Luka 14 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 14:1-35

Yesu Mʼnyumba ya Mfarisi

1Pa tsiku lina la Sabata, Yesu atapita kukadya ku nyumba ya Mfarisi wodziwika, Afarisi anamulonda mosamalitsa. 2Poteropo, patsogolo pake panali munthu amene anadwala matenda otupa mimba ndi miyendo. 3Yesu anafunsa Afarisi ndi akatswiri amalamulo kuti, “Kodi ndi zololedwa kuchiritsa pa tsiku la Sabata kapena ayi?” 4Koma iwo sanayankhe. Tsono atamutenga munthuyo, Iye anamuchiritsa ndipo anamuwuza kuti azipita.

5Kenaka Iye anawafunsa kuti, “Kodi ngati mmodzi mwa inu ali ndi mwana wamwamuna kapena ngʼombe imene yagwera mʼchitsime tsiku la Sabata, kodi simungamuvuwulemo tsiku lomwelo?” 6Ndipo iwo analibe choyankha.

Kudzichepetsa ndi Kulandira Ulemu

7Iye ataona momwe alendo amasankhira malo aulemu pa tebulo, Iye anawawuza fanizo ili: 8“Pamene wina wakuyitanani ku phwando la ukwati, musakhale pa malo aulemu ayi, chifukwa mwina anayitananso munthu wina wolemekezeka kuposa inu. 9Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika. 10Koma akakuyitanani, khalani pa malo otsika, kuti amene anakuyitanani uja adzakuwuzeni kuti, ‘Bwenzi, bwera udzakhale pa malo aulemu pano.’ Pamenepo inu mudzalandira ulemu pamaso pa alendo anzanu onse. 11Pakuti aliyense wodzikuza adzamuchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamukweza.”

12Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako. 13Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona. 14Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”

Fanizo la Phwando Lalikulu

15Mmodzi mwa amene amadya naye atamva izi, anati kwa Yesu, “Ndi wodala munthu amene adzadye nawo mu ufumu wa Mulungu.”

16Yesu anayankha kuti, “Munthu wina ankakonza phwando lalikulu ndipo anayitana alendo ambiri. 17Nthawi yaphwando itakwana anatuma wantchito wake kuti akawuze onse amene anayitanidwa kuti, ‘Bwerani, pakuti zonse zakonzeka.’

18“Koma onse anayamba kupereka zifukwa mofanana. Woyamba anati, ‘Ine ndangogula kumene munda, ndipo ndikuyenera kupita kuti ndikawuone. Pepani mundikhululukire.’

19“Wina anati, ‘Ndangogula kumene ngʼombe khumi zokoka ngolo ndipo kupita kukaziyesa. Pepani mundikhululukire.’

20“Wina anatinso, ‘Ine ndangokwatira kumene, choncho sinditha kubwera.’

21“Wantchitoyo anabwera ndikudzamuwuza bwana wakeyo zimenezi. Pamenepo mphwandoyo anapsa mtima ndipo analamula wantchito wakeyo kuti, ‘Pita msangamsanga kunja mʼmisewu ndi mʼmakwalala a mu mzinda ndipo ukabweretse osauka, ofa ziwalo, osaona ndi olumala.’

22“Wantchitoyo anati, ‘Bwana, zimene munanena zachitika koma malo akanalipobe.’

23“Ndipo mbuye uja anawuza wantchito wake kuti, ‘Pita kunja ku misewu ikuluikulu ndi kunja kwa mpanda ndipo ukawawuze kuti alowe, kuti nyumba yanga idzaze. 24Ine ndikukuwuzani inu kuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anayitanidwa adzalawa phwandolo.’ ”

Dipo la Kutsatira Yesu

25Gulu lalikulu la anthu linkayenda naye Yesu ndipo atatembenukira kwa iwo anati, 26“Ngati wina aliyense abwera kwa Ine ndipo sadana ndi abambo ndi amayi ake, mkazi wake ndi ana, abale ake ndi alongo ake, inde ngakhale moyo wake omwe, iye sangakhale ophunzira wanga. 27Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake ndi kunditsata Ine sangakhale ophunzira wanga.

28“Taganizani, ngati wina mwa inu akufuna kumanga nsanja, kodi iye sayamba wakhala pansi ndi kuganizira za mtengo wake kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kuti atsirizire? 29Pakuti ngati ayika maziko ndi kulephera kutsiriza, aliyense amene adzayiona adzamuseka, 30nanena kuti, ‘Munthu uyu anayamba kumanga koma sanathe kutsiriza.’

31“Kapena mfumu imene ikupita ku nkhondo kukamenyana ndi mfumu ina, kodi siyamba yakhala pansi ndi kulingalira ngati ingathe ndi anthu 10,000 kulimbana ndi amene akubwera ndi 20,000? 32Ngati singathe, idzatuma nthumwi pomwe winayo ali kutali ndi kukapempha mgwirizano wamtendere. 33Mʼnjira yomweyo, wina aliyense wa inu amene sasiya zonse ali nazo sangakhale ophunzira wanga.

34“Mchere ndi wabwino, koma ngati usukuluka adzawukoleretsanso ndi chiyani? 35Suyeneranso ngakhale mʼnthaka kapena kudzala la manyowa; umatayidwa kunja.

“Amene ali ndi makutu akumva, amve.”

Habrit Hakhadasha/Haderekh

הבשורה על-פי לוקס 14:1‏-35

1‏-2מנהיג פרושי אחד הזמין את ישוע לסעוד בביתו בשבת. האורחים האחרים שהיו בבית הפרוש הביטו בישוע בתשומת לב מרובה, כי רצו לראות אם ירפא איש חולה שהיה איתם. לאיש הייתה מחלה שמנפחת את הגוף בגלל עודף נוזלים. 3ישוע פנה אל הפרושים ואל חכמי־התורה ושאל: ”האם מותר לרפא חולה בשבת או אסור?“ 4משלא ענו לשאלתו אחז ישוע ביד החולה, ריפא אותו ושלח אותו לדרכו.

