Luka 4 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 4:1-44

Kuyesedwa kwa Yesu

1Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu, 2kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.

3Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”

4Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’ ”

5Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi. 6Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna. 7Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”

8Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’ ”

9Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano. 10Pakuti kwalembedwa,

“Adzalamulira angelo ake za iwe

kuti akutchinjirize mosamala;

11ndipo adzakunyamula ndi manja awo,

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”

12Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’ ”

13Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.

Yesu Akanidwa ku Nazareti

14Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi. 15Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.

16Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba. 17Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,

18“Mzimu wa Ambuye ali pa Ine;

chifukwa wandidzoza

kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka.

Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe

ndi kwa osaona kuti apenyenso,

kumasulidwa kwa osautsidwa,

19ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”

20Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye, 21ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”

22Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”

23Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”

24Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo. 25Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo. 26Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni. 27Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”

28Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi. 29Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho. 30Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.

Yesu Atulutsa Mzimu Woyipa

31Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu. 32Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.

33Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti 34“Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”

35Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.

36Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!” 37Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.

Yesu Achiritsa Anthu Ambiri

38Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize. 39Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.

40Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa. 41Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.

42Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere. 43Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.” 44Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.

Священное Писание

Лука 4:1-44

Искушение в пустыне

(Мат. 4:1-11; Мк. 1:12-13)

1Иса, исполненный Святого Духа, возвратился с Иордана, и Дух повёл Его в пустыню. 2Там Его сорок дней искушал дьявол. Всё это время Иса ничего не ел и под конец почувствовал сильный голод. 3Тогда дьявол сказал Ему:

– Если Ты Сын Всевышнего (Царственный Спаситель), то прикажи этому камню стать хлебом.

4Иса ответил ему:

– Написано: «Не одним хлебом живёт человек»4:4 Втор. 8:3..

5И дьявол, взяв Его на высокое место, показал Ему в один миг все царства мира.

6И сказал Ему:

– Я передам Тебе всю их власть и славу, потому что они отданы мне, и я даю их кому захочу. 7Итак, если Ты поклонишься мне, всё это будет Твоим.

8Иса ответил:

– Написано: «Поклоняйся Вечному, Богу твоему, и служи Ему одному»4:8 Втор. 6:13..

9После этого дьявол привёл Ису в Иерусалим и поставил Его на самый верх храма.

– Если Ты Сын Всевышнего, – сказал он Ему, – то бросься отсюда вниз. 10Ведь написано же:

«Своим ангелам повелит о Тебе

охранять Тебя,

11и они понесут Тебя на руках,

чтобы ноги Твои не ударились о камень»4:10-11 Заб. 90:11-12..

12А Иса ответил ему:

– Сказано: «Не испытывай Вечного, Бога твоего»4:12 Втор. 6:16..

13Когда дьявол исчерпал все свои искушения, он оставил Ису на время.

Иса Масих начинает Своё служение

(Мат. 4:12-17; Мк. 1:14-15)

14Иса возвратился в Галилею исполненный силой Святого Духа. Молва о Нём распространилась по всей округе. 15Он учил в молитвенных домах, и все прославляли Его.

Отвержение Исы Масиха в Назарете

(Мат. 13:54-58; Мк. 6:1-6)

16Однажды Иса пришёл в Назарет, в город, где Он вырос, и в субботу4:16 Суббота – седьмой день недели у иудеев, который был религиозным днём отдыха. См. пояснительный словарь., как обычно, Он отправился в молитвенный дом иудеев. Там Иса встал, чтобы читать. 17Ему подали свиток со словами пророка Исаии, Он развернул его и нашёл место, где было написано:

18«Дух Вечного на Мне,

потому что Он помазал4:18 Помазал – посредством иудейского обряда помазания человек посвящался на определённое служение. Такого помазания удостаивались пророки, цари и священнослужители. Меня

возвещать бедным Радостную Весть.

Он послал Меня провозглашать свободу пленникам,

прозрение слепым,

освободить угнетённых,

19возвещать время4:19 Букв.: «год». милости Вечного»4:18-19 Ис. 61:1-2..

20Иса свернул свиток, отдал его служителю и сел. Глаза всех находящихся в молитвенном доме были прикованы к Нему. 21Он начал говорить:

– Сегодня, когда вы слушали, исполнились эти слова Писания.

