Luka 18 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 18:1-43

Fanizo la Mayi Wakhama pa Kupempha

1Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke. 2Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu. 3Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’

4“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu, 5koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’ ”

6Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena. 7Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira? 8Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”

Fanizo la Mfarisi ndi Wolandira Msonkho

9Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse. 10“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho. 11Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu. 12Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’

13“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’

14“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”

Yesu Adalitsa Ana Aangʼono

15Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula. 16Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere. 17Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”

Munthu Wachuma ndi Ufumu wa Mulungu

18Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?”

19Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha. 20Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’ ”

21Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”

22Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”

23Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri. 24Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu! 25Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”

26Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”

27Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”

28Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”

29Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu 30adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.”

Yesu Aneneratu za Imfa Yake Kachitatu

31Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa. 32Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira, 33adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”

34Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.

Yesu Achiritsa Wosaona

35Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha, 36anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika. 37Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”

38Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”

39Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”

40Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti, 41“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?”

Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”

42Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.” 43Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.

Thai New Contemporary Bible

ลูกา 18:1-43

คำอุปมาเรื่องหญิงม่ายผู้ไม่ลดละ

1แล้วพระเยซูตรัสคำอุปมาสอนเหล่าสาวกให้อธิษฐานเสมออย่างไม่ลดละ 2พระองค์ตรัสว่า “ในเมืองหนึ่งมีผู้พิพากษาคนหนึ่งซึ่งไม่เกรงกลัวพระเจ้าและไม่เห็นแก่หน้ามนุษย์คนใด 3ในเมืองนั้นมีหญิงม่ายคนหนึ่งที่เพียรมาหาเขา และพร่ำวิงวอนว่า ‘กรุณาให้ความยุติธรรมในคดีของข้าพเจ้าด้วยเถิด’

4“ผู้พิพากษานั้นปฏิเสธนางอยู่ระยะหนึ่ง แต่ในที่สุดเขานึกในใจว่า ‘ถึงแม้เราไม่เกรงกลัวพระเจ้า และไม่เห็นแก่หน้ามนุษย์คนใด 5แต่เพราะหญิงม่ายคนนี้คอยกวนใจเราอยู่ตลอดเวลา เราจะให้ความยุติธรรมแก่นาง เพื่อนางจะได้ไม่มารบกวนให้เราระอาใจ!’ ”

6และองค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสว่า “จงฟังคำพูดของผู้พิพากษาอยุติธรรมคนนี้ 7แล้วพระเจ้าจะไม่ให้ความยุติธรรมแก่ผู้ที่พระองค์ทรงเลือกสรรหรือ? ในเมื่อเขาร้องทูลพระองค์ทั้งวันทั้งคืน พระองค์จะทรงผัดผ่อนเขาอยู่ร่ำไปหรือ? 8เราบอกท่านว่า พระองค์จะทรงดูแลให้พวกเขาได้รับความยุติธรรมโดยเร็ว แต่เมื่อบุตรมนุษย์เสด็จมา พระองค์จะพบความเชื่อในโลกหรือ?”

คำอุปมาเรื่องฟาริสีกับคนเก็บภาษี

9สำหรับบางคนที่มั่นใจในความชอบธรรมของตนเองและดูถูกคนอื่นทั้งปวงนั้น พระเยซูตรัสคำอุปมานี้ว่า 10“ชายสองคนไปที่พระวิหารเพื่ออธิษฐาน คนหนึ่งเป็นฟาริสี และอีกคนหนึ่งเป็นคนเก็บภาษี 11ฟาริสีคนนั้นยืนขึ้นอธิษฐานเกี่ยวกับ18:11 หรือต่อ ตนเองว่า ‘ข้าแต่พระเจ้าขอบพระคุณพระองค์ ที่ข้าพระองค์ไม่เหมือนคนอื่นๆ ที่เป็นโจรปล้น ทำชั่ว ล่วงประเวณี หรือเป็นอย่างคนเก็บภาษีคนนี้ 12ข้าพระองค์ถืออดอาหารสัปดาห์ละสองครั้ง และถวายสิบลดจากทุกสิ่งที่ได้มา’

13“แต่คนเก็บภาษีนั้นยืนไกลออกไป เขาไม่กล้าแม้แต่จะเงยหน้าขึ้นฟ้า แต่ทุบตีอกของตนและพูดว่า ‘ข้าแต่พระเจ้า ขอทรงเมตตาข้าพระองค์ผู้เป็นคนบาปด้วยเถิด’

14“เราบอกท่านว่า คนนี้ต่างหากที่กลับบ้านไปโดยถือว่าเป็นผู้ชอบธรรมต่อหน้าพระเจ้า เพราะทุกคนที่ยกตนเองขึ้นจะถูกทำให้ต่ำลง และผู้ที่ถ่อมตนลงจะได้รับการเชิดชูขึ้น”

พระเยซูกับเด็กเล็กๆ

(มธ.19:13-15; มก.10:13-16)

15ประชาชนอุ้มทารกมาให้พระเยซูทรงแตะต้อง เมื่อเหล่าสาวกเห็นก็ตำหนิพวกเขา 16แต่พระเยซูทรงเรียกเด็กๆ เข้ามาหาพระองค์และตรัสว่า “จงให้เด็กเล็กๆ มาหาเราและอย่าขัดขวางเขาเลย เพราะอาณาจักรของพระเจ้าเป็นของคนที่เป็นเหมือนเด็กๆ เหล่านี้ 17เราบอกความจริงแก่ท่านว่า ผู้ใดไม่รับอาณาจักรของพระเจ้าเหมือนเด็กเล็กๆ ผู้นั้นจะไม่มีวันได้เข้าอาณาจักรพระเจ้าเลย”

ขุนนางผู้ร่ำรวย

(มธ.19:16-29; มก.10:17-30)

18ขุนนางคนหนึ่งทูลถามพระองค์ว่า “ท่านอาจารย์ผู้ประเสริฐ ข้าพเจ้าจะต้องทำอะไรบ้างจึงจะได้ชีวิตนิรันดร์?”

