Machitidwe a Atumwi 12 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 12:1-25

Petro Apulumuka Mʼndende

1Inali nthawi yomweyi imene mfumu Herode anamanga ena a mu mpingo ndi cholinga chakuti awazunze. 2Iye analamula kuti Yakobo mʼbale wa Yohane, aphedwe ndi lupanga. 3Ataona kuti zimenezi zinakondweretsa Ayuda, anawonjeza ndi kugwiranso Petro. Izi zinachitika pa nthawi ya Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. 4Atamugwira Petro, namutsekera mʼndende, anamupereka kwa magulu anayi a asilikali kuti amuyangʼanire, gulu lililonse linali ndi asilikali anayi. Herode anafuna kumuzenga mlandu pamaso pa anthu onse chikondwerero cha Paska chitapita.

5Kotero Petro anasungidwa mʼndende, koma mpingo unamupempherera kolimba kwa Mulungu.

6Usiku woti mmawa mwake Herode amuzenga mlandu, Petro amagona pakati pa asilikali awiri, atamangidwa maunyolo awiri, ndiponso alonda atayima pa khomo. 7Mwadzidzidzi mngelo wa Ambuye anaonekera ndipo kuwala kunawunika mʼchipindamo. Mngeloyo anamugwedeza Petro mʼnthiti ndi kumudzutsa. Iye anati, “Fulumira, imirira!” Ndipo maunyolo anagwa kuchoka mʼmanja a Petro.

8Kenaka mngelo anati kwa iye, “Vala zovala ndi nsapato.” Ndipo Petro atachita izi mngeloyo anamuwuzanso kuti, “Funda chovala chako ndipo unditsate.” 9Petro anatsatira natuluka mʼndende, koma sanazindikire kuti zimene mngeloyo amachita zimachitikadi; iye amaganiza kuti amaona masomphenya. 10Iwo anadutsa gulu loyamba ndi lachiwiri la asilikali ndipo anafika pa chitseko chachitsulo cholowera mu mzinda. Chitsekocho chinatsekuka chokha ndipo anadutsa. Pamene anayenda kutalika kwa msewu umodzi, mwadzidzidzi mngelo uja anachoka.

11Pamenepo Petro anazindikira nati, “Tsopano ndikudziwa mosakayika kuti Ambuye anatuma mngelo wake kudzandipulumutsa mʼmanja mwa Herode, ndi ku zoyipa zonse zimene Ayuda amafuna kundichitira.”

12Atazindikira zimenezi anapita ku nyumba ya Mariya amayi ake a Yohane, wotchedwanso Marko, kumene kunasonkhana anthu ambiri ndipo amapemphera. 13Petro anagogoda pa chitseko cha panja, ndipo mtsikana wantchito dzina lake Roda anabwera kuti adzatsekule chitseko. 14Atazindikira mawu a Petro anakondwa kwambiri ndipo anabwerera osatsekula ndipo anafuwula kuti, “Petro ali pa khomopa!”

15Anthuwo anati kwa iye, “Wopenga iwe!” Atalimbikira kunena kuti zinali zoona, iwo anati, “Ameneyo ndi mngelo wake.”

16Koma Petro anapitiriza kugogoda ndipo atatsekula chitseko ndi kumuona, anthuwo anadabwa kwambiri. 17Petro anakweza dzanja ndi kuwawuza kuti akhale chete ndipo anawafotokozera mmene Ambuye anamutulutsira mʼndende. Iye anati, “Uzani Yakobo ndi abale ena za zimenezi.” Kenaka anachoka napita kumalo ena.

18Pamene kunacha kunali phokoso lalikulu pakati pa asilikali, iwo anafunsa kuti, “Kodi chamuchitikira Petro ndi chiyani?” 19Herode atamufunafuna ndipo wosamupeza, anawafunsa asilikali ndipo analamulira kuti asilikaliwo aphedwe.

Imfa ya Herode

Kenaka Herode anachoka ku Yudeya ndi kupita ku Kaisareya ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi 20Herode anakwiyira anthu a ku Turo ndi Sidoni; anthuwo anagwirizana zoti akambirane naye. Atapeza thandizo kuchokera kwa Blasito, wantchito wokhulupirika wa mfumu, anapempha kuti pakhale mtendere, chifukwa dziko lawo limadalira dziko la mfumuyo pa chakudya chawo.

