Luka 8 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 8:1-56

Fanizo la Wofesa

1Zitatha izi, Yesu anayendayenda kuchoka mzinda wina kupita wina ndiponso mudzi wina kupita wina, akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu. Ophunzira ake khumi ndi awiri aja anali naye, 2komanso akazi ena amene anachiritsidwa ku mizimu yoyipa ndi matenda: Mariya, wotchedwa Magadalena, amene mwa iye munatuluka ziwanda zisanu ndi ziwiri; 3Yohana mkazi wa Kuza, woyangʼanira mʼnyumba ya Herode; Suzana; ndi ena ambiri analinso. Akazi awa ankawathandiza ndi chuma chawo.

4Anthu ambiri ankasonkhana, ndipo pamene anthu ankabwera kwa Yesu kuchokera ku midzi, Iye anawawuza fanizo ili, 5“Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa mbewuzo, zina zinagwa mʼmbali mwa njira; zinapondedwa, ndipo mbalame zamlengalenga zinadya. 6Zina zinagwa pa thanthwe, ndipo pamene zinamera, zinafota chifukwa panalibe chinyezi. 7Mbewu zina zinagwera pakati pa minga, zinakulira pamodzi ndi mingazo ndipo zinalepheretsa mmerawo kukula. 8Mbewu zina zinagwera pa nthaka yabwino. Zinamera ndipo zinabala mowirikiza 100 kuposa zimene zinafesedwa zija.”

Atanena izi, anafuwula kuti, “Amene ali ndi makutu, amve.”

9Ophunzira ake anamufunsa tanthauzo lake la fanizolo. 10Iye anati, “Kudziwa zinsinsi za ufumu wa Mulungu kwapatsidwa kwa inu, koma kwa ena ndimawayankhula mʼmafanizo kuti,

“ngakhale akuona, asapenye;

ngakhale akumva, asazindikire.”

11“Tanthauzo la fanizoli ndi ili: Mbewu ndi mawu a Mulungu. 12Mbewu za mʼmbali mwa njira ndi anthu amene amamva mawu, ndipo kenaka mdierekezi amabwera ndi kuchotsa mawuwo mʼmitima mwawo kuti asakhulupirire ndi kupulumutsidwa. 13Mbewu za pa thanthwe ndi anthu amene amalandira mawu mwachimwemwe pamene akumva, koma mawuwo sazika mizu. Iwo amakhulupirira kwa kanthawi, koma pa nthawi ya mayesero, amagwa. 14Mbewu zimene zinagwa pakati pa minga zikuyimira anthu amene amamva mawu, koma akamayenda mʼnjira zawo amatsamwitsidwa ndi zodandaulitsa za moyo uno, chuma ndi zosangalatsa, ndipo iwo samakhwima. 15Koma mbewu za pa nthaka yabwino zikuyimira anthu amene ali ndi mtima woona ndi wabwino, amene amamva mawu nawasunga, ndipo amalimbikira mpaka amabala zipatso.

Nyale ndi Choyikapo Chake

16“Palibe amayatsa nyale ndi kuyibisa mu mtsuko kapena kuyika pansi pa bedi. Koma mʼmalo mwake, amayika pa choyikapo chake, kuti anthu olowamo aone kuwala. 17Pakuti palibe kanthu kobisika kamene sikadzawululika, ndipo palibe kanthu kophimbika kamene sikadzadziwika kapena kuonetsedwa poyera. 18Choncho ganizirani mozama. Iye amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, iye amene alibe, ngakhale chimene akuganiza kuti ali nacho adzalandidwa.”

Amayi ndi Abale a Yesu

19Tsopano amayi ndi abale a Yesu anabwera kudzamuona Iye, koma analephera kuti afike pafupi ndi Iye chifukwa cha gulu la anthu. 20Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunja, akufuna kukuonani.”

21Yesu anayankha kuti, “Amayi ndi abale anga ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kumachita zimene mawuwo akunena.”

Yesu Aletsa Namondwe

22Tsiku lina Yesu anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina la nyanja.” Ndipo analowa mʼbwato nanyamuka. 23Akuwoloka, Iye anagona tulo. Namondwe wamkulu anayamba pa nyanja, ndipo bwatolo linayamba kudzaza ndi madzi ndipo anali pa chiopsezo chachikulu.

24Ophunzira anapita ndi kukamudzutsa Iye, nati, “Ambuye, Ambuye, ife tikumira!”

Anadzuka ndipo anadzudzula mphepo ndi madzi owindukawo. Namondwe anasiya, ndipo panali bata. 25Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Chikhulupiriro chanu chili kuti?”

Koma pogwidwa ndi mantha ndi kudabwa anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndi ndani? Iye alamulira ngakhale mphepo ndi madzi, ndipo zimumvera Iye.”

