Machitidwe a Atumwi 23 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 23:1-35

1Paulo anayangʼanitsitsa anthu a Bwalo Lalikulu nati, “Abale anga, ndakhala ndi chikumbumtima chabwino pamaso pa Mulungu mpaka lero lino.” 2Chifukwa cha mawu amenewa, mkulu wa ansembe Ananiya analamulira amene anali pafupi ndi Paulo kuti amumenye pakamwa. 3Pamenepo Paulo anamuwuza kuti, “Mulungu adzakukantha, iwe munthu wachiphamaso! Wakhala pamenepo kuti undiweruze ine monga mwalamulo, koma iweyo ukuphwanya lamulolo polamulira kuti andimenye!”

4Anthu amene anayimirira pafupi ndi Paulo anati, “Bwanji ukunyoza mkulu wa ansembe wa Mulungu?”

5Paulo anayankha nati, “Abale, ine sindinazindikire kuti ndi mkulu wa ansembe; pakuti kunalembedwa kuti, ‘Usayankhule zoyipa kwa mtsogoleri wa anthu ako.’ ”

6Paulo atazindikira kuti ena mwa iwo anali Asaduki ndiponso ena anali Afarisi, anafuwula mʼbwalo muja kuti, “Abale anga, ine ndine Mfarisi, mwana wa Mfarisi. Ndikuweruzidwa chifukwa cha chiyembekezo cha kuuka kwa akufa.” 7Iye atanena zimenezi, mkangano unabuka pakati pa Afarisi ndi Asaduki mpaka anthu kugawikana. 8Asaduki amati kulibe kuuka kwa akufa, kulibenso ngakhale angelo kapena mizimu, koma Afarisi amakhulupirira zonsezi.

9Panali phokoso lalikulu, ndipo aphunzitsi ena amalamulo amene anali a gulu la Afarisi anayimirira natsutsa kwambiri. Iwo anati, “Ife sitikupeza cholakwa ndi munthu uyu, chifukwa mwina ndi mzimu kapena mngelo amene wayankhula naye.” 10Mkangano unakula kwambiri kotero kuti mkulu wa asilikali anachita mantha kuti mwina anthu angakhadzule Paulo. Iye analamulira asilikali ake apite kukamuchotsa pakati pawo mwamphamvu ndi kubwera naye ku malo a asilikaliwo.

11Usiku omwewo Ambuye anayimirira pambali pa Paulo nati, “Limba mtima! Monga wandichitira Ine umboni mu Yerusalemu, moteronso uyenera kundichitira umboni ku Roma.”

Ayuda Achita Chiwembu Paulo

12Kutacha Ayuda ena anakonza chiwembu ndipo analumbira kuti sadya kapena kumwa mpaka atapha Paulo. 13Anthu amene anakonza chiwembuchi analipo makumi anayi. 14Iwo anapita kwa akulu a ansembe ndi akuluakulu a Ayuda nakawawuza kuti, “Ife talumbira kolimba kuti sitidya kalikonse mpaka titapha Paulo. 15Tsopano inu pamodzi ndi akuluakulu a Bwalo Lalikulu mupemphe mkulu wa asilikali kuti akubweretsereni Paulo ngati kuti mukufuna kudziwa bwino za mlandu wake. Ife takonzeka kudzamupha asanafike kumeneko.”

16Koma mwana wa mlongo wake wa Paulo atamva za chiwembuchi, anapita ku malo a asilikali aja namufotokozera Paulo.

17Paulo anayitana mmodzi wa wolamulira asilikali 100 aja, namuwuza kuti, “Pita naye mnyamatayu kwa mkulu wa asilikali. Iyeyu ali ndi mawu oti akamuwuze.” 18Anamutengadi mnyamatayo napita naye kwa mkulu wa asilikali uja, nati, “Wamʼndende uja Paulo anandiyitana, nandipempha kuti ndibweretse mnyamatayu kwa inu chifukwa ali ndi kanthu koti akuwuzeni.”

19Mkulu wa asilikali uja anagwira dzanja mnyamatayo napita naye paseli ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna kuti undiwuze chiyani?”