19พระเยซูตรัสตอบว่า “ทำไมท่านจึงบอกว่าเราประเสริฐ? นอกจากพระเจ้าแล้ว ไม่มีใครอื่นที่ประเสริฐ 20ท่านก็รู้บทบัญญัติที่ว่า ‘อย่าล่วงประเวณี อย่าฆ่าคน อย่าลักขโมย อย่าเป็นพยานเท็จ จงให้เกียรติบิดามารดาของเจ้า’18:20 อพย.20:12-16ฉธบ.5:16-20

21เขาทูลว่า “ทั้งหมดนี้ ข้าพเจ้าถือปฏิบัติมาตั้งแต่เด็ก”

22เมื่อพระเยซูทรงได้ยินดังนั้น ก็ตรัสกับเขาว่า “ท่านยังขาดอยู่อย่างหนึ่ง จงขายทุกสิ่งที่มีและแจกจ่ายให้คนยากจน แล้วท่านจะมีทรัพย์สมบัติในสวรรค์ จากนั้นจงตามเรามา”

23เมื่อเขาได้ยินเช่นนั้นก็เศร้าสลด เพราะเขาร่ำรวยมาก 24พระเยซูทรงมองดูเขาและตรัสว่า “ยากนักที่คนรวยจะเข้าอาณาจักรของพระเจ้า! 25อันที่จริง ให้อูฐลอดรูเข็มยังง่ายกว่าที่คนรวยจะเข้าอาณาจักรของพระเจ้า”

26บรรดาผู้ที่ได้ฟังเช่นนี้ทูลถามว่า “ถ้าเช่นนั้น ใครจะรอดได้?”

27พระเยซูตรัสตอบว่า “สิ่งที่เป็นไปไม่ได้สำหรับมนุษย์ เป็นไปได้สำหรับพระเจ้า”

28เปโตรทูลว่า “ข้าพระองค์ทั้งหลายได้ละทุกสิ่งที่มีมาติดตามพระองค์!”

29พระเยซูตรัสแก่พวกเขาว่า “เราบอกความจริงแก่พวกท่านว่า ไม่มีผู้ใดที่ละทิ้งบ้านเรือน หรือภรรยา หรือพี่น้อง หรือบิดามารดา หรือลูกๆ เพื่ออาณาจักรของพระเจ้า 30แล้วจะไม่ได้รับผลตอบแทนหลายเท่าในยุคนี้ และชีวิตนิรันดร์ในยุคหน้า”

ทรงพยากรณ์อีกว่าจะต้องสิ้นพระชนม์

(มธ.20:17-19; มก.10:32-34)

31พระเยซูทรงพาสาวกทั้งสิบสองคนเลี่ยงออกมาและตรัสบอกพวกเขาว่า “พวกเรากำลังขึ้นไปยังกรุงเยรูซาเล็ม และทุกอย่างที่บรรดาผู้เผยพระวจนะเขียนไว้เกี่ยวกับบุตรมนุษย์จะสำเร็จ 32พระองค์จะถูกมอบให้คนต่างชาติ พวกเขาจะเยาะเย้ย ดูหมิ่น ถ่มน้ำลายรด โบยตี และฆ่าพระองค์ 33ในวันที่สามพระองค์จะเป็นขึ้นมาใหม่”

34เหล่าสาวกไม่เข้าใจสิ่งเหล่านี้เลย ความหมายของสิ่งเหล่านี้ถูกปิดบังจากพวกเขาและพวกเขาไม่รู้ว่าพระองค์กำลังตรัสถึงเรื่องอะไร

ขอทานตาบอดมองเห็น

(มธ.20:29-34; มก.10:46-52)

35เมื่อพระเยซูเสด็จมาใกล้เมืองเยรีโค มีชายตาบอดคนหนึ่งกำลังนั่งขอทานอยู่ริมทาง 36เมื่อได้ยินเสียงฝูงชนเดินผ่าน เขาจึงถามว่าเกิดอะไรขึ้น 37คนเหล่านั้นบอกเขาว่า “พระเยซูแห่งนาซาเร็ธกำลังเสด็จผ่าน”

38ชายตาบอดคนนั้นจึงร้องขึ้นว่า “พระเยซูบุตรดาวิดเจ้าข้า เมตตาข้าพระองค์ด้วยเถิด!”

39บรรดาผู้ที่เดินนำหน้าตำหนิและบอกให้เขาเงียบ แต่เขายิ่งร้องดังขึ้นอีกว่า “บุตรดาวิดเจ้าข้า เมตตาข้าพระองค์ด้วยเถิด!”

40พระเยซูทรงหยุดและตรัสสั่งให้คนพาเขามาหาพระองค์ เมื่อเขาเข้ามาใกล้พระเยซูตรัสถามว่า 41“ท่านต้องการให้เราทำอะไรให้?”

เขาทูลว่า “พระองค์เจ้าข้า ข้าพระองค์อยากมองเห็น”

42พระเยซูตรัสกับเขาว่า “จงมองเห็นเถิด ความเชื่อของท่านทำให้ท่านหายแล้ว” 43ทันใดนั้นเขาก็มองเห็นได้และตามพระเยซูไป พร้อมกับสรรเสริญพระเจ้า เมื่อคนทั้งปวงเห็นเช่นนั้นก็สรรเสริญพระเจ้าด้วย