Machitidwe a Atumwi 22 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 22:1-30

1Iye anati, “Inu abale anga ndi makolo anga, tamvani mawu akudziteteza kwanga.” 2Atamva iye akuyankhula Chihebri, anakhala chete.

Kenaka Paulo anati, 3“Ine ndine Myuda, wobadwira ku Tarisisi wa ku Kilikiya, koma ndinaleredwa mu mzinda muno, ndinaphunzitsidwa mwatsatanetsatane kusunga malamulo a makolo athu ndi Gamalieli ndipo ndinali wodzipereka pa za Mulungu monga mmene inu mulili lero. 4Ine ndinkazunza anthu otsatira Njirayi mpaka kuwapha. Ndinkagwira amuna ndi amayi ndi kuwayika mʼndende. 5Mkulu wa ansembe ndiponso akuluakulu a Ayuda angathe kundichitira umboni. Iwowa anandipatsa makalata opita nawo kwa abale awo ku Damasiko. Ndipo ndinapita kumeneko kuti ndikawagwire anthu amenewa ndi kubwera nawo ku Yerusalemu kuti adzalangidwe.

6“Nthawi ya masana, nditayandikira ku Damasiko, mwadzidzidzi kuwala kwakukulu kochokera kumwamba kunandizungulira. 7Ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akuti, ‘Saulo! Saulo! Ukundizunziranji?’ ”

8Ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?”

Iye anayankha kuti, “Ndine Yesu wa ku Nazareti, amene iwe ukumuzunza.” 9Anzanga a paulendo anaona kuwalako, koma sanamve mawuwo, a Iye amene amayankhula nane.

10Ine ndinafunsa kuti, “Kodi ndichite chiyani Ambuye?”

Ambuye anati, “Imirira ndipo pita ku Damasiko. Kumeneko adzakuwuza zonse zimene ukuyenera kuchita.” 11Anzanga anandigwira dzanja kupita nane ku Damasiko, popeza kuwala kunja kunandichititsa khungu.

12“Munthu wina dzina lake Hananiya anabwera kudzandiona. Iyeyu anali munthu woopa Mulungu ndi wosunga Malamulo. Ayuda onse okhala kumeneko amamupatsa ulemu waukulu. 13Iye anayimirira pafupi nane nati, ‘Mʼbale Saulo, penyanso!’ Ndipo nthawi yomweyo ndinapenya ndikumuona iyeyo.

14“Ndipo iye anati, ‘Mulungu wa makolo athu wakusankha iwe kuti udziwe chifuniro chake ndi kuona Wolungamayo ndi kumva mawu ochokera pakamwa pake. 15Iwe udzakhala mboni yake kwa anthu onse pa zimene waziona ndi kuzimva. 16Ndipo tsopano ukudikira chiyani? Dzuka ndi kutama dzina la Ambuye mopemba, ubatizidwe ndi kuchotsa machimo ako.’

17“Nditabwerera ku Yerusalemu, ndikupemphera mʼNyumba ya Mulungu, ndinachita ngati ndakomoka. 18Ndinaona Ambuye akundiwuza kuti, ‘Fulumira! Tuluka mu Yerusalemu msangamsanga, chifukwa anthuwa sadzavomereza umboni wako wonena za Ine.’ ”

19Ine ndinayankha Ambuye kuti, “Anthu awa akudziwa kuti ine ndinkapita ku sunagoge iliyonse ndipo ndinkawaponya mʼndende ndi kuwakwapula amene ankakhulupirira inu. 20Ndipo pamene ankapha Stefano, ine ndinali pomwepo kuvomereza ndi kusunga zovala za amene amamupha.”

21Pamenepo Ambuye anandiwuza kuti, “Nyamuka; Ine ndidzakutuma kutali kwa anthu a mitundu ina.”

Paulo Nzika ya Chiroma

22Gulu la anthu linamvetsera mawu a Paulo mpaka pamene ananena izi, kenaka anakweza mawu awo nafuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi! Ngosayenera kukhala moyo!”

23Akufuwula ndi kuponya zovala zawo ndi kuwaza fumbi kumwamba, 24mkulu wa asilikali analamulira kuti amutenge Paulo kupita naye ku malo a asilikali. Iye analamula kuti Paulo akwapulidwe kwambiri ndi kumufunsa kuti apeze chimene anthu ankafuwulira chotere. 25Atamumanga kuti amukwapule, Paulo anati kwa msilikali wolamulira asilikali 100 amene anayima pamenepo, “Kodi malamulo amalola kukwapula nzika ya Chiroma imene sinapezedwe yolakwa?”

26Wolamulira asilikali 100 uja atamva zimenezi, anapita kwa mkulu wa asilikali ndi kumufotokozera. Iye anafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani ndi munthuyu amene ndi nzika ya Chiroma?”

27Mkulu wa asilikali uja anapita kwa Paulo ndipo anamufunsa kuti, “Tandiwuze, kodi ndiwe nzika ya Chiroma?”