20Mnyamatayo anati, “Ayuda agwirizana zoti akupempheni kuti mawa mubwere ndi Paulo ku Bwalo Lalikulu, ngati kuti akufuna kudziwa bwino za iye. 21Inu musawamvere, chifukwa pali anthu opitirira makumi anayi amene akumudikirira pa njira. Iwo alumbira kuti sadya kapena kumwa mpaka atapha Paulo. Panopa ndi okonzeka kale, akungodikira kuti muwavomere pempho lawo.”

22Mkulu wa asilikaliyo anawuza mnyamatayo kuti apite koma anamuchenjeza kuti, “Usawuze munthu aliyense kuti wandifotokozera zimenezi.”

Paulo Apita ku Kaisareya

23Kenaka mkulu wa asilikaliyo anayitana awiri a asilikali olamulira asilikali 100 nawalamula kuti, “Uzani asilikali 200, asilikali 70 okwera pa akavalo ndi 200 onyamula mikondo kuti akonzeke kupita ku Kaisareya usiku omwe uno nthawi ya 9 koloko. 24Mumukonzerenso Paulo akavalo woti akwerepo kuti akafike bwino kwa bwanamkubwa Felike.”

25Iye analemba kalata iyi:

26Ine Klaudiyo Lusiya,

Kwa wolemekezeka, bwanamkubwa Felike:

Ndikupereka moni.

27Munthuyo Ayuda anamugwira ndipo anali pafupi kumupha, koma ine ndinapita ndi asilikali nʼkukamulanditsa pakuti ndinamva kuti ndi nzika ya Chiroma. 28Ndinkafuna kudziwa mlandu umene anapalamula, choncho ndinapita naye ku Bwalo lawo Lalikulu. 29Ine ndinapeza kuti amamuyimba mlandu wa nkhani ya malamulo awo, koma panalibe mlandu woyenera kumuphera kapena kumuyika mʼndende. 30Nditawuzidwa kuti amukonzera chiwembu munthuyu, ine ndamutumiza kwa inu msanga. Ine ndalamulanso amene akumuyimba mlanduwo kuti abwere kwa inu kudzafotokoza nkhaniyo.

31Pamenepo asilikali aja anatenga Paulo monga anawalamulira napita naye ku Antipatri usiku. 32Mmawa mwake iwo anabwerera ku malo a asilikali nasiya okwera pa akavalo kuti apitirire ndi Paulo. 33Asilikali okwera pa akavalowo atafika ku Kaisareya anapereka kalatayo kwa bwanamkubwa, namuperekanso Paulo. 34Bwanamkubwayo anawerenga kalatayo ndipo anamufunsa Paulo za dera limene amachokera. Atazindikira kuti amachokera ku Kilikiya, 35iye anati, “Ndidzamva mlandu wako okuyimba mlandu akabwera kuno.” Ndipo analamulira kuti asilikali adzimulondera Paulo ku nyumba ya mfumu Herode.

Knijga O Kristu

Djela Apostolska 23:1-35

1Pavao se zagleda u vijećnike i reče: “Braćo, sve do danas sam pred Bogom živio posve mirne savjesti.”

2Nato veliki svećenik Ananija zapovjedi onima do Pavla da ga udare po ustima. 3“Udarit će tebe Bog, zidu obijeljeni! Sjediš tu da me sudiš po Zakonu, a sam ga kršiš i zapovijedaš da me tuku!”

4Nazočni rekoše Pavlu: “Zar tako grdiš Božjega velikog svećenika?”

5“Nisam znao, braćo, da je veliki svećenik”, odvrati Pavao. “Jer u Svetome pismu piše: ‘Ne psuj poglavara svojega naroda.’”23:5 Izlazak 22:7.

6Pavao je znao da su neki članovi Velikoga vijeća saduceji, a neki farizeji, pa poviče: “Braćo, ja sam farizej i preci su mi farizeji! Sudi mi se zbog nade u uskrsnuće mrtvih!”

