ɔbabaa Bunu?

Wʼapirakuro so sɛ ɛpo.

Hwan na ɔbɛtumi asa ama woɔ?

14Wʼadiyifoɔ anisoadehunu

yɛ atorɔ a ɛho nni mfasoɔ;

wɔanna mo amumuyɛ adi

ansi mo nnommumfa ano.

Nkɔmhyɛ a wɔde maa mo no

yɛ atorɔ ne nnaadaa.

15Wɔn a wɔtwam wo ɛkwan soɔ nyinaa

bobɔ wɔn nsam gu wo so;

wɔdi wo ho fɛ na wɔwoso wɔn tiri

gu Yerusalem Ɔbabaa so ka sɛ,

“Yei ne kuropɔn a na wɔfrɛ no

ahoɔfɛ a ɛdi mu no?

Asase nyinaa anigyedeɛ no nie?”

16Wʼatamfoɔ nyinaa baeɛ wɔn anom

kakraa tia wo;

wɔsere na wɔtwɛre wɔn se

na wɔka sɛ, “Yɛamene no.

Ɛda a na yɛretwɛn no nie;

Yɛatena ase ahunu.”

17Awurade ayɛ deɛ ɔhyehyɛeɛ;

wama nʼasɛm a

ɔhyɛɛ dadaada no aba mu.

Watu wo agu a wanhunu wo mmɔbɔ,

wama ɔtamfoɔ no ani agye

wama wʼatamfoɔ no mmɛn so.

18Nnipa no akoma

su frɛ Awurade.

Ao, Sion Ɔbabaa fasuo,

ma wo nisuo nsene sɛ asubɔnten

awia ne anadwo;

nnye wʼahome

mma wʼani nso nnya ahomeɛ.

19Sɔre, su denden anadwo

ɔdasuom mfitiaseɛ;

hwie wʼakoma mu nsɛm sɛ nsuo

gu Awurade anim.

Ma wo nsa so kyerɛ no

wo mma nkwa enti,

wɔn a ɛkɔm ama wʼatotɔ baha

wɔ mmɔntene so.

20“Hwɛ na dwene ho, Ao, Awurade:

Hwan na wode no afa saa ɛkwan yi so pɛn?

Ɛsɛ sɛ mmaa we wɔn yafunu mma nam anaa,

mma a wɔahwɛ wɔn?

Ɛsɛ sɛ wɔkum ɔsɔfoɔ ne odiyifoɔ

Awurade kronkronbea anaa?

21“Mmɔfra ne mpanin adeda abɔ mu

mfuturo mu wɔ mmɔntene so,

me mmeranteɛ ne mmabaawa

atotɔ wɔ akofena ano.

Wakum wɔn wɔ wʼabufuo da;

wayam wɔn na wannya ahummɔborɔ.

22“Sɛdeɛ wotoo wo nsa frɛ wɔ apontoɔ da no,

saa ara na wofrɛfrɛɛ

amanehunu firi afanan nyinaa tiaa me.

Awurade abufuo da no,

obiara annwane na obiara anka:

wɔn a mehwɛɛ wɔn na metetee wɔn no,

me ɔtamfoɔ adwerɛ wɔn.”