Machitidwe a Atumwi 13 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 13:1-52

Barnaba ndi Saulo Atumidwa ndi Mpingo

1Mu mpingo wa ku Antiokeya munali aneneri ndi aphunzitsi awa: Barnaba, Simeoni, Lukia wa ku Kurene, Manayeni (amene analeredwa pamodzi ndi mfumu Herode), ndiponso Saulo. 2Iwo pamene ankapembedza Ambuye ndi kusala kudya, Mzimu Woyera anati, “Mundipatulire Barnaba ndi Saulo kuti akagwire ntchito imene ndinawayitanira.” 3Ndipo atasala kudya ndi kupemphera anasanjika manja awo pa iwo nawatumiza.

Ku Kupro

4Barnaba ndi Saulo motumidwa ndi Mzimu Woyera, anapita ku Selukeya ndipo kuchokera kumeneko anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro. 5Pamene anafika ku Salamisi, analalikira Mawu a Mulungu mʼMasunagoge a Ayuda. Iwo anali ndi Yohane monga wowatumikira.

6Iwo anayenda pa chilumba chonse mpaka anafika ku Pafo, kumeneko anapezanako ndi Myuda, wamatsenga amene analinso mneneri wonama dzina lake Barayesu. 7Iyeyu, amathandiza mkulu wa boma, Sergio Paulo. Mkulu wa bomayu, munthu wanzeru, anayitana Barnaba ndi Saulo chifukwa anafuna kumva Mawu a Mulungu. 8Koma Elima wamatsengayo, (Elima tanthauzo lake ndi wamatsenga), anatsutsana nawo ndipo anafuna kumuletsa mkulu wa bomayo kuti asakhulupirire. 9Koma Saulo, amenenso amatchedwa Paulo, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera anamuyangʼanitsitsa Elima ndipo anati, 10“Iwe ndiwe mwana wa mdierekezi ndiponso mdani wa chilungamo! Ndiwe wodzaza ndi chinyengo cha mtundu uliwonse ndi kuchenjera konse. Kodi sudzaleka kupotoza njira zolungama za Ambuye? 11Tsopano dzanja la Ambuye likukutsutsa iwe. Udzakhala wosaona ndipo kwa kanthawi sudzatha kuona kuwala kwa dzuwa.”

Nthawi yomweyo khungu ndi mdima zinamugwera ndipo anafunafuna munthu woti amugwire dzanja kuti amutsogolere. 12Pamene mkulu wa bomayo anaona zimene zinachitika anakhulupirira pakuti anadabwa ndi chiphunzitso cha Ambuye.

Antiokeya wa ku Pisidiya

13Kuchokera ku Pafo, Paulo ndi anzake anayenda pa sitima ya pamadzi kupita ku Perga wa ku Pamfiliya, kumeneko Yohane anawasiya nabwerera ku Yerusalemu. 14Kuchokera ku Perga anapita ku Pisidiya wa ku Antiokeya. Pa tsiku la Sabata analowa mʼsunagoge, nakhala pansi. 15Atawerenga mawu a mʼMalamulo ndi Aneneri, akulu a sunagoge anawatumizira mawu ndi kuti, “Abale ngati muli ndi mawu olimbikitsa nawo anthuwa, nenani.”

16Atayimirira, Paulo anakweza dzanja lake ndi kuti, “Inu Aisraeli ndiponso inu a mitundu ina amene mumapembedza Mulungu, tandimverani! 17Mulungu wa Aisraeli anasankha makolo athu ndipo anawapatsa chuma chambiri pamene amakhala ku Igupto. Anawatulutsa mʼdzikomo ndi dzanja lake lamphamvu. 18Ndipo Iye anapirira khalidwe lawo mʼchipululu kwa zaka makumi anayi. 19Mulungu anawagonjetsera mitundu isanu ndi iwiri ya ku Kanaani ndipo anapereka dzikolo kwa Israeli kuti likhale lawo. 20Izi zonse zinatenga zaka 450.

“Zitatha izi, Mulungu anawapatsa oweruza mpaka nthawi ya mneneri Samueli. 21Kenaka anthu anapempha kuti awapatse mfumu, ndipo anawapatsa Sauli mwana wa Kisi, wa fuko la Benjamini amene analamulira zaka makumi anayi. 22Mulungu atamuchotsa Sauli, anayika Davide kukhala mfumu yawo. Mulungu anamuchitira umboni kuti, ‘Ndapeza Davide mwana wa Yese munthu wa pamtima panga; iye adzachita zonse zimene ine ndikufuna kuti iye achite.’