7Nato izbije svađa među farizejima i saducejima i mnoštvo se podijeli. 8Saduceji, naime, kažu da nema ni uskrsnuća, ni anđela, ni duhova, a farizeji u sve to vjeruju. 9Nastane silna graja. Neki pismoznanci iz farizejske sljedbe ustanu u Pavlovu obranu žestoko prosvjedujući: “Ne nalazimo da je taj čovjek počinio ikakvo zlo! A što ako mu je govorio duh ili anđeo?” 10Nastane tako velika svađa da se zapovjednik prestrašio da Pavla ne rastrgaju. Zapovjedi zato da vojnici siđu po njega. Oni ga otrgnu iz svjetine i odvedu natrag u vojarnu.

11Te noći Gospodin pristupi Pavlu i reče mu: “Samo hrabro, Pavle! Kao što si za mene posvjedočio ovdje u Jeruzalemu, tako trebaš svjedočiti i u Rimu.”

Zavjera protiv Pavla

12Kad se razdanilo, Židovi skuju urotu i zakunu se da neće ni jesti ni piti dok ne ubiju Pavla. 13Bilo ih je više od četrdesetorice. 14Odu zatim kazati velikim svećenicima i starješinama: “Zakleli smo se da nećemo jesti ni piti dok ne ubijemo Pavla. 15Zato vi sada skupa s Vijećem zamolite zapovjednika da ga opet dovedu u Vijeće. Recite da želite pobliže razmotriti njegov slučaj. A mi ćemo ga pogubiti na putu ovamo.”

16Ali Pavlov nećak, sin njegove sestre, dočuje za tu zavjeru pa ode u vojarnu dojaviti Pavlu. 17Pavao pozove nekog stotnika i reče mu: “Odvedi ovoga mladića k zapovjedniku. Ima mu nešto važno reći.”

18Stotnik ga odvede i reče zapovjedniku: “Zatvorenik Pavao pozvao me i zamolio da ovoga mladića dovedem k tebi jer ti ima nešto reći.”

19Zapovjednik ga uhvati za ruku i povede u stranu te ga upita: “Što mi želiš reći?”

20“Neki su se Židovi dogovorili da te sutra zamole da dovedeš Pavla u Vijeće pretvarajući se da žele pomnjivije ispitati njegov slučaj. 21Ne čini to! Čekat će ga u zasjedi više od četrdesetero ljudi koji su se zakleli da neće ni jesti ni piti dok ga ne ubiju. Već su spremni i samo čekaju tvoj pristanak.”

22Zapovjednik otpusti mladića i zapovjedi mu: “Nikomu ne reci da si mi to javio.”

Pavla šalju u Cezareju

23Dozove zatim dva stotnika i reče im: “Priredite dvjesto vojnika, sedamdeset konjanika i dvjesto strijelaca da večeras po devetoj uri23:23 U grčkome: nakon treće ure noću. pođu u Cezareju. 24Pripravite Pavlu konje za jahanje te ga živa i zdrava odvedite upravitelju Feliksu.” 25Napiše zatim pismo upravitelju:

26Od Klaudija Lizijavrlome upravitelju Feliksu. Pozdravljam vas!

27Ovoga su čovjeka uhvatili Židovi i umalo ga ubili, kad sam pritrčao s vojnicima. Doznavši da je rimski građanin, sklonio sam ga od njih na sigurno. 28Odveo sam ga zatim pred njihovo Vijeće da doznam što je skrivio. 29Utvrdio sam da ga optužuju za nešto prijeporno glede njihova vjerskoga zakona—ali nije skrivio ništa što bi zasluživalo da ga se kazni smrću ili zatvorom. 30Javili su mi da su protiv njega skovali urotu. Šaljem ga zato tebi, a njegove tužitelje uputio sam da tužbu iznesu pred tobom.

31Te noći vojnici, prema zapovijedi, povedu Pavla u Antipatridu. 32Sutradan se vrate u vojarnu ostavivši konjanike da ga odvedu dalje. 33Kad su oni pak s njim stigli u Cezareju, uruče upravitelju pismo i privedu Pavla pred njega. 34Upravitelj pročita pismo te zapita Pavla iz koje je pokrajine. “Iz Cilicije”, odgovori Pavao.

35“Saslušat ću te kad stignu tvoji tužitelji”, reče mu i zapovjedi da ga čuvaju u Herodovoj palači.