Luka 13 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 13:1-35

Za Kutembenuka Mtima

1Nthawi yomweyo panali ena amene analipo omwe amamuwuza Yesu za Agalileya amene magazi awo Pilato anawasakaniza ndi nsembe zawo. 2Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuganiza kuti Agalileya amenewa anali ochimwa kwambiri kuposa Agalileya ena onse chifukwa anavutika mʼnjira iyi? 3Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse. 4Kapena anthu 18 aja amene anafa nsanja ya Siloamu itawagwera, kodi mukuganiza kuti iwo aja anali ochimwa kwambiri kuposa onse amene amakhala mu Yerusalemu? 5Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.”

6Kenaka Iye anawawuza fanizo kuti, “Munthu wina anali ndi mtengo wamkuyu, umene anadzala mʼmunda wamphesa, ndipo Iye anapita kukayangʼana zipatso, koma sanazipeze. 7Tsono kwa munthu amene amasamalira munda wamphesawo anati, ‘Kwa zaka zitatu tsopano ndakhala ndikubwera kudzafuna chipatso pa mtengo uwu ndipo sindinachipeze. Udule! Nʼchifukwa chiyani ukuwononga nthaka?’

8“Munthuyo anayankha kuti, ‘Bwana, tawusiyani kwa chaka chimodzi chokha ndipo ine ndikumba ngalande mozungulira ndi kuthira manyowa. 9Ngati udzabale zipatso chaka chamawa, zili bwino! Koma ngati sudzabala, pamenepo mudzawudule.’ ”

Mayi Wokhota Msana Achiritsidwa pa Sabata

10Pa Sabata Yesu ankaphunzitsa mʼsunagoge ina, 11ndipo momwemo munali mayi amene anali ndi mzimu woyipa umene unamudwalitsa zaka 18. Iye anali wokhota msana ndipo samatha kuweramuka ndi pangʼono pomwe. 12Yesu atamuona anamuyitana kutsogolo ndipo anati kwa iye, “Amayi, mwamasulidwa ku mavuto.” 13Kenaka anasanjika manja ake pa iye, ndipo nthawi yomweyo anawongoka nayamika Mulungu.

14Chifukwa cha kuyipidwa kuti Yesu anachiritsa pa Sabata, wolamulira sunagoge anati kwa anthu, “Pali masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito. Choncho bwerani kuti mudzachiritsidwe masiku amenewo osati pa Sabata.”

15Ambuye anamuyankha kuti, “Iwe wachiphamaso! Kodi nonsenu simumasula pa Sabata ngʼombe zanu kapena bulu kumuchotsa mʼkhola ndi kupita naye kukamupatsa madzi? 16Nanga mayiyu, amene ndi mwana wa Abrahamu, ndipo anamangidwa ndi Satana zaka 18, kodi siwoyenera kuti amasulidwe msinga imeneyi pa tsiku la Sabata?”

17Atanena izi, onse omutsutsa anachititsidwa manyazi, koma anthu anakondwera ndi zodabwitsa zonse zimene Iye anazichita.

Fanizo la Mbewu ya Mpiru ndi la Yisiti

18Kenaka Yesu anafunsa kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani? Kodi Ine ndingawufanizire ndi chiyani? 19Uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake. Inakula, nʼkukhala mtengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinakhala mʼnthambi zake.”

20Iye anafunsanso kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu ndingawufanizire ndi chiyani? 21Uli ngati yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza ndi ufa wambiri mpaka anafufumitsa ufawo.”

Khomo Lopapatiza

22Ndipo Yesu anayendayenda mʼmizinda ndi mʼmidzi, kumaphunzitsa pamene Iye ankapita ku Yerusalemu. 23Wina anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndi anthu ochepa okha amene adzapulumutsidwe?”

Iye anawawuza kuti, 24“Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza, chifukwa ndikukuwuzani kuti ambiri adzafuna kulowa koma sadzatha kutero. 25Nthawi yomwe mwini nyumba adzayimirira ndi kutseka chitseko, inu mudzayima kunja kugogoda ndi kudandaula kuti, ‘Bwana, tatitsekulirani khomo.’

“Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera.’

26“Ndipo inu mudzati, tinkadya ndi kumwa ndi inu ndipo munkaphunzitsa mʼmisewu yathu.

27“Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera. Chokereni inu nonse ochita zoyipa!’

28“Mudzalira ndi kukuta mano mukadzaona Abrahamu, Isake ndi Yakobo ndi aneneri onse ali mu ufumu wa Mulungu koma inuyo mutaponyedwa kunja. 29Anthu adzachokera kummawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kummwera, kudzakhala pa phwando mu ufumu wa Mulungu. 30Ndithudi otsirizira ndiye adzakhale oyambirira, ndipo oyambirira ndiye adzakhale otsirizira.”

Yesu Amvera Chisoni Yerusalemu

31Pa nthawi imeneyo Afarisi anabwera kwa Yesu ndipo anati kwa Iye, “Chokani malo ano ndipo pitani kumalo ena aliwonse. Herode akufuna kukuphani.”

32Iye anayankha kuti, “Pitani kawuzeni nkhandweyo, Ine ndikutulutsa ziwanda ndi kuchiritsa anthu lero ndi mawa ndipo tsiku lachitatu ndidzakwaniritsa cholinga changa.” 33Mʼnjira ina iliyonse, Ine ndiyenera kupitirira ulendo wanga lero, mawa ndi mkuja. Zoona nʼzakuti mneneri sangafere kunja kwa Yerusalemu.

