Machitidwe a Atumwi 13 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 13:1-52

Barnaba ndi Saulo Atumidwa ndi Mpingo

1Mu mpingo wa ku Antiokeya munali aneneri ndi aphunzitsi awa: Barnaba, Simeoni, Lukia wa ku Kurene, Manayeni (amene analeredwa pamodzi ndi mfumu Herode), ndiponso Saulo. 2Iwo pamene ankapembedza Ambuye ndi kusala kudya, Mzimu Woyera anati, “Mundipatulire Barnaba ndi Saulo kuti akagwire ntchito imene ndinawayitanira.” 3Ndipo atasala kudya ndi kupemphera anasanjika manja awo pa iwo nawatumiza.

Ku Kupro

4Barnaba ndi Saulo motumidwa ndi Mzimu Woyera, anapita ku Selukeya ndipo kuchokera kumeneko anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro. 5Pamene anafika ku Salamisi, analalikira Mawu a Mulungu mʼMasunagoge a Ayuda. Iwo anali ndi Yohane monga wowatumikira.

6Iwo anayenda pa chilumba chonse mpaka anafika ku Pafo, kumeneko anapezanako ndi Myuda, wamatsenga amene analinso mneneri wonama dzina lake Barayesu. 7Iyeyu, amathandiza mkulu wa boma, Sergio Paulo. Mkulu wa bomayu, munthu wanzeru, anayitana Barnaba ndi Saulo chifukwa anafuna kumva Mawu a Mulungu. 8Koma Elima wamatsengayo, (Elima tanthauzo lake ndi wamatsenga), anatsutsana nawo ndipo anafuna kumuletsa mkulu wa bomayo kuti asakhulupirire. 9Koma Saulo, amenenso amatchedwa Paulo, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera anamuyangʼanitsitsa Elima ndipo anati, 10“Iwe ndiwe mwana wa mdierekezi ndiponso mdani wa chilungamo! Ndiwe wodzaza ndi chinyengo cha mtundu uliwonse ndi kuchenjera konse. Kodi sudzaleka kupotoza njira zolungama za Ambuye? 11Tsopano dzanja la Ambuye likukutsutsa iwe. Udzakhala wosaona ndipo kwa kanthawi sudzatha kuona kuwala kwa dzuwa.”

Nthawi yomweyo khungu ndi mdima zinamugwera ndipo anafunafuna munthu woti amugwire dzanja kuti amutsogolere. 12Pamene mkulu wa bomayo anaona zimene zinachitika anakhulupirira pakuti anadabwa ndi chiphunzitso cha Ambuye.

Antiokeya wa ku Pisidiya

13Kuchokera ku Pafo, Paulo ndi anzake anayenda pa sitima ya pamadzi kupita ku Perga wa ku Pamfiliya, kumeneko Yohane anawasiya nabwerera ku Yerusalemu. 14Kuchokera ku Perga anapita ku Pisidiya wa ku Antiokeya. Pa tsiku la Sabata analowa mʼsunagoge, nakhala pansi. 15Atawerenga mawu a mʼMalamulo ndi Aneneri, akulu a sunagoge anawatumizira mawu ndi kuti, “Abale ngati muli ndi mawu olimbikitsa nawo anthuwa, nenani.”

16Atayimirira, Paulo anakweza dzanja lake ndi kuti, “Inu Aisraeli ndiponso inu a mitundu ina amene mumapembedza Mulungu, tandimverani! 17Mulungu wa Aisraeli anasankha makolo athu ndipo anawapatsa chuma chambiri pamene amakhala ku Igupto. Anawatulutsa mʼdzikomo ndi dzanja lake lamphamvu. 18Ndipo Iye anapirira khalidwe lawo mʼchipululu kwa zaka makumi anayi. 19Mulungu anawagonjetsera mitundu isanu ndi iwiri ya ku Kanaani ndipo anapereka dzikolo kwa Israeli kuti likhale lawo. 20Izi zonse zinatenga zaka 450.