Achiritsidwa Munthu Wogwidwa ndi Ziwanda

26Iwo anawolokera ku chigawo cha Gerasa chimene chili tsidya lina la nyanja kuchokera ku Galileya. 27Yesu ataponda pa mtunda, anakumana ndi munthu wogwidwa ndi ziwanda wochokera mu mzindawo. Kwa nthawi yayitali munthuyu sanavale zovala kapena kukhala mʼnyumba, koma amakhala ku manda. 28Iye ataona Yesu, anakuwa nagwa pa mapazi ake akufuwula kwambiri kuti, “Mukufuna chiyani ndi ine, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Ndikupemphani Inu, musandizunze ine!” 29Pakuti Yesu analamula mzimu woyipawo kuti utuluke mwa munthuyo. Kawirikawiri umamugwira iye, ndipo ngakhale anali womangidwa ndi unyolo dzanja ndi mwendo ndi kuti ankamuyangʼanira, koma amadula maunyolo akewo ndipo ziwanda zimamutengera kumalo a yekha.

30Yesu anamufunsa kuti, “Dzina lako ndani?”

Iye anayankha kuti, “Legiyo,” chifukwa ziwanda zambiri zinalowa mwa iye. 31Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima.

32Gulu lalikulu la nkhumba limadya pamenepo mʼmbali mwa phiri. Ziwandazo zinamupempha Yesu kuti azilole kuti zikalowe mu nkhumbazo ndipo Iye anazilola. 33Ziwanda zija zitatuluka mwa munthuyo, zinakalowa mwa nkhumbazo, ndipo gulu lonselo linathamangira ku mtsetse ndi kukalowa mʼnyanja ndi kumira.

34Oweta nkhumbazo ataona zimene zinachitikazo, anathamanga ndi kukanena izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi. 35Ndipo anthu anapita kukaona zimene zinachitika. Atafika kwa Yesu, anapeza munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja atakhala pa mapazi a Yesu, atavala ndipo ali ndi nzeru zake; ndipo iwo anachita mantha. 36Amene anaona izi anawuza anthu mmene munthu wogwidwa ndi ziwandayo anachiritsidwira. 37Kenaka anthu onse a ku chigawo cha Gerasa anamupempha Yesu kuti achoke kwa iwo, chifukwa anadzazidwa ndi mantha. Choncho Iye analowa mʼbwato nachoka.

38Munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja, anapempha Yesu kuti apite nawo, koma Yesu anamubweza nati, 39“Bwerera kwanu kafotokoze zimene Mulungu wakuchitira.” Ndipo munthuyo anachoka ndi kukanena ku mzinda wonsewo zimene Yesu anamuchitira iye.

Mwana Wamkazi wa Yairo ndi Mayi Wokhudza Chovala cha Yesu

40Yesu atabwerera, gulu lalikulu la anthu linamulandira, chifukwa onse ankamuyembekezera. 41Nthawi yomweyo munthu wotchedwa Yairo, woweruza wa mu sunagoge, anabwera ndi kugwa pa mapazi a Yesu, namupempha Iye kuti apite ku nyumba kwake, 42chifukwa mwana wake yekhayo wamkazi, kamtsikana ka zaka khumi ndi ziwiri, kanali pafupi kufa.

Pamene Yesu ankapita gulu la anthu linkamupanikiza. 43Ndipo pomwepo panali mayi wina amene ankataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, koma panalibe wina akanamuchiritsa. 44Iye anafika kumbuyo kwake ndi kukhudza mothera mwa chovala chake, ndipo nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka.

45Yesu anafunsa kuti, “Wandikhudza ndani?”

Onse atakana, Petro anati, “Anthu akukupanikizani ndi kukukankhani.”

46Koma Yesu anati, “Wina wandikhudza; ndikudziwa chifukwa mphamvu yachoka mwa Ine.”

47Ndipo mayiyo podziwa kuti sanathe kuchoka wosadziwika, anabwera akunjenjemera ndipo anagwa pa mapazi a Yesu. Pamaso pa anthu onse, anafotokoza chifukwa chimene anamukhudzira Iye ndi mmene iye anachiritsidwira nthawi yomweyo. 48Kenaka anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere.”

49Pamene Yesu ankayankhulabe, munthu wina anabwera kuchokera ku nyumba ya Yairo, woweruza wa ku sunagoge uja. Iye anati, “Mwana wanu wa mkazi wamwalira, musawavutitsenso Aphunzitsiwa.”

50Atamva zimenezi, Yesu anati kwa Yairo, “Usachite mantha, ingokhulupirira basi ndipo adzachiritsidwa.”

51Iye atafika ku nyumba ya Yairo, sanalole wina aliyense kulowa kupatula Petro, Yohane, ndi Yakobo ndi abambo ndi amayi a mwanayo. 52Pa nthawiyi nʼkuti anthu onse akubuma ndi kumulirira iye. Yesu anati, “Lekani kulira, sanafe koma wagona tulo.”

53Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira. 54Koma Iye anamugwira dzanja lake ndipo anati, “Mwana wanga, dzuka!” 55Mzimu wake unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anayimirira. Kenaka Yesu anawawuza kuti amupatse chakudya. 56Makolo ake anadabwa, koma Iye anawalamulira kuti asawuze wina aliyense zimene zinachitikazo.

Slovo na cestu

Lukáš 8:1-56

Ženy provázejí Ježíše a učedníky

1Potom Ježíš chodil od města k městu, od vesnice k vesnici a všude kázal radostnou zvěst, že Boží království přichází. Doprovázelo ho jeho dvanáct učedníků 2a některé ženy, které zbavil démonů a uzdravil z různých nemocí. Byly to: Marie Magdaléna, kterou osvobodil od naprosté posedlosti, 3Jana – žena Herodova správce Chuzy, Zuzana a mnohé jiné, které je ze svých prostředků podporovaly.

Ježíš vypráví podobenství o rozsévači

4Jednou se okolo Ježíše shromáždilo mnoho lidí ze všech koutů. Vyprávěl jim toto podobenství: 5„Vyšel rolník na pole, aby rozséval. Jak rozséval, padlo některé zrno na cestu, kde je buď zašlapali lidé, nebo sezobali ptáci. 6Jiné padlo na skalnatou půdu. Vyklíčilo sice, ale pro nedostatek vláhy uschlo. 7I do trní některé zapadlo, trní je však přerostlo a udusilo. 8Pouze v připravené půdě se zrno trvale uchytilo a vyhnalo do plných klasů, v jakých bývá i na sto zrnek.“ Když dovyprávěl, řekl: „Slyšeli jste – přemýšlejte!“

9Později se ho učedníci ptali, co to podobenství znamená. 10Ježíš odpověděl: „Bůh vám dopřává, abyste porozuměli jeho záměrům se světem. Ostatním jsou dána podobenství:

vidí, a přece mnozí nic nepoznají, slyší,

a nakonec většinou nepochopí nic.

11Tomu podobenství je třeba rozumět takto: Zrno je Boží řeč k lidem. 12U mnohých se mu daří tak jako zrnu, které padlo na cestu. Ti Boží slovo vyslechnou, a pak přichází ďábel a to, co slyšeli, jim ze srdce sebere, jen aby neuvěřili a nebyli zachráněni. 13U těch druhých se daří slovu jako zrnu, které padlo na skalnatou půdu. Ti Boží slovo vyslechnou, radostně je přijmou, ale nedovolí, aby v jejich životě zapustilo kořeny. Nějakou dobu vydrží věřit, ale když přijdou zkoušky, odpadnou. 14U jiných je to jako se zrnem, které padlo do trní. Ti rozumějí Božímu slovu, ale nedozraje v nich a nepřinese užitek; každodenní starosti, snaha něco vlastnit a honba za požitky je udusí. 15A konečně u některých je to jako se zrnem, které padlo do úrodné půdy. Ti slyší rádi Boží slovo, opatrují je v připraveném srdci a upřímně mu věří. Ti pak přinášejí trvalý užitek. 16Nikdo nerozsvěcuje svíci proto, aby ji přikryl nádobou nebo strčil pod postel, ale proto, aby ji postavil na svícen. Jenom tak posvítí na cestu těm, kdo vcházejí. 17Všechno, co je skryté, bude jednou vyneseno na světlo a vše, co se úzkostlivě tají, vyjde najevo. 18Zamyslete se nad tím, jak nasloucháte Božímu slovu! Kdo je bere vážně, porozumí víc a víc, ale kdo je bere na lehkou váhu, přijde nakonec i o to, co si myslí, že má!“

Ježíš říká, kdo tvoří jeho rodinu

19Ježíšova matka a jeho bratři pro něj přišli, ale nemohli se k němu dostat pro nával lidí. 20Lidé mu oznámili: „Tvoje matka a tvoji bratři stojí venku a chtějí ti něco říci.“ 21Ježíš jim odpověděl: „Moje matka a moji bratři jsou ti, kteří slyší Boží slovo a řídí se podle něho.“

Ježíš utišuje bouři

22Jednoho dne nastoupil Ježíš se svými učedníky na loď a řekl jim: „Přeplavíme se na druhý břeh jezera.“ 23Cestou usnul. Vtom se na jezero přihnala větrná bouře. Vlny se vysoko zvedaly, loď se plnila vodou a hrozilo, že se potopí. 24Učedníci Ježíše vzbudili a volali: „Pane, Pane, utopíme se!“ Ježíš vstal, poručil větru a utišil vlny. 25V nastalém tichu se zeptal učedníků: „Kde zůstala vaše víra?“ Byli celí vyděšení a udivení a říkali si mezi sebou: „Kdo to jen může být, že ho i vítr a vlny poslouchají?“

