Malaki 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 1:1-14

1Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.

Ndamukonda Yakobo, Ndamuda Esau

2Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’ ”

Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo, 3koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”

4Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.”

Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya. 5Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’

Nsembe Zosayenera

6“Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa.

“Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’

7“Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe.

“Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’

“Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka. 8Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

9“Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

10“Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu. 11Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

12“Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’ 13Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova. 14“Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’ ”

Persian Contemporary Bible

ملاكی 1:1-14

1اين است پيام خداوند كه بوسيلهٔ ملاكی نبی به اسرائيل داده شد.

محبت خداوند نسبت به اسرائيل

2‏-3خداوند می‌فرمايد: «من شما را هميشه دوست داشته‌ام!»

ولی شما می‌گوييد: «تو چگونه ما را دوست داشته‌ای؟»

خداوند می‌فرمايد: «من جد شما يعقوب را محبت نمودم، هر چند لايق محبت نبود، و به اين ترتيب نشان دادم كه شما را دوست دارم، ولی عيسو را كه برادرش بود رد كردم و سرزمين كوهستانی او را ويران نمودم و آن را جای شغالهای بيابان ساختم.»

4شايد ادومی‌ها كه فرزندان عيسو هستند بگويند: «ما برمی‌گرديم و سرزمين ويران خود را دوباره آباد می‌كنيم.» ولی خداوند قادر متعال می‌گويد: «اگر آن را آباد كنند من دوباره ويرانش خواهم كرد. سرزمين آنها ”سرزمين شرارت“ خوانده خواهد شد و مردمشان به ”قومی كه خداوند آنها را هرگز نمی‌بخشد“، مشهور خواهند گرديد.»

5ای قوم اسرائيل، وقتی با چشمان خود آنچه را كه خداوند در سراسر دنيا انجام می‌دهد ببينيد، خواهيد گفت: «براستی كه قدرت عظيم خداوند در آن سوس مرزهای ما نيز ديده می‌شود.»

سرزنش كاهنان

6خداوند قادر متعال به كاهنان می‌فرمايد: «پسر، پدر خود را و غلام، ارباب خويش را احترام می‌كند. پس اگر من پدر شما هستم احترام من كجاست؟ و اگر من ارباب شما هستم، حرمت من كجاست؟ شما نام مرا بی‌حرمت كرده‌ايد. می‌گوييد: ”ما چگونه نام تو را بی‌حرمت كرده‌ايم؟“ 7شما هنگامی نام مرا بی‌حرمت می‌كنيد كه قربانیهای ناپاک روی قربانگاه من می‌گذاريد. بلی، با اين كارتان مرا تحقير می‌كنيد. 8حيوانات لنگ و كور و بيمار را برای من قربانی می‌كنيد. آيا اين قبيح نيست؟ اگر آن را به حاكم خود هديه می‌كرديد آيا او آن را می‌پسنديد و از شما راضی می‌شد؟

9«دعا می‌كنيد و می‌گوييد: ”خداوندا، بر ما رحم كن! خداوندا، لطف تو شامل حال ما بشود!“ ولی وقتی كه چنين هدايايی می‌آوريد، چطور انتظار داريد دعای شما را اجابت كنم؟»

10خداوند قادر متعال می‌فرمايد: «ای كاش يكی از شما كاهنان، درها را می‌بست تا چنين هدايايی روی قربانگاه من گذاشته نشود. از شما راضی نيستم و قربانیهای شما را نمی‌پذيرم.

11«نام من در سراسر جهان بوسيلهٔ مردم غيريهود مورد احترام قرار خواهد گرفت و آنها به احترام نام من بخور خوشبو خواهند سوزانيد و قربانیهای پاک تقديم خواهند كرد. آری آنها نام مرا با احترام فراوان ياد خواهند كرد. 12ولی شما نام مرا بی‌حرمت می‌سازيد و قربانگاه مرا نجس می‌كنيد، زيرا حيوانات معيوب بر آن می‌گذاريد. 13می‌گوييد: ”خدمت كردن به خداوند كار مشكل و خسته كننده‌ای است“، و از دستورات من سرپيچی می‌كنيد. حيوانات دزديده شده، لنگ و بيمار برای من قربانی می‌كنيد. آيا فكر می‌كنيد من آنها را از دست شما قبول خواهم كرد؟ 14لعنت بر كسی كه بخواهد مرا فريب دهد و با آنكه نذر كرده قوچ سالمی از گلهٔ خود هديه كند، حيوان معيوبی برای من قربانی نمايد. من پادشاه عظيم هستم و مردم دنيا بايد اسم مرا با ترس و احترام ياد كنند.»