23“Kuchokera mwa zidzukulu za munthu ameneyu, Mulungu anawutsa Yesu kukhala Mpulumutsi wa Aisraeli, monga analonjezera. 24Yesu asanabwere, Yohane analalikira kwa anthu onse Aisraeli za kutembenuka mtima ndi ubatizo. 25Pamene Yohane amatsiriza ntchito yake anati: ‘Mukuganiza kuti ine ndine yani? Ine sindine ameneyo ayi, koma Iye akubwera pambuyo panga, amene ine sindine woyenera kumasula zingwe za nsapato zake.’

26“Abale, ana a Abrahamu, ndiponso inu a mitundu ina amene mumaopa Mulungu, Iye watumiza uthenga wachipulumutsowo kwa ife. 27Anthu a ku Yerusalemu ndi atsogoleri awo sanazindikire Yesu, komabe pomuweruza Yesu anakwaniritsa mawu a Aneneri amene amawerengedwa Sabata lililonse. 28Ngakhale sanapeze chifukwa choti afe, anapempha Pilato kuti amuphe. 29Atachita zonse zimene zinalembedwa za Iye, iwo anamuchotsa pa mtengo ndipo anamuyika mʼmanda. 30Koma Mulungu anamuukitsa, 31ndipo kwa masiku ambiri anaonekera kwa amene anayenda naye kuchokera ku Galileya mpaka ku Yerusalemu. Iwowa tsopano ndi mboni zake kwa anthu a Israeli.

32“Ife tikukuwuzani Uthenga Wabwino; umene Mulungu analonjeza makolo athu. 33Iye wakwaniritsa zimenezi kwa ife ana awo, poukitsa Yesu kuchokera kwa akufa. Monga zinalembedwa mu Salimo lachiwiri kuti,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

lero ine ndakhala Atate ako.”

34Zakuti Mulungu anamuukitsa kuti asawole konse, zinanenedwa mʼmawu awa:

“ ‘Ine, ndidzakupatsa madalitso opatulika ndi odalirika amene ndinalonjeza Davide.’

35Nʼchifukwa chakenso zinalembedwa mu Salimo lina kuti,

“ ‘Simudzalekerera woyera wanu kuti awole.’

36“Pakuti pamene Davide anatsiriza kutumikira Mulungu mu mʼbado wake, anamwalira, iye anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ndipo thupi lake linawola. 37Koma amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa sanawole ayi.

38“Nʼchifukwa chake, abale anga, dziwani kuti mwa Yesu chikhululukiro cha machimo chikulalikidwa. 39Kudzera mwa Iye aliyense amene akhulupirira, alungamitsidwa kuchoka ku tchimo lililonse limene silingachoke ndi Malamulo a Mose. 40Samalani kuti zimene aneneri akunena zisakuchitikireni inu:

41“ ‘Onani, inu anthu onyoza,

dabwani ndipo wonongekani,

chifukwa ine ndidzachita china chake mʼmasiku anu,

inu simudzazikhulupirira

ngakhale wina atakufotokozerani!’ ”

42Pamene Paulo ndi Barnaba amatuluka mʼSunagoge, anthu anawapempha kuti adzapitirize kuyankhula zinthu zimenezi Sabata linalo. 43Atatha mapemphero, Ayuda ambiri ndi anthu odzipereka otembenukira ku Chiyuda anatsatira Paulo ndi Barnaba, iwo anayankhula ndi anthuwo ndipo anawapempha kuti apitirire mʼchisomo cha Mulungu.

44Pa Sabata linalo pafupifupi anthu onse a mu mzindawo anasonkhana kudzamva Mawu a Ambuye. 45Pamene Ayuda anaona gulu la anthu, anachita nsanje ndipo anayankhula zamwano kutsutsana ndi zimene Paulo amanena.

46Ndipo Paulo ndi Barnaba anawayankha molimba mtima kuti, “Ife tinayenera kuyankhula Mawu a Mulungu kwa inu poyamba. Popeza inu mwawakana ndi kudziyesa nokha osayenera moyo wosatha, ife tsopano tikupita kwa anthu a mitundu ina. 47Pakuti izi ndi zimene Ambuye anatilamula ife:

“ ‘Ine ndakuyika iwe ukhale kuwunika kwa anthu a mitundu ina,

kuti ukafikitse chipulumutso ku malekezero a dziko lapansi!’ ”

48Anthu a mitundu ina atamva izi, anakondwa ndipo analemekeza Mawu Ambuye; ndipo onse amene anawasankha kuti alandire moyo osatha anakhulupirira.