“Zitatha izi, Mulungu anawapatsa oweruza mpaka nthawi ya mneneri Samueli. 21Kenaka anthu anapempha kuti awapatse mfumu, ndipo anawapatsa Sauli mwana wa Kisi, wa fuko la Benjamini amene analamulira zaka makumi anayi. 22Mulungu atamuchotsa Sauli, anayika Davide kukhala mfumu yawo. Mulungu anamuchitira umboni kuti, ‘Ndapeza Davide mwana wa Yese munthu wa pamtima panga; iye adzachita zonse zimene ine ndikufuna kuti iye achite.’

23“Kuchokera mwa zidzukulu za munthu ameneyu, Mulungu anawutsa Yesu kukhala Mpulumutsi wa Aisraeli, monga analonjezera. 24Yesu asanabwere, Yohane analalikira kwa anthu onse Aisraeli za kutembenuka mtima ndi ubatizo. 25Pamene Yohane amatsiriza ntchito yake anati: ‘Mukuganiza kuti ine ndine yani? Ine sindine ameneyo ayi, koma Iye akubwera pambuyo panga, amene ine sindine woyenera kumasula zingwe za nsapato zake.’

26“Abale, ana a Abrahamu, ndiponso inu a mitundu ina amene mumaopa Mulungu, Iye watumiza uthenga wachipulumutsowo kwa ife. 27Anthu a ku Yerusalemu ndi atsogoleri awo sanazindikire Yesu, komabe pomuweruza Yesu anakwaniritsa mawu a Aneneri amene amawerengedwa Sabata lililonse. 28Ngakhale sanapeze chifukwa choti afe, anapempha Pilato kuti amuphe. 29Atachita zonse zimene zinalembedwa za Iye, iwo anamuchotsa pa mtengo ndipo anamuyika mʼmanda. 30Koma Mulungu anamuukitsa, 31ndipo kwa masiku ambiri anaonekera kwa amene anayenda naye kuchokera ku Galileya mpaka ku Yerusalemu. Iwowa tsopano ndi mboni zake kwa anthu a Israeli.

32“Ife tikukuwuzani Uthenga Wabwino; umene Mulungu analonjeza makolo athu. 33Iye wakwaniritsa zimenezi kwa ife ana awo, poukitsa Yesu kuchokera kwa akufa. Monga zinalembedwa mu Salimo lachiwiri kuti,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

lero ine ndakhala Atate ako.”

34Zakuti Mulungu anamuukitsa kuti asawole konse, zinanenedwa mʼmawu awa:

“ ‘Ine, ndidzakupatsa madalitso opatulika ndi odalirika amene ndinalonjeza Davide.’

35Nʼchifukwa chakenso zinalembedwa mu Salimo lina kuti,

“ ‘Simudzalekerera woyera wanu kuti awole.’

36“Pakuti pamene Davide anatsiriza kutumikira Mulungu mu mʼbado wake, anamwalira, iye anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ndipo thupi lake linawola. 37Koma amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa sanawole ayi.

38“Nʼchifukwa chake, abale anga, dziwani kuti mwa Yesu chikhululukiro cha machimo chikulalikidwa. 39Kudzera mwa Iye aliyense amene akhulupirira, alungamitsidwa kuchoka ku tchimo lililonse limene silingachoke ndi Malamulo a Mose. 40Samalani kuti zimene aneneri akunena zisakuchitikireni inu:

41“ ‘Onani, inu anthu onyoza,

dabwani ndipo wonongekani,

chifukwa ine ndidzachita china chake mʼmasiku anu,

inu simudzazikhulupirira

ngakhale wina atakufotokozerani!’ ”

42Pamene Paulo ndi Barnaba amatuluka mʼSunagoge, anthu anawapempha kuti adzapitirize kuyankhula zinthu zimenezi Sabata linalo. 43Atatha mapemphero, Ayuda ambiri ndi anthu odzipereka otembenukira ku Chiyuda anatsatira Paulo ndi Barnaba, iwo anayankhula ndi anthuwo ndipo anawapempha kuti apitirire mʼchisomo cha Mulungu.

