1Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni
ndi mtambo wa mkwiyo wake!
Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli
kuchoka kumwamba.
Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso
popondapo mapazi ake.
2Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;
mu mkwiyo wake anagwetsa
malinga a mwana wamkazi wa Yuda.
Anagwetsa pansi mochititsa manyazi
maufumu ndi akalonga ake.
3Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola
nyanga iliyonse ya Israeli.
Anabweza dzanja lake lamanja
pamene mdani anamuyandikira.
Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa
umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;
wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,
ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.
Ukali wake ukuyaka ngati moto
pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5Ambuye ali ngati mdani;
wawonongeratu Israeli;
wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu
ndipo wawononga malinga ake.
Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira
kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;
wawononga malo ake a msonkhano.
Yehova wayiwalitsa Ziyoni
maphwando ake oyikika ndi masabata ake.
Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza
mfumu ndi wansembe.
7Ambuye wakana guwa lake la nsembe
ndipo wasiya malo ake opatulika.
Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu
kwa mdani wake;
adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova
ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8Yehova anatsimikiza kugwetsa
makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.
Anawayesa ndi chingwe
ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.
Analiritsa malinga ndi makoma;
onse anawonongeka pamodzi.
9Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;
wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.
Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,
palibenso lamulo,
ndipo aneneri ake sakupeza
masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni
akhala chete pansi;
awaza fumbi pa mitu yawo
ndipo avala ziguduli.
Anamwali a Yerusalemu
aweramitsa mitu yawo pansi.
11Maso anga atopa ndi kulira,
ndazunzika mʼmoyo mwanga,
mtima wanga wadzaza ndi chisoni
chifukwa anthu anga akuwonongeka,
chifukwa ana ndi makanda akukomoka
mʼmisewu ya mu mzinda.
12Anawo akufunsa amayi awo kuti,
“Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”
pamene akukomoka ngati anthu olasidwa
mʼmisewu ya mʼmizinda,
pamene miyoyo yawo ikufowoka
mʼmanja mwa amayi awo.
13Ndinganene chiyani za iwe?
Ndingakufanizire ndi chiyani,
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?
Kodi ndingakufanizire ndi yani
kuti ndikutonthoze,
iwe namwali wa Ziyoni?
Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,
kodi ndani angakuchiritse?
14Masomphenya a aneneri ako
anali abodza ndi achabechabe.
Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo
poyika poyera mphulupulu zako.
Mauthenga amene anakupatsa
anali achabechabe ndi osocheretsa.
15Onse oyenda mʼnjira yako
akukuwombera mʼmanja;
akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:
“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa
wokongola kotheratu,
chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;
iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,
ndipo akuti, “Tamumeza.
Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;
tili ndi moyo kuti tilione.”
17Yehova wachita chimene anakonzeratu;
wakwaniritsa mawu ake,
amene anatsimikiza kale lomwe.
Wakuwononga mopanda chifundo,
walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,
wakweza mphamvu za adani ako.
18Mitima ya anthu
ikufuwulira Ambuye.
Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,
misozi yako itsike ngati mtsinje
usana ndi usiku;
usadzipatse wekha mpumulo,
maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19Dzuka, fuwula usiku,
pamene alonda ayamba kulondera;
khuthula mtima wako ngati madzi
pamaso pa Ambuye.
Kweza manja ako kwa Iye
chifukwa cha miyoyo ya ana ako,
amene akukomoka ndi njala
mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:
kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?
Kodi amayi adye ana awo,
amene amawasamalira?
Kodi ansembe ndi aneneri awaphere
mʼmalo opatulika a Ambuye?
21Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi
pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;
anyamata anga ndi anamwali anga
aphedwa ndi lupanga.
Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;
mwawapha mopanda chifundo.
22Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,
chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.
Pa tsiku limene Yehova wakwiya
palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;
mdani wanga wawononga
onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.
1Sɛdeɛ Awurade de nʼabufuhyeɛ omununkum
akata Ɔbabaa Sion so nie?
Wato Israel animuonyam
firi soro abɛhwe fam;
wankae ne nan ntiasoɔ
wɔ nʼabufuo da no.
2Awurade annya ahummɔborɔ
na wamene Yakob atenaeɛ nyinaa;
nʼabufuhyeɛ mu, wadwiri
Yuda Ɔbabaa aban denden no agu fam.
Wagu nʼahennie ne ne mmapɔmma
ho fi.
3Ɔde abufuhyeɛ atwitwa
Israel mmɛn nyinaa.
Wayi ne banbɔ
wɔ ɛberɛ a atamfoɔ no reba.
Wasɔ wɔ Yakob mu sɛ ogyadɛreɛ
a ɛhye biribiara a atwa ho ahyia.
4Wapoma ne bɛmma te sɛ ɔtamfoɔ;
ne nsa nifa ayɛ krado.
Sɛdeɛ ɔtamfoɔ yɛ no, wakunkum
wɔn a wɔyɛ fɛ wɔ anisoɔ nyinaa;
wahwie nʼabufuhyeɛ sɛ ogya
agu Ɔbabaa Sion ntomadan so.
5Awurade ayɛ sɛ ɔtamfoɔ;
wamene Israel.
Wamene nʼahemfie nyinaa
asɛe nʼabandenden.
Wama awerɛhoɔdie ne agyaadwotwa adɔɔso
ama Yuda Ɔbabaa.
6Wama nʼatenaeɛ ada mpan sɛ turo;
wasɛe ne dwabirem.