34Iwe Yerusalemu, Yerusalemu! Umapha aneneri ndi kuwagenda miyala anthu amene atumizidwa kwa iwe. Nthawi zambiri ndakhala ndikufuna kusonkhanitsa ana ako pamodzi, monga nkhuku imasonkhanitsira anapiye pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune! 35Taona, nyumba yako yasanduka bwinja. Ine ndikukuwuza kuti, sudzandionanso mpaka pamene udzati, “Wodala amene akubwera mʼdzina la Ambuye!”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Лука 13:1-35

Призыв к покаянию

1Некоторые из тех, кто слушал Ису, рассказали Ему о галилеянах, которых Пилат приказал убить в храме в то время, когда они совершали жертвоприношение. 2Иса ответил:

– Вы думаете, что эти галилеяне так пострадали, потому что они были грешнее всех других галилеян? 3Нет! Но говорю вам, если вы не раскаетесь, вы тоже погибнете, как они. 4Или взять тех восемнадцать человек, которые погибли, когда на них упала Силоамская башня. Вы думаете, они были хуже всех других жителей Иерусалима? 5Нет, но говорю вам: если вы не раскаетесь, то тоже погибнете, как они.

Притча о бесплодном дереве

6Затем Иса рассказал им притчу:

– У одного человека в винограднике рос инжир. Однажды он пошёл посмотреть, нет ли на нём плодов, но ничего не нашёл. 7Тогда он сказал виноградарю: «Вот уже три года я прихожу смотреть, нет ли на этом инжире плодов, и ничего не нахожу. Сруби его, зачем он без пользы занимает место?» 8«Господин, – ответил работник, – оставь его ещё на один год. Я его окопаю, положу удобрение, 9и если в следующем году будут плоды – хорошо, а если нет, тогда ты срубишь его».

Исцеление женщины в субботу

10В субботу Иса учил в одном из молитвенных домов. 11Там была женщина, скорченная духом болезни. Она не могла выпрямиться вот уже восемнадцать лет. 12Увидев её, Иса вызвал её вперёд и сказал:

– Женщина! Ты свободна от своей болезни!

13Он возложил на неё руки, и она сразу выпрямилась и стала славить Аллаха. 14Но начальника молитвенного дома разозлило, что Иса исцелил в субботу, и он обратился к присутствующим:

– Есть шесть дней для работы, вот и приходите для исцеления не в субботу, а в один из этих дней.

15На это Иса ответил ему:

– Лицемеры! Разве в субботу вы не отвязываете в стойле вола или осла и не ведете его поить? 16Так не нужно ли было освободить в субботу и эту женщину, одну из дочерей Ибрахима, вот уже восемнадцать лет связанную Шайтаном?

17Когда Он это сказал, всем Его противникам стало стыдно, а весь народ радовался чудесным делам, которые Он совершал.

Притча о горчичном зерне и о закваске

(Мат. 13:31-33; Мк. 4:30-32)

18Затем Иса сказал:

– На что похоже Царство Аллаха? С чем можно его сравнить? 19Оно как горчичное зерно, которое человек взял и посеял в своём саду. Зерно выросло и превратилось в настоящее дерево, так что даже птицы небесные свили гнёзда в его ветвях.

20И ещё Он сказал:

– На что похоже Царство Аллаха? 21Оно как закваска, которую женщина смешала с большим количеством13:21 Букв.: «три саты». Это, вероятно, около 36 л (23 кг муки). муки, чтобы вскисло всё тесто.

Об узкой двери

(Мат. 7:13-14, 22-23; 8:11-12)

22Направляясь в Иерусалим, Иса проходил через города и селения, повсюду уча народ. 23Кто-то спросил Его:

– Повелитель, разве только немногие будут спасены?

Иса ответил:

24– Старайтесь войти через узкую дверь, потому что многие будут пытаться войти, но не смогут. 25Когда хозяин дома встанет и закроет дверь, вы будете стоять снаружи и стучать, умоляя: «Господин, открой нам». Но Он ответит: «Не знаю вас, откуда вы». 26Тогда вы скажете: «Мы ели и пили с Тобой, и Ты учил на наших улицах». 27Но Он ответит: «Я не знаю вас, откуда вы, отойдите от Меня все, делающие зло!»13:27 См. Заб. 6:9.

28Там будет плач и скрежет зубов, когда вы увидите Ибрахима, Исхака, Якуба и всех пророков в Царстве Аллаха, а сами вы будете изгнаны вон. 29Придут люди с востока и с запада, с севера и с юга и возлягут на пиру в Царстве Аллаха. 30И униженные будут возвышены, а возвышенные – унижены.

Иса аль-Масих оплакивает Иерусалим

(Мат. 23:37-39)

31Тогда же к Исе подошли несколько блюстителей Закона и сказали:

– Уходи, оставь это место, потому что Ирод13:31 Это Ирод Антипа (см. сноску на 3:1). хочет Тебя убить.

32Иса ответил:

– Пойдите и передайте этой лисице: «Я буду изгонять демонов и исцелять людей сегодня и завтра, а на третий день Я закончу Своё дело». 33Но сегодня, завтра и послезавтра Я должен следовать Своим путём, потому что не бывает так, чтобы пророка Аллаха убили ещё где-то, кроме Иерусалима!

34– О, Иерусалим, Иерусалим, убивающий пророков и побивающий камнями посланных к тебе! Сколько раз Я хотел собрать твоих детей, как птица собирает своих птенцов под крылья, но вы не захотели! 35А теперь ваш дом оставляется вам пустым13:35 См. Иер. 22:5.. Говорю вам, что вы уже не увидите Меня до тех пор, пока не скажете: «Благословен Тот, Кто приходит во имя Вечного!»13:35 Заб. 117:26.