44Pa Sabata linalo pafupifupi anthu onse a mu mzindawo anasonkhana kudzamva Mawu a Ambuye. 45Pamene Ayuda anaona gulu la anthu, anachita nsanje ndipo anayankhula zamwano kutsutsana ndi zimene Paulo amanena.

46Ndipo Paulo ndi Barnaba anawayankha molimba mtima kuti, “Ife tinayenera kuyankhula Mawu a Mulungu kwa inu poyamba. Popeza inu mwawakana ndi kudziyesa nokha osayenera moyo wosatha, ife tsopano tikupita kwa anthu a mitundu ina. 47Pakuti izi ndi zimene Ambuye anatilamula ife:

“ ‘Ine ndakuyika iwe ukhale kuwunika kwa anthu a mitundu ina,

kuti ukafikitse chipulumutso ku malekezero a dziko lapansi!’ ”

48Anthu a mitundu ina atamva izi, anakondwa ndipo analemekeza Mawu Ambuye; ndipo onse amene anawasankha kuti alandire moyo osatha anakhulupirira.

49Mawu a Ambuye anafalikira mʼchigawo chonse. 50Koma Ayuda anawutsa mitima ya akazi otchuka opembedza Mulungu ndi akulu a mu mzindamo. Iwo anabweretsa mazunzo kwa Paulo ndi Barnaba ndipo anawathamangitsa mʼchigawo chawo. 51Tsono iwo anasasa fumbi la ku mapazi awo powatsutsa, ndipo anapita ku Ikoniya. 52Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chimwemwe ndiponso ndi Mzimu Woyera.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

使徒行传 13:1-52

巴拿巴和扫罗接受差遣

1安提阿教会中有几位先知和教师,就是巴拿巴、绰号“黑人”的希缅古利奈路求、与分封王希律一同长大的马念以及扫罗2一天,他们正在敬拜主、禁食的时候,圣灵对他们说:“要为我把巴拿巴扫罗分别出来,好让他们做我呼召他们去做的事。” 3于是,他们禁食祷告并把手按在巴拿巴扫罗身上,然后差遣他们出去。

4二人受圣灵差遣,下到西流基,从那里乘船去塞浦路斯5他们到了撒拉米,就在当地的犹太会堂传讲上帝的道。约翰·马可做他们的助手。

6他们走遍全岛,远至帕弗,在那里遇见一个冒充先知的犹太术士巴·耶稣7这人和当地的士求·保罗总督常有来往。士求·保罗是个聪明人,他邀请了巴拿巴扫罗来,要听上帝的道。 8希腊名字叫以吕马的那个术士反对使徒,试图拦阻总督信主。 9又名扫罗保罗被圣灵充满,盯着他说: 10“你这魔鬼的儿子,充满了诡诈和邪恶,是一切正义之敌,到现在还想歪曲主的正道吗? 11现在主要亲手惩罚你,使你瞎眼,暂时不见天日!”

他顿觉眼前一片漆黑,只好四处摸索,求人领他走路。 12总督看见所发生的事,对主的道感到惊奇,就信了。

保罗传扬基督

13保罗和同伴从帕弗乘船到旁非利亚别加约翰·马可在那里离开他们回耶路撒冷去了。 14他们由别加继续前行,来到彼西底区的安提阿。在安息日那天,他们进了会堂坐下来。 15读完律法书和先知书后,会堂主管派人告诉他们:“弟兄们,如果你们有什么劝勉众人的话,请讲。”

