Luka 20 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 20:1-47

Amufunsa Yesu za Ulamuliro Wake

1Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye. 2Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”

3Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe, 4‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’ ”

5Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’ 6Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”

7Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”

8Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”

Fanizo la Olima Mʼmunda Wamphesa

9Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali. 10Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu. 11Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu. 12Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.

13“Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’

14“Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’ 15Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha.

“Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa? 16Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.”

Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”

17Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti,

“ ‘Mwala umene omanga nyumba anawukana

wasanduka mwala wa pa ngodya.

18Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’ ”

19Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.

Za Kupereka Msonkho kwa Kaisara

20Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza. 21Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi. 22Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”

23Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti, 24“Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”

25Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.”

Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”

26Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.

Za Kuuka kwa Akufa ndi Ukwati

27Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso. 28Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo. 29Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana. 30Wachiwiri 31ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana. 32Pa mapeto pake mkaziyo anafanso. 33Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”

34Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. 35Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. 36Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa. 37Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’ 38Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”

39Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!” 40Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.

Khristu ndi Mwana wa Ndani?

41Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide? 42Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti,

“Ambuye anati kwa Ambuye anga:

‘Khalani ku dzanja langa lamanja,

43mpaka Ine nditasandutsa adani anu

chopondapo mapazi anu?’

44Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”

Achenjeza za Aphunzitsi Amalamulo

45Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake, 46“Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando. 47Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”

Thai New Contemporary Bible

ลูกา 20:1-47

ปัญหาเรื่องสิทธิอำนาจของพระเยซู

(มธ.21:23-27; มก.11:27-33)

1วันหนึ่งขณะพระเยซูทรงสอนประชาชนอยู่ในลานพระวิหารและประกาศข่าวประเสริฐ พวกหัวหน้าปุโรหิต ธรรมาจารย์ และผู้อาวุโสมาหาพระองค์ 2และทูลว่า “จงบอกเราว่าท่านทำสิ่งเหล่านี้โดยอาศัยสิทธิอำนาจใด? ใครให้สิทธิอำนาจนี้แก่ท่าน?”

3พระองค์ตรัสตอบว่า “เราจะถามท่านสักข้อเช่นกัน จงบอกเราว่า 4บัพติศมาของยอห์นมาจากสวรรค์หรือจากมนุษย์?”

5พวกเขาหารือกันว่า “ถ้าเราตอบว่า ‘มาจากสวรรค์’ เขาก็จะถามว่า ‘ทำไมท่านไม่เชื่อยอห์น?’ 6แต่ถ้าเราตอบว่า ‘มาจากมนุษย์’ ประชาชนทั้งปวงก็จะเอาหินขว้างเรา เพราะพวกเขาเชื่อว่ายอห์นเป็นผู้เผยพระวจนะ”

7ดังนั้นพวกเขาจึงทูลตอบว่า “เราไม่ทราบว่ามาจากไหน”

8พระเยซูตรัสว่า “เราก็จะไม่บอกพวกท่านเช่นกันว่าเราอาศัยสิทธิอำนาจใดที่ทำสิ่งเหล่านี้”

คำอุปมาเรื่องผู้เช่าสวน

(มธ.21:33-46; มก.12:1-12)

9แล้วพระองค์ตรัสคำอุปมาให้ประชาชนฟังว่า “ชายคนหนึ่งทำสวนองุ่นให้ชาวสวนเช่า แล้วจากไปต่างแดนเสียนาน 10เมื่อถึงฤดูเก็บเกี่ยว เขาก็ส่งคนรับใช้ไปหาผู้เช่าเพื่อรับส่วนแบ่งของผลผลิตจากสวนองุ่น แต่พวกผู้เช่าทุบตีและไล่คนรับใช้นั้นกลับมามือเปล่า 11เขาส่งคนรับใช้อีกคนไป พวกเขาก็ทุบตีคนรับใช้นั้น ทำให้อับอายขายหน้า และไล่กลับมามือเปล่าอีก 12เขายังส่งคนที่สามไปอีก พวกนั้นก็ทำร้ายคนรับใช้นั้นและโยนออกมา

