Levitiko 20 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 20:1-27

Zilango za Tchimo

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala. 3Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera. 4Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha, 5Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”

6“ ‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.

7“ ‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu. 8Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.

9“ ‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.

10“ ‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.

11“ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.

12“ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

13“ ‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

14“ ‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.

15“ ‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.

16“ ‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

17“ ‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.

18“ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.

19“ ‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.

20“ ‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.

21“ ‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.

22“ ‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni. 23Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo. 24Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.

25“ ‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu. 26Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.

27“ ‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’ ”

Thai New Contemporary Bible

เลวีนิติ 20:1-27

โทษทัณฑ์ของบาป

1องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสว่า 2“จงกล่าวแก่ชนอิสราเอลว่า ‘ผู้ใดก็ตามไม่ว่าชาวอิสราเอลหรือคนต่างด้าวซึ่งมาอาศัยอยู่กับพวกเขา ที่ยก20:2 หรือถวายบูชาเช่นเดียวกับข้อ 3 และ 4ลูกหลานของตนให้พระโมเลคจะต้องตาย ประชากรในชุมชนจะเอาหินขว้างเขา 3เราเองจะเป็นปฏิปักษ์กับคนนั้น และตัดเขาออกจากหมู่ประชากรของเขา เพราะการที่เขายกลูกให้พระโมเลคก็ทำให้สถานนมัสการของเราเป็นมลทินและลบหลู่นามอันบริสุทธิ์ของเรา 4และหากประชากรในชุมชนทำเป็นไม่รู้ไม่เห็น ไม่ยอมประหารคนนั้นที่ยกลูกให้พระโมเลค 5เราจะเป็นศัตรูกับคนนั้นและครอบครัวของเขา และจะตัดเขากับทุกคนที่ทำตามเขาที่ขายตัวให้พระโมเลคออกจากหมู่ประชากรของเขา

6“ ‘เราจะเป็นศัตรูกับผู้ที่หันไปหาคนทรงและหมอผี ทำตัวแพศยาโดยการติดตามคนเหล่านี้ และเราจะตัดคนนั้นออกจากหมู่ประชากรของเขา

7“ ‘จงชำระตัวและจงบริสุทธิ์ เพราะเราคือพระยาห์เวห์พระเจ้าของเจ้า 8จงรักษาและปฏิบัติตามกฎหมายของเรา เราคือพระยาห์เวห์ผู้ทำให้เจ้าบริสุทธิ์20:8 หรือผู้ชำระเจ้าให้บริสุทธิ์หรือผู้ที่แยกเจ้าไว้ให้บริสุทธิ์

9“ ‘ผู้ใดแช่งด่าบิดามารดาของตนจะต้องมีโทษถึงตาย เขาได้แช่งด่าบิดามารดาของเขาเอง ที่เขาต้องตายนั้นก็เพราะความผิดของเขาเอง

10“ ‘ผู้ใดเป็นชู้กับภรรยาของคนอื่น คือกับภรรยาของเพื่อนบ้าน ทั้งชายและหญิงที่เป็นชู้กันจะต้องถูกประหาร

11“ ‘ผู้ใดหลับนอนกับภรรยาของบิดา ก็ทำให้บิดาของตนอับอายขายหน้า ทั้งชายและหญิงคู่นั้นจะต้องตาย ที่พวกเขาต้องตายนั้นก็เพราะความผิดของพวกเขาเอง

12“ ‘ผู้ใดหลับนอนกับบุตรสะใภ้ของตน ทั้งคู่ต้องถูกประหารเพราะได้ทำสิ่งที่วิปริต ที่พวกเขาต้องตายนั้นก็เพราะความผิดของพวกเขาเอง

13“ ‘ผู้ใดสมสู่รักร่วมเพศ พวกเขาทำสิ่งที่น่ารังเกียจเดียดฉันท์ จะต้องประหารทั้งคู่ ที่พวกเขาต้องตายนั้นก็เพราะความผิดของพวกเขาเอง