16保罗站起来向大家挥手示意,说:“各位以色列同胞和各位敬畏上帝的外族朋友们,请听我说。 17以色列的上帝拣选了我们的祖先,让他们在埃及寄居期间人丁兴旺成为大族,后来祂伸出臂膀带领他们离开埃及18他们在旷野漂泊的那四十年间,上帝一直照顾、容忍他们。 19后来上帝又灭了迦南境内的七族,把土地分给他们作产业。 20前后历时约四百五十年。之后,上帝又为他们设立士师,直到撒母耳先知的时代。

21“后来,他们求上帝为他们立一位王,上帝就选立便雅悯支派中基士的儿子扫罗为王,执政四十年。 22之后,上帝废掉扫罗,选立大卫做王,并为他作证说,‘我找到了耶西的儿子大卫,他是合我心意的人,他必遵行我一切的旨意。’ 23上帝照自己的应许,从大卫的后裔中为以色列人立了一位救主,就是耶稣。 24在耶稣还未公开露面以前,约翰已经劝告以色列人要悔改,接受洗礼。 25约翰在工作快要完成的时候说,‘你们以为我是谁?我不是基督。在我之后来的那位,我连给祂解鞋带也不配。’

26“弟兄们,各位亚伯拉罕的子孙和敬畏上帝的外族人啊,这救恩之道原是传给我们的。 27可是耶路撒冷的人和他们的官长不知道耶稣是基督,虽然每个安息日都诵读先知的信息,却把基督判死罪。这正应验了先知们的话。 28他们虽然找不到判祂死罪的理由,却强求彼拉多将祂处死。 29祂受死的记载全部应验之后,有人把祂从十字架上取下来,安放在石墓里。 30但上帝却使祂从死里复活。 31之后有许多天,那些从加利利跟随祂上耶路撒冷的人都看见过祂,他们如今在百姓中都是祂的见证人。 32我们要报给你们一个好消息,上帝给我们祖先的应许, 33祂借着使耶稣复活已为我们做子孙的成就了。正如诗篇第二篇所说,

“‘你是我的儿子,

我今日成为你父亲。’

34圣经曾这样记载上帝使祂从死里复活、永不朽坏的事,

“‘我必将应许大卫的圣洁、

可靠的恩福赐给你们。’

35又在诗篇上说,

“‘你必不让你的圣者身体朽坏。’

36大卫在世时遵行上帝的旨意,最后死了,葬在他祖先那里,肉身也朽坏了。 37然而,上帝使之复活的那位却没有朽坏。 38所以,弟兄们,你们应该知道,赦罪的信息是借着耶稣传给你们的。 39你们靠遵行摩西律法不能被称为义人,只有信靠耶稣才能被称为义人。 40你们要当心,免得先知说的话应验在你们身上,

41“‘藐视真理的人啊,看吧!

你们要在惊惧中灭亡,

因为我要在你们的时代行一件事,

即使有人告诉你们,

你们也不会信。’”

42保罗巴拿巴离开会堂时,会堂里的人请求他们下一个安息日再来讲道。 43许多犹太人和诚心改信犹太教的外族人都跟随保罗巴拿巴,二人就与他们谈论,劝勉他们要坚定不移地信靠上帝的恩典。

44到了下一个安息日,几乎全城的人都聚集起来,要听上帝的道。 45犹太人看见那么多人聚集,充满嫉妒,便反驳保罗所讲的,诽谤他。 46保罗巴拿巴毫不畏惧地说:“上帝的道本该先传给你们,你们既然拒绝接受,认为自己不配得永生,我们现在就把这道传给外族人。 47因为主这样吩咐我们,

“‘我已使你成为外族人的光,

好把救恩带到地极。’”

48外族人听后,非常欢喜,颂赞主的道。凡被选定得永生的人都信了主。 49主的道传遍了那个地方。

50犹太人煽动虔诚的贵妇和城中显要迫害保罗巴拿巴,将二人赶出城去。 51保罗巴拿巴便当众跺掉脚上的尘土13:51 表示两不相干,参见马太福音10:14,去了以哥念52门徒满心喜乐,被圣灵充满。