13“แล้วเจ้าของสวนองุ่นจึงกล่าวว่า ‘เราจะทำอย่างไรดี? เราจะส่งบุตรชายที่รักของเราไป บางทีพวกนั้นจะเคารพเขา’

14“แต่เมื่อผู้เช่าเห็นบุตรชายของเจ้าของสวนก็ปรึกษากันว่า ‘นี่ไงทายาท ให้เราฆ่าเขา แล้วมรดกจะตกเป็นของเรา’ 15ดังนั้นพวกเขาจึงจับบุตรชายเจ้าของสวนโยนออกมานอกสวนองุ่นแล้วฆ่า

“แล้วเจ้าของสวนจะทำอย่างไรกับคนพวกนั้น? 16เขาย่อมจะมาฆ่าพวกผู้เช่าเหล่านั้น และให้คนอื่นเช่าสวนองุ่นนี้”

เมื่อประชาชนได้ยินดังนี้ก็ทูลว่า “ขออย่าให้เป็นเช่นนั้นเลย!”

17พระเยซูทอดพระเนตรตรงไปที่พวกเขาและตรัสว่า “ก็แล้วที่เขียนไว้นั้นหมายความว่าอย่างไร? ที่ว่า

“ ‘ศิลาซึ่งช่างก่อได้ทิ้งแล้ว

บัดนี้กลับกลายเป็นศิลามุมเอก20:17 หรือศิลาหัวมุม20:17 สดด.118:22

18ทุกคนที่ตกทับศิลานั้นจะแหลกเป็นชิ้นๆ แต่ศิลานี้ตกทับผู้ใด ผู้นั้นจะแหลกลาญ”

19พวกธรรมาจารย์และพวกหัวหน้าปุโรหิตหาทางจะจับกุมพระองค์ทันที เพราะรู้ว่าพระองค์ตรัสคำอุปมานี้ว่าพวกตน แต่พวกเขากลัวประชาชน

การเสียภาษีแก่ซีซาร์

(มธ.22:15-22; มก.12:13-17)

20พวกเขาจับตาดูพระองค์อย่างใกล้ชิดโดยส่งคนสอดแนมซึ่งแสร้งทำเป็นคนซื่อตรงมา หวังจะจับผิดถ้อยคำของพระเยซู จะได้มอบพระองค์ไว้ในอำนาจและการพิพากษาของผู้ว่าการ 21คนสอดแนมนั้นจึงมาทูลถามพระองค์ว่า “ท่านอาจารย์ เรารู้ว่าท่านพูดและสอนสิ่งที่ถูกต้อง ไม่เข้าข้างใคร แต่สอนทางของพระเจ้าตามความจริง 22เป็นการถูกต้องหรือไม่ที่เราจะเสียภาษีให้แก่ซีซาร์?”

23พระเยซูทรงรู้ทันอุบายของพวกเขา จึงตรัสว่า 24“ไหนเอาเงินหนึ่งเหรียญเดนาริอันมาให้เราดูซิ รูปและคำจารึกบนเหรียญเป็นของใคร?”

25พวกเขาทูลว่า “ของซีซาร์” พระองค์จึงตรัสว่า “ของของซีซาร์จงให้แก่ซีซาร์ และของของพระเจ้าจงถวายแด่พระเจ้า”

26พวกเขาไม่สามารถจับผิดสิ่งที่พระองค์ตรัสต่อสาธารณชนได้ และต้องนิ่งอึ้งเพราะประหลาดใจในคำตอบของพระองค์

เรื่องการเป็นขึ้นจากตายและการแต่งงาน

(มธ.22:23-33; มก.12:18-27)