21Pa tsiku limene anasankha Herode, atavala zovala zake zaufumu, anakhala pa mpando wake ndipo anayankhula kwa anthuwo. 22Anthuwo anafuwula nati, “Amenewa ndi mawu a mulungu osati a munthu ayi.” 23Nthawi yomweyo mngelo wa Mulungu anamukantha chifukwa sanapereke ulemu kwa Mulungu ndipo anadyedwa ndi mphutsi nafa.

24Koma Mawu a Mulungu anapitirirabe kufalikirafalikira.

25Barnaba ndi Saulo atamaliza ntchito yawo anachoka ku Yerusalemu, atatenga Yohane wotchedwanso Marko.

Knijga O Kristu

Djela Apostolska 12:1-25

Jakovljevo smaknuće i Pavlovo utamničenje

1Tada kralj Herod Agripa12:1 U grčkome: kralj Herod. Nećak Heroda Antipe i unuk Heroda Velikoga. počne zlostavljati neke vjernike iz Crkve. 2Ivanova brata Jakova pogubi mačem. 3Kad je vidio da je to drago židovskim vođama, uhiti i Petra za Blagdana beskvasnih kruhova.12:3 Za vrijeme Pashe. 4Uhiti ga i baci u tamnicu te zapovjedi da ga čuvaju četiri vojničke straže. Kanio ga je poslije Pashe izvesti pred narod da mu sude. 5Dok je Petar bio u tamnici, Crkva se žarko molila Bogu za njega.

6Noć prije nego što ga je Herod kanio izvesti pred sud Petar je spavao okovan između dvojice vojnika, a pred vratima su stražarili vojnici.

Petrovo čudesno izbavljenje iz tamnice

7Ali odjednom ćeliju obasja svjetlost: pojavi se anđeo Gospodnji. Udari Petra po rebrima i reče “Brzo ustani!” I lanci mu spadnu s ruku. 8Zatim mu anđeo reče: “Opaši se i obuj sandale.” Petar posluša. “Obuci sada ogrtač i pođi za mnom!” zapovjedi anđeo.

9Petar iziđe i pođe za njim, ali nije znao da se to zaista događa. Mislio je da ima viđenje. 10Prošli su pokraj prve i druge straže te došli do željeznih vrata na izlazu iz zatvora. Ona se sama otvore te iziđu na ulicu. Kad su prošli jednu ulicu, anđeo odjednom ode od njega.

11Petar napokon shvati što se dogodilo: “Gospodin je zaista poslao anđela da me izbavi od Heroda i od onoga što su mi Židovi htjeli učiniti!” reče on.

12Kad je to shvatio, uputi se domu Marije, majke Ivana zvanoga Marko. Ondje su mnogi bili okupljeni na molitvi. 13Zakuca na dvorišna vrata. Sluškinja imenom Ruža dođe poslušati tko kuca. 14Kad je prepoznala Petrov glas, od veselja zaboravi otvoriti vrata. Utrči u kuću i javi im da je pred vratima Petar.

15“Poludjela si”, odgovore joj, ali ona je to i dalje uporno tvrdila. “Vjerojatno je to njegov anđeo”, zaključe zatim.

16Petar je i dalje kucao. Kad su na koncu otvorili i ugledali ga, zaprepaste se. 17On im rukom pokaže da šute te ispriča kako ga je sam Gospodin izveo iz tamnice. “Javite Jakovu i drugoj braći što se dogodilo!” reče. Zatim ode na drugo mjesto.

18Kad se razdanilo, među vojnicima nastane uzbuna zbog Petrova nestanka. 19Herod Agripa pošalje potragu za njim, a kad ga ne nađu, sasluša stražare i zapovjedi da se smaknu. Ode zatim iz Judeje u Cezareju te ondje ostane neko vrijeme.

Herodova smrt

20Herod je bio u žestoku sukobu sa žiteljima Tira i Sidona. Pošalju mu stoga izaslanike da s pomoću kraljevskoga komornika Blasta, kojega su pridobili, zaiskaju mir jer su hranu nabavljali iz Herodove zemlje. 21Na dan sastanka Herod obuče kraljevsko ruho te sjedne na prijestolje i počne im govoriti. 22Narod je vikao: “Božji je to glas, a ne ljudski!”

23Ali zato što je prihvatio da mu se ljudi klanjaju i što nije dao slavu Bogu, udari ga anđeo Gospodnji te ga izjedu crvi i umre.

24Ali Božja riječ brzo se širila i stjecala nove vjernike.

25Kad su Barnaba i Savao završili sa služenjem u Jeruzalemu, vrate se u Antiohiju i povedu sa sobom Ivana zvanog Marko.