49Mawu a Ambuye anafalikira mʼchigawo chonse. 50Koma Ayuda anawutsa mitima ya akazi otchuka opembedza Mulungu ndi akulu a mu mzindamo. Iwo anabweretsa mazunzo kwa Paulo ndi Barnaba ndipo anawathamangitsa mʼchigawo chawo. 51Tsono iwo anasasa fumbi la ku mapazi awo powatsutsa, ndipo anapita ku Ikoniya. 52Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chimwemwe ndiponso ndi Mzimu Woyera.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Деяния 13:1-52

Варнава и Шаул посланы на служение

1В общине верующих Антиохии были пророки и учители: Варнава, Шимон, называемый Нигер13:1 Нигер – «чёрный» (лат.)., киренец Луций, Менахем, получивший воспитание вместе с правителем Иродом, и Шаул. 2Однажды, когда они совершали служение Вечному Повелителю и постились, Святой Дух сказал:

– Отделите мне Варнаву и Шаула для дела, к которому Я их призвал.

3И они после поста и молитвы возложили на них руки и отпустили их.

Служение на Кипре

4Шаул и Варнава, посланные Святым Духом, пошли в Селевкию, а оттуда отплыли на Кипр. 5Они прибыли в Саламин и там возвещали слово Всевышнего в иудейских молитвенных домах. Иохан тоже был с ними и помогал им. 6Они прошли весь остров и пришли в Паф. Там они встретили одного иудея по имени Бар-Иешуа, который был колдуном и лжепророком. 7Он был из окружения правителя Сергия Павлуса, человека большого ума. Правитель пригласил Варнаву и Шаула, желая услышать слово Всевышнего. 8Но колдун, которого также звали Елима (что значит «чародей»), действовал против них и пытался отвратить правителя от веры. 9Тогда Шаул, он же Павлус, исполнившись Святого Духа, посмотрел прямо на Елиму 10и сказал:

– Сын дьявола, враг всякой праведности, полный лжи и нечестия! Неужели ты никогда не перестанешь искривлять прямые пути13:10 Ср. Мудр. 10:9. Вечного Повелителя? 11Рука Повелителя обращена против тебя, ты будешь поражён слепотой и некоторое время не будешь видеть солнечного света.

И сразу же его окутали мрак и тьма, и он стал метаться из стороны в сторону, ища кого-либо, кто бы повёл его за руку. 12Когда правитель увидел, что произошло, он уверовал, изумлённый учением о Повелителе.

Служение в Писидийской Антиохии

13Отплыв из Пафа, Павлус и его спутники прибыли в Пергию в Памфилии13:13 Далее (до 14:26) это путешествие проходило по территории Малой Азии (часть современной Турции).. Там Иохан оставил их и возвратился в Иерусалим. 14Из Пергии они пошли дальше, в Писидийскую Антиохию. В субботу они пришли в молитвенный дом иудеев и сели. 15После чтения из Таврота и Книги Пророков начальники молитвенного дома передали им:

– Братья, если у вас есть что-либо сказать в назидание людям, то говорите.

16Павлус встал и, сделав жест рукой, сказал:

– Народ Исроила и все боящиеся Всевышнего, выслушайте меня! 17Бог исроильского народа избрал наших отцов. Он возвысил народ во время пребывания его в Египте и могучей рукой вывел их оттуда13:17 См. Исх. 6:6; 12:51.. 18Сорок лет13:18 См. Исх. 16:35; Чис. 14:34. Он терпел их13:18 Или: «заботился о них». в пустыне. 19Он истребил в Ханоне семь народов13:19 Семь народов – см. Втор. 7:1. и отдал их землю в наследие нашим предкам.

20На это ушло около четырёхсот пятидесяти лет. Затем, до времени пророка Самуила, Всевышний давал им судей13:20 См. Суд. 2:16.. 21Потом народ попросил себе царя, и Всевышний дал им Шаула, сына Киша, из рода Вениамина. Шаул правил лет сорок. 22Потом, отстранив Шаула, Всевышний сделал царём Довуда. Он свидетельствовал о нём: «Я нашёл Довуда, сына Есея, человек этот Мне по сердцу, он исполнит все Мои желания»13:22 См. 1 Цар. 13:14; Заб. 88:21..

23Из потомков Довуда Всевышний, согласно Своему обещанию, призвал Спасителя Исроилу – Исо. 24Перед пришествием Исо Яхьё призывал весь народ Исроила принять обряд погружения в воду13:24 Или: «обряд омовения». в знак покаяния. 25Заканчивая своё служение, Яхьё говорил: «За кого вы меня принимаете? За Масеха? Я не Он. Но за мной идёт Тот, у Кого я не достоин даже развязать ремни сандалий на ногах»13:25 См. Лк. 3:15-16; Ин. 1:19-27..

