Machitidwe a Atumwi 3 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 3:1-26

Petro Achiritsa Wolumala Miyendo

1Tsiku lina Petro ndi Yohane ankapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera nthawi ya 3 koloko masana. 2Ndipo munthu wolumala chibadwire ankanyamulidwa tsiku ndi tsiku kukayikidwa pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola kuti azikapempha amene amalowa ku bwalo la Nyumbayo. 3Ataona Petro ndi Yohane ali pafupi kulowa anawapempha ndalama. 4Iwo anamuyangʼanitsitsa iye. Kenaka Petro anati, “Tiyangʼane!” 5Munthuyo anawayangʼanitsitsa kuyembekezera kuti alandira kanthu kuchokera kwa iwo.

6Petro anati kwa iye, “Ine ndilibe siliva kapena golide, koma chimene ndili nacho ndikupatsa. Mʼdzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti, yenda.” 7Ndipo anamugwira dzanja lamanja, namuthandiza kuti ayimirire ndipo nthawi yomweyo mapazi ake ndi akakolo ake analimba. 8Iye analumpha ndi kuyamba kuyenda. Kenaka analowa nawo pamodzi mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, akuyenda ndi kulumpha ndiponso kuyamika Mulungu. 9Anthu onse atamuona akuyenda ndiponso kuyamika Mulungu, 10anamuzindikira kuti ndi yemwe uja ankakhala pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola, ndipo anazizwa ndi kudabwa ndi zimene zinamuchitikira.

Petro Ayankhula kwa Anthu

11Wopempha uja akuyenda pamodzi ndi Petro ndi Yohane, anthu onse anadabwa ndipo anawathamangira iwo kumalo wotchedwa Khonde la Solomoni. 12Petro ataona zimenezi anawawuza kuti, “Inu Aisraeli, chifukwa chiyani mukudabwa ndi zimene zachitikazi? Bwanji mukuyangʼana ife ngati kuti tamuyendetsa munthuyu ndi mphamvu yathu kapena chifukwa cha kupembedza kwathu? 13Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, Mulungu wa makolo athu, wamulemekeza mtumiki wake Yesu. Amene inu munamukana pamaso pa Pilato ndi kumupereka Iye kuti aphedwe, ngakhale kuti Pilato anafuna kuti amumasule. 14Koma inu munamukana Woyera ndi Wolungamayo ndipo munapempha kuti akumasulireni munthu wakupha anthu. 15Inu munapha mwini moyo, koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Ife ndife mboni za zimenezi. 16Mwachikhulupiriro mʼdzina la Yesu, munthu uyu amene mukumuona ndi kumudziwa analimbikitsidwa. Mʼdzina la Yesu ndi chikhulupiriro chimene chili mwa iye chamuchiritsa kwathunthu, monga nonse mukuona.

17“Tsopano abale ine ndikudziwa kuti inu munachita zimenezi mosadziwa, monga momwenso anachitira atsogoleri anu. 18Koma umu ndi mmene Mulungu anakwaniritsira zimene zinanenedwa kale ndi aneneri onse, kuti Khristu adzamva zowawa. 19Chifukwa chake, lapani, bwererani kwa Mulungu, kuti machimo anu afafanizidwe, kuti nthawi ya kutsitsimuka ibwere kuchokera kwa Ambuye, 20ndi kuti Iye atumize Yesu Khristu amene anasankhidwa chifukwa cha inu. 21Iye ayenera kukhalabe kumwamba mpaka nthawi ya kukonzanso zinthu zonse monga Mulungu analonjeza kale kudzera mwa aneneri ake oyera mtima. 22Pakuti Mose anati, ‘Ambuye Mulungu wanu adzakuukitsirani mneneri monga ine kuchokera pakati pa anthu anu; mumvere zonse zimene iye akuwuzeni. 23Aliyense amene sadzamvera mawu a mneneriyo, adzayenera kuchotsedwa pakati pa abale ake.’