22Все хвалили Его и удивлялись силе Его слов.

– Но разве Он не сын Юсуфа? – спрашивали они.

23Иса сказал им:

– Вы Мне, конечно, напомните пословицу: «Если ты врач, то исцели в начале самого себя!» И скажете Мне: «Мы слышали, что Ты сотворил много чудес в Капернауме, сотвори же и здесь, у Себя на родине, что-либо подобное». 24Но говорю вам истину, ни одного пророка не принимают на его родине. 25Уверяю вас, что во времена Ильяса, когда три с половиной года не было дождя и по всей стране был ужасный голод, в Исраиле было много вдов, 26однако Ильяс не был послан ни к одной из них, а лишь ко вдове в Сарепту4:26 Сарепта – финикийский город, находившийся на территории современного государства Ливан. В те времена там жили народности, не признававшие Всевышнего. близ Сидона4:25-26 См. 3 Цар. 17.. 27Много было в Исраиле прокажённых4:27 На языке оригинала стоит слово, которое обозначает несколько разных кожных болезней, а не только проказу. во времена пророка Елисея, однако ни один из них не был очищен, кроме сирийца Наамана4:27 См. 4 Цар. 5:1-14..

28Все в молитвенном доме иудеев пришли в ярость, когда услышали это. 29Они вскочили, вытащили Ису за пределы города и привели к обрыву горы, на которой был построен город, чтобы сбросить Его вниз. 30Но Иса прошёл сквозь толпу и ушёл.

Изгнание нечистого духа

(Мк. 1:21-28)

31Он пошёл в галилейский город Капернаум и по субботам учил там народ. 32Все изумлялись Его учению, потому что в Его словах ощущалась власть. 33В молитвенном доме иудеев был человек, одержимый демоном, нечистым духом, и вдруг он громко закричал:

34– А-а-а… Что Ты хочешь от нас, Иса из Назарета? Ты пришёл, чтобы погубить нас? Я знаю, кто Ты! Ты – Святой Всевышнего!

35– Замолчи! – строго приказал Иса. – Выйди из него!

Бросив человека перед всеми на землю, демон вышел из него, не причинив ему вреда. 36Все изумлялись и говорили друг другу:

– Что это такое? С такой властью и силой Он приказывает нечистым духам, что они выходят!

37Слух об Исе распространялся по всей округе.

Исцеление больных

(Мат. 8:14-16; Мк. 1:29-34)

38Покинув молитвенный дом иудеев, Иса пошёл в дом Шимона. У тёщи же Шимона в это время был сильный жар, и Ису попросили помочь ей. 39Наклонившись над ней, Иса приказал горячке покинуть женщину, и та оставила её. Она сразу же встала и начала накрывать им на стол.

40Когда же солнце стало клониться к закату, все, у кого были больные различными болезнями, начали приносить их к Исе, и Он возлагал на каждого руки и исцелял их. 41Также и демоны выходили из многих людей с криком:

– Ты – Сын Всевышнего (Царственный Спаситель)!

Но Иса запрещал им и не разрешал говорить, потому что они знали, что Он – Масих4:41 Запрет (не только демонам, но и людям – см. 8:56) говорить о том, Кем Он является, вероятно, был продиктован тем, что люди неверно понимали пророчества о Масихе. Они ждали, что пришедший Масих возглавит восстание против римской оккупации и таким образом установит Своё Царство (см. Ин. 6:15), в то время как Его целью было духовное освобождение от власти греха (см. Ин. 8:31-36; 18:36). Вторая причина – в том, что ещё не пришло Его время открыться (см. Ин. 7:8). К тому же растущая популярность мешала Его служению (см. Мк. 1:43-45). Иса также не хотел, чтобы люди видели в нём только чудотворца-целителя. И, конечно же, Он не хотел принимать свидетельства от демонов..

Иса Масих возвещает Радостную Весть в Иудее

(Мк. 1:35-38)

42На рассвете Иса вышел из города и пошёл в безлюдное место. Люди стали искать Его, и когда нашли, то уговаривали остаться у них. 43Но Иса сказал:

– Я должен возвещать Радостную Весть о Царстве Всевышнего и в других городах, ведь для этого Я и послан.

44И Он проповедовал в молитвенных домах Иудеи.