Levitiko 21 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 21:1-24

Malamulo a Ansembe

1Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake. 2Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake, 3kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha. 4Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.

5“ ‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo. 6Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.

7“ ‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo. 8Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.

9“ ‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.

10“ ‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni. 11Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake. 12Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.

13“ ‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna. 14Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake, 15kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’ ”

16Yehova anawuza Mose kuti, 17“Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake. 18Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri, 19munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala, 20kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi. 21Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake. 22Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika. 23Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’ ”

24Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.

O Livro

Levítico 21:1-24

Leis para os sacerdotes

1O Senhor disse a Moisés: “Diz aos sacerdotes, filhos de Aarão, que nunca se contaminem, tocando numa pessoa morta, 2a menos que se trate de um parente próximo, como mãe, pai, filho, filha, irmão, 3ou uma irmã solteira por quem tenha uma responsabilidade especial pelo facto de ela não ter marido. 4Porque o sacerdote é um responsável entre o povo e não deve ficar cerimonialmente impuro, como acontece com as outras pessoas.

5O sacerdote não deverá cortar o cabelo de forma a deixar pedaços de calva na cabeça; tão-pouco fará isso na barba. Não fará incisões, dando golpes na sua carne. 6Serão santos para o seu Deus e não deverão desonrar o meu nome; doutra forma tornar-se-ão indignos de fazerem ofertas queimadas ao Senhor, seu Deus.

7Um sacerdote não se casará com uma prostituta, nem com uma divorciada, porque é um homem santo de Deus. 8O sacerdote é consagrado para oferecer sacrifícios a vosso Deus; ele é santo, porque eu o Senhor que vos santifica sou santo.

9A filha de um sacerdote que se tornar prostituta, violando a santidade do seu pai, e a sua própria, será queimada.

10O sumo sacerdote, ungido com o azeite especial de unção e trazendo o seu vestuário especial, não deverá deixar os cabelos despenteados, em sinal de luto, nem raspar as suas vestes; 11tão-pouco deve permanecer na presença duma pessoa morta, mesmo que seja o seu pai ou a sua mãe. 12Não deixará o santuário, nem tomará o meu tabernáculo como se fosse uma habitação vulgar; porque tem sobre si a unção do azeite santo que o consagrou para Deus. Eu sou o Senhor.

13Deverá casar com uma virgem. 14Não pode casar com uma viúva, nem com uma mulher divorciada, nem com uma prostituta. A sua mulher deve ser virgem dentre o seu povo, 15pois assim não profanará a sua descendência, pois eu sou o Senhor que o santifico.”

16E o Senhor disse a Moisés: 17“Diz a Aarão que qualquer dos seus descendentes, e isto por todas as gerações, que tenha algum defeito corporal não pode oferecer sacrifícios a Deus. 18Por exemplo, se um homem for cego ou coxo, ou se tiver o nariz partido ou os membros deformados; 19ou ainda se tiver uma mão ou um pé partido, 20ou for corcunda ou anão, ou se tiver defeito na vista, ou impigens e sarna na pele, ou testículos imperfeitos, 21ainda que sendo filho de Aarão, não tem autorização para oferecer ofertas de comida ao Senhor, por causa do seu defeito físico. 22No entanto, será alimentado com a comida dos sacerdotes, das ofertas apresentadas a Deus, tanto dos sacrifícios santos como dos santíssimos. 23Mas não poderá chegar perto do véu, nem aproximar-se do altar, porque tem um defeito físico; isso profanaria o meu santuário, porque eu, o Senhor, os santifico.”

24Moisés deu estas instruções a Aarão e aos seus filhos, assim como a todo o povo de Israel.