24“Ndipo aneneri onse ambiri amene anayankhula kuyambira Samueli, ananeneratu za masiku ano. 25Inu ndinu ana a aneneri ndiponso ana apangano limene Mulungu anachita ndi makolo anu. Iye anati kwa Abrahamu, ‘Anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako.’ 26Pamene Mulungu anaukitsa mtumiki wake, anamutuma Iye poyamba kwa inu kuti akudalitseni pobweza aliyense wa inu ku zoyipa zake.”

Knijga O Kristu

Djela Apostolska 3:1-26

Petar iscjeljuje hromog čovjeka

1Dok su Petar i Ivan jednoga popodneva išli u Hram na molitveni sastanak koji se održavao u tri ure,3:1 U grčkome: na molitvu u devetu uru. 2naiđu neki ljudi noseći čovjeka hroma od rođenja, kojega su svaki dan donosili pred hramska vrata zvana Divna da prosi milostinju od ljudi koji ulaze u Hram. 3Kad ugleda Petra i Ivana kako ulaze u Hram, zamoli ih za milostinju.

4Petar i Ivan prodorno ga pogledaju. “Pogledaj nas!” reče mu Petar. 5Hromi ih je čovjek molećivo gledao očekujući milostinju. 6Ali Petar mu reče: “Nemam novca, ni srebrna ni zlatna. Ali dajem ti što imam: u ime Isusa Krista Nazarećanina, ustani i hodaj!”

7Uhvati čovjeka za desnu ruku i podigne ga. Čovjeku smjesta ojačaju noge i gležnjevi. 8On skoči, uspravi se i počne hodati. Uđe s njima u Hram hodajući, poskakujući i slaveći Boga.

9Svi su ga vidjeli kako hoda i slavi Boga. 10Shvatili su da je to isti čovjek koji je na Divnim vratima prosio milostinju i zaprepastili su se, gotovo izbezumili zbog toga što se s njim dogodilo. 11On se pak držao Petra i Ivana koji su bili u Salomonovu trijemu. Zato svi nagrnu onamo.

Petar propovijeda u Hramu

12Kad je to vidio Petar, reče ljudima: “Što se čudite ovomu, Izraelci? I što gledate u nas, kao da smo mi svojom snagom ili pobožnošću učinili da ovaj čovjek prohoda! 13Učinio je to Abrahamov, Izakov i Jakovljev Bog, Bog naših predaka, i tako proslavio svojega slugu Isusa. A vi ste toga Isusa predali da ga uhite i odrekli ste ga se pred Pilatom kad ga je već odlučio osloboditi. 14Odrekli ste se Sveca i Pravednika, a namolili ste da vam oslobode ubojicu. 15Ubili ste začetnika života, ali Bog ga je uskrisio od mrtvih. Mi smo tomu svjedoci.

16Isusovo je ime iscijelilo ovoga čovjeka, a znate da je bio hrom. Vjera u Isusovo ime vratila mu je potpuno zdravlje naočigled svih vas.

17Braćo, znam da ste s Isusom tako postupili zbog neznanja, kao i vaši poglavari. 18Ali Bog je tako ispunio ono što su proroci prorekli o Mesiji: da će pretrpjeti sve to. 19Pokajte se dakle za grijehe i obratite se Bogu pa će vam on izbrisati grijehe 20i poslati vam vrijeme okrepe: unaprijed vam namijenjenoga Mesiju Isusa. 21On mora ostati u nebu sve dok ne dođe vrijeme svekolike obnove koju je Bog odavno obećao kroz svete proroke. 22Mojsije je rekao:

‘Gospodin, vaš Bog, podignut će vam proroka

poput mene iz vašega vlastitog naroda.

Dobro slušajte sve

što vam on kaže!

23A tko god ne bude slušao tog proroka,

neka se iskorijeni iz naroda!’

24Još od Samuela, svi su proroci navijestili ovo što se sada događa. 25Vi ste djeca tih proroka i Saveza koji je Bog sklopio s vašim precima. Bog je rekao Abrahamu:

‘Tvoje će potomstvo biti na blagoslov

svim narodima na zemlji.’3:25 Postanak 22:18.

26Bog je podignuo svojega slugu i najprije ga je poslao da vas blagoslovi—da se svatko od vas obrati od svojih opačina.”