Paulo anayankha kuti, “Inde.”

28Kenaka mkulu wa asilikaliyo anati, “Ine ndinapereka ndalama zambiri kuti ndikhale nzika.”

Paulo anayankha kuti, “Koma ine ndinabadwa nzika.”

29Iwo amene anati amufunse analeka nthawi yomweyo. Mkulu wa asilikali uja anachita mantha atazindikira kuti wamanga Paulo amene ndi nzika ya Chiroma.

Paulo ku Bwalo Lalikulu la Ayuda

30Mmawa mwake, mkulu wa asilikali pofuna kupeza chifukwa chenicheni chimene Ayuda amamunenera Paulo, anamumasula ndipo analamula kuti akulu a ansembe ndi onse akuluakulu a Bwalo Lalikulu asonkhane. Ndipo iye anabweretsa Paulo namuyimiritsa patsogolo pawo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Деяния 22:1-30

1– Братья и отцы, разрешите мне высказаться в свою защиту.

2Когда они услышали, что он говорит на языке иудеев, то вовсе утихли. И он сказал:

3– Я иудей, уроженец Тарса в Киликии, но воспитывался я в этом городе у Гамалиила и был в точности научен Закону наших отцов. Я ревнитель дела Аллаха, как и каждый из вас сегодня. 4Я преследовал и мучил до смерти последователей Пути Исы, арестовывал мужчин и женщин и отправлял их в темницы. 5Свидетели тому – верховный священнослужитель и весь Совет старейшин. Я даже получил от них письма к соплеменникам в Дамаске и отправился туда, чтобы арестовать там всех последователей Исы и привести их в Иерусалим для наказания.

6По пути, когда я уже подходил к Дамаску, около полудня меня вдруг озарил ослепительный свет с неба. 7Я упал на землю и услышал голос, который говорил мне: «Шаул! Шаул! Зачем ты преследуешь Меня?» 8Я спросил: «Кто Ты, Владыка?» Он ответил: «Я Иса из Назарета, Которого ты преследуешь». 9Мои спутники видели свет, но того, что говорил мне голос, они не поняли. 10Я спросил: «Повелитель, что мне делать?» Повелитель ответил: «Встань и иди в Дамаск. Там тебе скажут всё, что тебе предстоит сделать». 11Мои спутники за руку привели меня в Дамаск, так как я был ослеплён сиянием этого света.

12Там ко мне пришёл человек по имени Анания, тщательно соблюдающий Закон и уважаемый всеми местными иудеями. 13Он подошёл ко мне и, встав рядом, сказал: «Брат Шаул, прозри!» И в тот же момент я прозрел и увидел этого человека. 14Он сказал: «Бог наших предков избрал тебя, чтобы ты узнал Его волю, увидел Праведного и услышал голос из Его уст. 15Ты будешь для всех людей свидетелем того, что ты видел и слышал. 16Не медли! Вставай, пройди обряд погружения в воду22:16 Или: «обряд омовения». и смой свои грехи, призвав Его имя».

17Потом я возвратился в Иерусалим, и когда я молился в храме, мне было видение. 18Я увидел Повелителя, Который говорил мне: «Скорее выйди из Иерусалима, потому что здесь не примут твоего свидетельства обо Мне». 19Я ответил: «Повелитель, эти люди знают, что я ходил из одного молитвенного дома иудеев в другой, чтобы арестовывать и избивать тех, кто верит в Тебя. 20Когда проливалась кровь Твоего свидетеля Стефана, я стоял там и одобрял это, я сторожил одежды его убийц». 21Тогда Повелитель сказал мне: «Иди, Я посылаю тебя далеко, к другим народам».

Паул перед командиром римского полка

22До этих слов толпа слушала Паула, но тут они стали кричать:

– Стереть его с лица земли! Он не достоин жизни!

23Они кричали, размахивали своими плащами и бросали пыль в воздух. 24Командир римского полка приказал увести Паула в казарму. Он велел избить его и допросить, чтобы узнать, почему народ так негодует на него. 25Но когда Паула привязали, чтобы бить, он сказал стоявшему рядом офицеру:

– Разве позволено бить римского гражданина, да к тому же и без суда?

26Когда офицер это услышал, он пошёл и доложил командиру полка.

– Что ты делаешь? Этот человек римский гражданин, – сказал он.

27Командир вышел к Паулу и спросил:

– Ты действительно римский гражданин?

– Да, – ответил тот.

28Тогда командир сказал:

– Мне пришлось заплатить немало денег за моё гражданство.

– А я родился римским гражданином, – ответил Паул.

29Те, кто должен был его допрашивать, сразу же отступили от него. Командир тоже встревожился, когда узнал, что он заковал в цепи римского гражданина.

Паул перед Высшим Советом иудеев

30На следующий день командир, желая точно узнать, в чём же иудеи обвиняют Паула, освободил его от оков и приказал, чтобы собрались главные священнослужители и весь Высший Совет. Затем он ввёл Паула и поставил перед ними.