5לאחר מכן פנה ישוע אל הנוכחים ואמר: ”מי מכם אינו עובד בשבת? אם החמור או השור שלכם ייפול בשבת לתוך באר, לא תמהרו לחלץ אותו?“ 6גם הפעם לא השיבו לו. 7ישוע שם לב לכך שכל אחד מהאורחים בבית הפרוש השתדל לתפוס מקום ישיבה מכובד, ולכן אמר להם: 8”אם הוזמנת לחתונה, אל תשב בראש השולחן, שמא יבוא אורח חשוב ממך, 9ואז יבוא המארח ויבקש ממך לפנות את מקומך לאורח הנכבד. בבושת פנים תאלץ לקום ולשבת בפינה, היכן שנותר כיסא פנוי.

10”נהג כך: בבואך לחתונה שב בפינה. כשיראה אותך המארח הוא יבוא ויאמר: ’ידידי היקר, מדוע אתה יושב בפינה? עליך לשבת במקום נכבד יותר!‘ וכך תכובד לעיני כל האורחים. 11כי מי שמכבד את עצמו יושפל ומי שמשפיל את עצמו יכובד.“ 12לאחר מכן פנה ישוע אל מארחו ואמר: ”כשאתה עורך סעודה אל תזמין את חבריך, אחיך, קרוביך או שכניך העשירים, כי יש להניח שהם יזמינו אותך לסעוד בביתם, וכך תקבל את גמולך המלא. 13הזמן במקומם את העניים, הצולעים, בעלי המום והעיוורים. 14אמנם אין באפשרותם להשיב לך כגמולך, אך בתחיית המתים אלוהים עצמו ישלם ויגמול לך ולכל עושה טוב.“

15אחד מהמסובים, שהקשיב בתשומת לב לדברי ישוע, קרא: ”זכות גדולה היא להשתתף בסעודת מלכות האלוהים!“

16ישוע ענה לו במשל: ”איש אחד ערך סעודה גדולה והזמין אורחים רבים. 17כאשר הושלמו ההכנות שלח את עבדו להודיע למוזמנים שהסעודה מוכנה. 18אך כל אחד מהמוזמנים מצא תירוץ וסיבה שלא לבוא. האחד אמר: ’אני באמת מצטער שאיני יכול לבוא, זה עתה קניתי חלקת אדמה ואני מוכרח ללכת לבדוק אותה‘. 19השני אמר: ’הבוקר קניתי חמישה צמדי שוורים, ואני מוכרח ללכת לראות איך הם עובדים, קבל בבקשה את התנצלותי‘. 20השלישי בדיוק נשא אישה, ולכן לא השתתף בסעודה.

21”העבד חזר אל אדוניו ומסר לו את דברי המוזמנים השונים. אדוניו התרגז מאוד וביקש מהעבד למהר אל הרחובות ואל הסמטאות ולהזמין את העניים, בעלי המום, העיוורים והפיסחים. 22העבד מילא את רצון אדוניו, אך עדיין היה מקום לאורחים נוספים.

23” ’לך אל הסמטאות, אל השבילים ואל מקומות־מחבוא‘, אמר בעל הבית לעבדו, ’והפצר בקבצנים ובנוודים לבוא לסעודה, כדי שהבית יתמלא עד אפס מקום. 24איש מהמוזמנים הראשונים לא יטעם מהסעודה שלי!‘ “

25כשהלך אחריו קהל גדול, פנה ישוע לאחור ודיבר אל האנשים: 26”מי שרוצה ללכת בעקבותיי עליו לאהוב אותי יותר מאשר את אביו, אמו, אשתו, ילדיו, אחיו ואחיותיו – אפילו יותר מחייו – אחרת לא יוכל להיות תלמיד שלי. 27מי שאינו נושא את צלבו ואינו בא אחרי איננו יכול להיות תלמידי. 28עליכם לחשוב ולשקול היטב לפני שאתם מחליטים ללכת אחרי. אם ברצונך לבנות בית, האם לא תשב תחילה ותחשב את המחיר, כדי לראות אם יש באפשרותך להשלים את הבנייה? 29אם לא תחשב את המחיר תיווכח, לאחר שתניח את היסודות, שאין לך מספיק כסף ולא תוכל להשלים את הבניין. כל מי שיראה את המבנה הלא־גמור ילעג לך ויאמר: 30’האיש הזה התחיל לבנות בית, אבל הפסיק באמצע משום שלא היה מספיק כסף!‘

31”או איזה מלך יאיים במלחמה נגד מלך אחר, לפני שיישב תחילה וישקול בכובד ראש אם צבאו המונה 10,000 חיילים, מסוגל להביס את 20,000 חיילי האויב? 32אם יגיע למסקנה שאין לו סיכוי לנצח הוא ישלח אל יריבו שליחים, לפני שיהיה מאוחר מדי, ויבקש לערוך משא ומתן לשלום. 33גם אתם צריכים לחשוב ולשקול היטב לפני שאתם מחליטים ללכת אחרי. מי שאינו מוכן לוותר על כל רכושו למעני לא יוכל להיות תלמידי.

34”מלח הוא דבר מועיל, אבל אם הוא מאבד את מליחותו, כיצד ניתן להשיב לו את טעמו? 35מלח חסר־טעם אינו מביא כל תועלת – אי־אפשר להשתמש בו אפילו כדשן. מי שמסוגל לשמוע שיקשיב.“