Levitiko 27 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 27:1-34

Kuwombola Zomwe ndi za Yehova

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole, 3mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60. 4Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu. 5Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi. 6Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva. 7Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi. 8Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.

9“ ‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika. 10Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika. 11Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe, 12ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake. 13Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.

14“ ‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake. 15Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.

16“ ‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu. 17Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa. 18Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo. 19Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake. 20Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso. 21Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.

22“ ‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake, 23wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova. 24Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake. 25Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.

26“ ‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova. 27Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.

28“ ‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.

29“ ‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.

30“ ‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova. 31Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo. 32Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova. 33Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’ ”

34Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.

New Serbian Translation

3. Мојсијева 27:1-34

Заветовани дарови

1Господ рече Мојсију: 2„Говори Израиљцима и реци им: ’Ако неко заветује Господу особу, али хоће да се откупи, овако ћеш вршити процену: 3мушкарца између двадесет и шездесет година старости процени на педесет сребрних шекела27,3 Око 580 gr. према храмском шекелу27,3 Око 12 gr.. 4Ако се ради о жени процени је на тридесет шекела27,4 Око 345 gr.. 5Мушко између пет и двадесет година старости процени на двадесет сребрних шекела27,5 Око 230 gr., а женско на десет шекела27,5 Око 115 gr.. 6Мушко између месец дана и пет година старости процени на пет сребрних шекела27,6 Око 58 gr., а женско на три сребрна шекела27,6 Око 35 gr.. 7Мушко од шездесет година и старије процени на петнаест шекела27,7 Око 175 gr., а женско на десет шекела. 8Уколико особа не може да плати процењену вредност, нека дође к свештенику, који ће га проценити; свештеник ће проценити онога који чини завет према његовим могућностима.

9Ако неко доноси живинче као принос Господу, што год се даје Господу, свето је. 10Добро живинче се не сме надоместити, нити заменити за лоше, или лоше живинче за добро. Ако се једно живинче замени другим, тада ће и заветовано и замењено бити свето. 11Ако је живинче нечисто, те није од оних које се могу принети Господу, нека га донесе пред свештеника. 12Нека га свештеник процени према томе да ли је добро или лоше. Какву му вредност свештеник одреди, тако ће бити. 13Ако власник хоће да га откупи, нека дода једну петину на процењену вредност.

14Ако неко заветује своју кућу Господу, нека свештеник процени кућу према томе да ли је добра или лоша. Какву му вредност свештеник одреди, тако ће бити. 15Уколико онај који заветује своју кућу хоће да је откупи, нека дода једну петину на процењени износ, и биће његова.

16Ако неко заветује Господу једну њиву од свог породичног имања, процени је према количини семена које иде у сетву: за један хомер27,16 Један хомер захвата око 220 l. јечменог семена педесет сребрних шекела27,16 Око 580 gr.. 17Ако заветује своју њиву у опросној години, процењена вредност остаје иста. 18Ако своју њиву заветује након опросне године, свештеник ће прорачунати цену према броју година које преостају до наредне опросне године, па ће се њена процењена вредност сразмерно умањити. 19Ако онај који заветује њиву пожели да је откупи, нека дода једну петину на процењену вредност, и биће његова. 20У случају да не откупи њиву, него је прода другоме, више је не може откупити. 21Кад њива буде ослобођена у опросној години, нека буде посвећена као њива заветована Господу и постане свештеникова имовина.

22Ако неко заветује Господу њиву коју је купио, али није део његовог породичног имања, 23нека свештеник прорачуна њену вредност према процени до опросне године, и нека истога дана исплати процењени износ као ствар посвећену Господу. 24У опросној години њива ће се вратити ономе од кога ју је купио; ономе који држи њиву у поседу. 25Свака процена ће се вршити према храмском шекелу: у једном шекелу има двадесет гера27,25 Око 12 gr..

26Првина стоке, пошто је првина, припада Господу, и зато се не може заветовати. Било во или овца, оно припада Господу. 27Ако је то једна од нечистих животиња, она се може откупити по процењеној вредности додавши петину цене. Ако се не откупи, нека се прода по процењеној вредности.

28Шта год неко има, па заветом посвети Господу, било то особа, живинче, или њива на породичном имању, не сме се продати, нити откупити. Све што је заветом посвећено, најсветије је Господу.

29Ниједна особа, која је одређена за клето уништење, не сме се откупити: мора свакако да се погуби.

30Десетак од сваког земаљског семена и од плодова са стабала припада Господу: то је свето Господу. 31Ако неко хоће да откупи део свог десетка, нека дода на то петину цене. 32Десетак од све крупне и ситне стоке, свако десето од оног што пролази испод пастирског штапа, нека буде свето Господу. 33Нека нико не испитује је ли добро или лоше, и нека се не замењује. А ако се замени, тада ће и прво и замењено бити свето; не сме се откупити.’“

34Ово су заповести које је Господ дао Мојсију за Израиљце на Синајској гори.