27บางคนในพวกสะดูสีซึ่งกล่าวว่าไม่มีการเป็นขึ้นจากตาย มาทูลถามพระเยซูว่า 28“ท่านอาจารย์ โมเสสเขียนสั่งพวกเราไว้ว่า ถ้าชายใดเสียชีวิตไปโดยไม่มีบุตร พี่ชายหรือน้องชายของเขาต้องแต่งงานกับภรรยาม่ายเพื่อจะมีบุตรสืบสกุลให้ผู้นั้น 29คราวนี้มีพี่น้องเจ็ดคน พี่คนโตแต่งงานแล้วตายไปโดยไม่มีบุตร 30คนที่สอง 31และจากนั้นคนที่สามได้รับนางมาเป็นภรรยา และเป็นอย่างนั้นถัดมาเรื่อยๆ จนถึงคนที่เจ็ด ทั้งหมดล้วนตายโดยไม่มีบุตร 32ในที่สุดหญิงนั้นก็ตายด้วย 33แล้วเมื่อเป็นขึ้นจากตาย หญิงนี้จะเป็นภรรยาของใคร ในเมื่อทั้งเจ็ดคนล้วนได้นางเป็นภรรยา?”

34พระเยซูทรงตอบว่า “คนยุคนี้แต่งงาน ยกให้เป็นสามีภรรยากัน 35แต่ผู้ที่สมควรมีส่วนในยุคนั้นและในการเป็นขึ้นจากตาย จะไม่แต่งงานหรือยกให้เป็นสามีภรรยากัน 36และพวกเขาจะไม่ตายอีกเลย เพราะจะเป็นเหมือนทูตสวรรค์ พวกเขาเป็นบุตรของพระเจ้าเนื่องจากเป็นบุตรแห่งการเป็นขึ้นจากตาย 37แต่ในเรื่องพุ่มไม้นั้น แม้กระทั่งโมเสสยังแสดงให้เห็นว่าคนตายเป็นขึ้นมาใหม่ เพราะเขาเรียกองค์พระผู้เป็นเจ้าว่า ‘พระเจ้าของอับราฮัม พระเจ้าของอิสอัค และพระเจ้าของยาโคบ’20:37 อพย.3:6 38พระองค์ไม่ใช่พระเจ้าของคนตาย แต่เป็นพระเจ้าของคนเป็น เพราะสำหรับพระองค์แล้ว คนทั้งปวงเป็นอยู่”

39ธรรมาจารย์บางคนทูลว่า “ท่านอาจารย์ ท่านพูดดีแล้ว!” 40และไม่มีใครกล้าทูลถามพระองค์อีก

พระคริสต์เป็นบุตรของใคร

(มธ.22:41—23:7; มก.12:35-40)

41จากนั้นพระเยซูตรัสกับพวกเขาว่า “เป็นไปได้อย่างไรที่พวกเขาบอกว่าพระคริสต์20:41 หรือพระเมสสิยาห์เป็นบุตรของดาวิด? 42ดาวิดเองได้ประกาศไว้ในพระธรรมสดุดีว่า

“ ‘พระเจ้าตรัสกับองค์พระผู้เป็นเจ้า

ของข้าพเจ้าว่า

“จงนั่งที่ขวามือของเรา

43จนกว่าเราจะทำให้ศัตรูของเจ้า

เป็นแท่นวางเท้าของเจ้า” ’20:43 สดด.110:1

44ในเมื่อดาวิดเรียกพระองค์ว่า ‘องค์พระผู้เป็นเจ้า’ แล้วพระองค์จะเป็นบุตรของดาวิดได้อย่างไร?”

45ขณะประชาชนทั้งปวงกำลังฟังอยู่ พระเยซูตรัสกับเหล่าสาวกของพระองค์ว่า 46“จงระวังพวกธรรมาจารย์ พวกเขาชอบใส่เสื้อชุดยาวเดินไปมา ชอบให้ผู้คนมาคำนับทักทายในย่านตลาด ชอบนั่งในที่ที่สำคัญที่สุดในธรรมศาลาและที่อันทรงเกียรติในงานเลี้ยง 47เขาริบบ้านของหญิงม่าย และแสร้งอธิษฐานยืดยาวให้คนเห็น คนเช่นนี้จะถูกลงโทษอย่างหนักที่สุด”