Awurade ama Sion werɛ afiri
nʼafahyɛ ne home nna;
wɔ nʼabufuhyeɛ mu no
wabu ɔhene ne ɔsɔfoɔ animtia.
7Awurade apo nʼafɔrebukyia
na wagyae ne kronkronbea mu.
Ɔde nʼahemfie afasuo
ahyɛ nʼatamfoɔ nsa.
Wɔteam wɔ Awurade efie
te sɛ afahyɛ da.
8Awurade sii nʼadwene pi sɛ ɔbɛsɛe
Ɔbabaa Sion ɔfasuo a atwa ne ho ahyia no.
Ɔde susuhoma too ho
na wannyae ɔsɛeɛ no.
Ɔmaa apie ne afasuo dii abooboo;
wɔn nyinaa sɛeɛ.
9Nʼapono amem fam;
wɔn adaban nso, wabubu mu asɛe no.
Ne ɔhene ne ne mmapɔmma, watwa wɔn asuo kɔ amanaman no mu,
mmara nni hɔ bio,
na nʼadiyifoɔ nnnya anisoadehunu a
ɛfiri Awurade hɔ bio.
10Ɔbabaa Sion mpanimfoɔ
tete fam ayɛ komm;
wɔde mfuturo agu wɔn tirim
afirafira ayitoma.
Yerusalem mmabaawa
asisi wɔn tiri ase.
11Mʼani rentumi nnyae nisuteɛ,
me yafunu mu retwa me,
mʼakoma rete atɔ fam,
ɛfiri sɛ wɔasɛe me nkurɔfoɔ,
ɛfiri sɛ mmɔfra ne mmotafowa totɔ piti
wɔ kuropɔn no mmɔntene so.
12Wɔbisa wɔn maamenom sɛ,
“Ɛhe na aduane ne nsã wɔ?”
Ɛberɛ a wɔtotɔ piti sɛ apirafoɔ
wɔ kuropɔn no mmɔntene so,
ɛberɛ a wɔn nkwa resa
wɔ wɔn maamenom abasa so.
13Ɛdeɛn na mɛtumi aka ama woɔ?
Ɛdeɛn ho na mɛtumi de wo atoto,
Ao, Yerusalem Ɔbabaa?
Ɛdeɛn na mɛtumi de asusu woɔ,
de akyekyere wo werɛ,
Ao, Sion Ɔbabaa Bunu?
Wʼapirakuro so sɛ ɛpo.
Hwan na ɔbɛtumi asa ama woɔ?
14Wʼadiyifoɔ anisoadehunu
yɛ atorɔ a ɛho nni mfasoɔ;
wɔanna mo amumuyɛ adi
ansi mo nnommumfa ano.
Nkɔmhyɛ a wɔde maa mo no
yɛ atorɔ ne nnaadaa.
15Wɔn a wɔtwam wo ɛkwan soɔ nyinaa
bobɔ wɔn nsam gu wo so;
wɔdi wo ho fɛ na wɔwoso wɔn tiri
gu Yerusalem Ɔbabaa so ka sɛ,
“Yei ne kuropɔn a na wɔfrɛ no
ahoɔfɛ a ɛdi mu no?
Asase nyinaa anigyedeɛ no nie?”
16Wʼatamfoɔ nyinaa baeɛ wɔn anom
kakraa tia wo;
wɔsere na wɔtwɛre wɔn se
na wɔka sɛ, “Yɛamene no.
Ɛda a na yɛretwɛn no nie;
Yɛatena ase ahunu.”
17Awurade ayɛ deɛ ɔhyehyɛeɛ;
wama nʼasɛm a
ɔhyɛɛ dadaada no aba mu.
Watu wo agu a wanhunu wo mmɔbɔ,
wama ɔtamfoɔ no ani agye
wama wʼatamfoɔ no mmɛn so.
18Nnipa no akoma
su frɛ Awurade.
Ao, Sion Ɔbabaa fasuo,
ma wo nisuo nsene sɛ asubɔnten
awia ne anadwo;
nnye wʼahome
mma wʼani nso nnya ahomeɛ.
19Sɔre, su denden anadwo
ɔdasuom mfitiaseɛ;
hwie wʼakoma mu nsɛm sɛ nsuo
gu Awurade anim.
Ma wo nsa so kyerɛ no
wo mma nkwa enti,
wɔn a ɛkɔm ama wʼatotɔ baha
wɔ mmɔntene so.
20“Hwɛ na dwene ho, Ao, Awurade:
Hwan na wode no afa saa ɛkwan yi so pɛn?
Ɛsɛ sɛ mmaa we wɔn yafunu mma nam anaa,
mma a wɔahwɛ wɔn?
Ɛsɛ sɛ wɔkum ɔsɔfoɔ ne odiyifoɔ
wɔ Awurade kronkronbea anaa?
21“Mmɔfra ne mpanin adeda abɔ mu
mfuturo mu wɔ mmɔntene so,
me mmeranteɛ ne mmabaawa
atotɔ wɔ akofena ano.
Wakum wɔn wɔ wʼabufuo da;
wayam wɔn na wannya ahummɔborɔ.
22“Sɛdeɛ wotoo wo nsa frɛ wɔ apontoɔ da no,
saa ara na wofrɛfrɛɛ
amanehunu firi afanan nyinaa tiaa me.
Awurade abufuo da no,
obiara annwane na obiara anka:
wɔn a mehwɛɛ wɔn na metetee wɔn no,
me ɔtamfoɔ adwerɛ wɔn.”