26Братья, дети рода Иброхима, и все, кто боится Всевышнего! Эта весть спасения была послана к нам! 27Жители Иерусалима и их начальники не узнали Масеха, они осудили Его и тем самым исполнили слова пророков, которые читаются каждую субботу. 28Они не нашли в Нём никакой вины, за которую Он был бы достоин смерти, и всё-таки выпросили у Пилата разрешение казнить Его. 29Когда они исполнили всё, что было о Нём написано, они сняли Его с дерева13:29 См. сноску на 5:30. и положили в могильную пещеру. 30Но Всевышний воскресил Его из мёртвых, 31и ещё много дней те, кто пришёл вместе с Ним из Галилеи в Иерусалим, видели Его. Они сейчас – Его свидетели перед народом.

32Мы провозглашаем вам сейчас эту Радостную Весть: то, что Всевышний обещал нашим отцам, Он исполнил для нас, их детей, воскресив Исо. 33Во второй песне из Забура написано:

«Ты Сын Мой (Избранный Мной Царь).

Я Отцом Твоим отныне буду назван»13:33 Букв.: «Ты Сын Мой, сегодня Я родил Тебя» (Заб. 2:7). Вторая песнь из Забура говорит о коронации иудейского царя, и значит, слова «Я родил тебя» здесь указывают на его воцарение..

34А о том, что Всевышний воскресил Его из мёртвых, так что тело Его уже никогда не увидит тления, Он сказал так:

«Я дам вам святые и неизменные благословения, обещанные Довуду»13:34 Ис. 55:3..

35И в другом месте Он говорит:

«Ты не дашь Верному Твоему увидеть тление»13:35 Заб. 15:10..

36Довуд, в своё время послужив воле Всевышнего, умер. Его похоронили с его отцами, и тело его истлело13:36 См. 3 Цар. 2:10.. 37Но Тот, Кого Всевышний воскресил, избежал тления!

38– Поэтому, братья, я хочу, чтобы вы знали, что, благодаря Исо вам сегодня возвещается прощение грехов. 39Соблюдением Закона Мусо вы не могли оправдаться перед Всевышним, но каждый верующий в Исо получает оправдание в Нём. 40Смотрите, чтобы не случилось с вами того, о чём сказано в Книге Пророков:

41«Посмотрите, насмешники!

Изумитесь и погибните!

Я совершу в ваши дни такое,

чему бы вы никогда не поверили,

если бы вам рассказали об этом»13:41 Авв. 1:5..

42Когда Павлус и Варнава покидали молитвенный дом иудеев, их попросили говорить о том же в следующую субботу. 43Собрание разошлось, но многие иудеи и люди, чтущие Всевышнего, обращённые из других народов, пошли за Павлусом и Варнавой. Те говорили с ними и убеждали их и дальше жить, доверяясь благодати Всевышнего.

44В следующую субботу почти весь город собрался, чтобы послушать слово о Повелителе Исо. 45Но когда иудеи, которые не поверили, увидели столько народа, они исполнились завистью и стали с оскорблениями возражать тому, что говорил Павлус. 46Тогда Павлус и Варнава решительно сказали им:

– Слово Всевышнего в первую очередь должно было быть возвещено вам. Но так как вы отрицаете его и считаете себя недостойными вечной жизни, мы обращаемся теперь к другим народам, 47как и повелел нам Вечный. Он сказал:

«Я сделал Тебя светом для других народов,

чтобы через Тебя спасение достигло концов земли»13:47 Ис. 49:6..

48Когда люди из других народов слышали это, они радовались и славили Вечного за Его слово, и все предназначенные к вечной жизни уверовали.

49Слово о Повелителе Исо распространилось по всей той области.

50Но отвергающие Исо иудеи подговорили чтущих Всевышнего женщин из знатных семей и влиятельных людей города, и те возбудили преследование против Павлуса и Варнавы и выгнали их из своих пределов. 51Тогда они отряхнули пыль со своих ног во свидетельство против своих гонителей13:51 Благочестивые иудеи отряхивали пыль со своих ног, когда возвращались из других стран, как бы очищаясь от ритуального осквернения. Делая же это по отношению к другим иудеям, они приравнивали их к язычникам. и пошли в Конию. 52Ученики же исполнялись радости и Святого Духа.