Ježíš vyhání démony do stáda vepřů

26Plavili se dále do gerasenského kraje, který leží na protějším břehu než Galilea. 27Sotva Ježíš vystoupil na břeh, přiběhl k němu muž z Gerasy, posedlý démony. Již delší dobu pobíhal nahý, potloukal se bez domova a přespával v prázdných skalních hrobech. 28Když uviděl Ježíše, zaječel, vrhl se před ním na zem a křičel: „Co ode mne chceš, Ježíši, synu Nejvyššího Boha? Nech mne na pokoji!“ 29Ježíš přikázal démonu, aby toho muže opustil; záchvaty jej totiž týraly už dlouhou dobu. Lidé ho svazovali na rukou řetězy, na nohy mu nasazovali okovy, ale on měl takovou sílu, že všechno zpřetrhal. Pak se skrýval v pustinách. 30Ježíš se ho zeptal: „Kdo vlastně jsi?“ On odpověděl: „Nás je spousta.“ Byl totiž posedlý mnoha démony. 31Nešťastník teď za ně prosil Ježíše, aby je úplně nezničil. 32Vybrali si stádo vepřů, které se páslo nedaleko na stráni. Když Ježíš dovolil, 33démoni opustili muže a zmocnili se vepřů. Stádo se splašilo a hnalo se po srázu rovnou do jezera, kde utonulo. 34Když to viděli pasáci vepřů, utekli a ve městě i na vesnicích vyprávěli, co se stalo. 35-36Lidé se chtěli na vlastní oči přesvědčit a přišli k Ježíši. U jeho nohou seděl onen muž uzdravený a oblečený, Bylo na něm jasně znát, že má zdravý rozum. Nejvíce lidmi otřáslo vyprávění očitých svědků, jakým způsobem byl ten člověk uzdraven. 37Zmocnil se jich takový strach, že prosili Ježíše, aby jejich krajinu opustil. A tak vstoupil na loď a plavil se zpět. 38Muž, kterého Ježíš uzdravil, prosil, aby ho vzal s sebou. Ježíš odmítl a rozloučil se s ním se slovy: 39„Jdi domů a vypravuj, jak veliké věci s tebou Bůh učinil.“ Muž poslechl, odešel a všude vyprávěl, jaké dobrodiní mu Ježíš prokázal.

Ježíš uzdravuje krvácející ženu a křísí děvče

40Na druhém břehu zatím čekal na Ježíšův návrat zástup lidí. 41Byl mezi nimi také představený synagogy Jairus. Padl Ježíšovi k nohám a prosil, aby šel k němu, 42že jeho jediná, dvanáctiletá dcerka umírá. Cestou se na Ježíše tlačili lidé ze všech stran. 43Byla tam i jedna žena, která již dvanáct let trpěla krvácením, a ačkoliv nechala u lékařů již celé své jmění, nikomu se nepodařilo ji uzdravit. 44Ta se zezadu dotkla třásní Ježíšova pláště a hned ucítila, že její nemoc přestala. 45Ježíš se zeptal: „Kdo se mne to dotkl?“ Nikdo se nepřiznával a Petr řekl: „Pane, vždyť je kolem tebe tolik lidí a ti se na tebe tlačí.“ 46Ježíš na tom však trval: „Někdo se mne úmyslně dotkl, pocítil jsem, že ze mne vyšla síla.“ 47Když žena viděla, že se to nedá tajit, přišla celá rozechvělá k Ježíši a padla na kolena. Přede všemi lidmi mu vyprávěla, proč se ho dotkla a že se v tom okamžiku uzdravila. 48Ježíš jí řekl: „Tvoje víra tě uzdravila. Jdi pokojně domů.“ 49Zatímco Ježíš mluvil, přišel kdosi k Jairovi a sděloval mu: „Tvoje dcera zemřela, už Ježíše neobtěžuj.“ 50Ježíš to slyšel a řekl: „Neboj se, jen věř a tvoje dcerka bude zachráněna.“ 51Když došli k Jairovu domu, vzal s sebou Ježíš dovnitř jen Petra, Jana, Jakuba a rodiče dívenky. 52Tam už nad ní všichni plakali a naříkali. Ježíš řekl: „Neplačte, vždyť neumřela, ale spí.“ 53Hořce se mu vysmáli, protože věděli, že dívka skutečně zemřela. Ježíš všechny poslal ven, 54vzal ji za ruku a zvolal: „Dítě, vstaň!“ 55A ona hned začala dýchat a vstala. Nařídil, aby jí dali něco k jídlu. 56Rodičů se zmocnil úžas a radost. Ježíš jim však nařídil, aby nikomu nevyprávěli, co se stalo.