14“ ‘ผู้ใดแต่งงานกับทั้งหญิงสาวและแม่ของนาง นั่นเป็นความชั่วช้า ทั้งสามคนจะต้องถูกเผา เพื่อไม่ให้มีความชั่วร้ายท่ามกลางพวกเจ้า

15“ ‘ชายใดสมสู่กับสัตว์ จงประหารทั้งคนและสัตว์

16“ ‘หญิงใดสมสู่กับสัตว์ จงประหารทั้งคนและสัตว์ ที่เขาต้องตายนั้นก็เพราะความผิดของเขาเอง

17“ ‘ชายใดแต่งงานและมีเพศสัมพันธ์กับพี่สาวหรือน้องสาวของตน แม้จะต่างบิดาหรือต่างมารดา ก็เป็นการกระทำอันน่าละอาย ทั้งสองคนจะต้องถูกตัดออกไปต่อหน้าต่อตาหมู่ประชากรของพวกเขา เขาทำให้พี่สาวน้องสาวต้องอับอายขายหน้าและเขาจะต้องรับผิดชอบ

18“ ‘ชายใดหลับนอนและมีเพศสัมพันธ์กับหญิงที่กำลังมีประจำเดือน ทั้งคู่จะต้องถูกตัดออกจากหมู่ประชากรของพวกเขา เพราะเขาได้เปิดเผยแหล่งโลหิตของนาง และนางก็ได้เปิดเผยด้วย

19“ ‘ชายใดมีเพศสัมพันธ์กับป้า น้า หรืออาของตน ก็ทำให้ญาติสนิทอับอายขายหน้า ทั้งคู่จะต้องรับผิดชอบ

20“ ‘ชายใดหลับนอนกับป้าสะใภ้ น้าสะใภ้ หรืออาสะใภ้ ก็ทำให้ลุง น้า หรืออาอับอายขายหน้า พวกเขาจะต้องรับผิดชอบและตายโดยปราศจากผู้สืบสกุล

21“ ‘ชายใดแต่งงานกับพี่สะใภ้หรือน้องสะใภ้ของตน เป็นการกระทำอันไม่บริสุทธิ์ เขาทำให้พี่ชายน้องชายต้องอับอายขายหน้า คนทั้งคู่จะไม่มีบุตรสืบสกุล

22“ ‘จงถือรักษาและปฏิบัติตามกฎหมายและบทบัญญัติทั้งสิ้นของเรา เพื่อดินแดนที่เรากำลังจะนำเจ้าทั้งหลายเข้าไปอาศัยจะไม่สำรอกพวกเจ้าออกมา 23เจ้าอย่าได้ดำเนินตามขนบธรรมเนียมของประชาชาติทั้งหลายที่เรากำลังจะขับไล่ออกไปต่อหน้าเจ้า เพราะพวกเขาทำสิ่งทั้งปวงเหล่านี้ เราจึงชิงชังพวกเขา 24แต่เราพูดกับเจ้าว่า “เจ้าจะครอบครองดินแดนของพวกเขา เราจะให้ดินแดนนั้นเป็นกรรมสิทธิ์ของเจ้า เป็นดินแดนอันอุดมด้วยน้ำนมและน้ำผึ้ง” เราคือพระยาห์เวห์พระเจ้าของเจ้าผู้แยกเจ้าออกจากชนชาติเหล่านั้น

25“ ‘ฉะนั้นเจ้าต้องแยกแยะระหว่างสัตว์และนกที่เป็นมลทินและไม่เป็นมลทิน อย่าปล่อยตัวแปดเปื้อนมลทินด้วยสัตว์ นก สัตว์ที่เลื้อยคลาน ซึ่งเราได้สั่งห้ามเจ้าแล้ว 26เจ้าต้องบริสุทธิ์สำหรับเรา20:26 หรือเป็นคนบริสุทธิ์ของเรา เพราะเราผู้เป็นพระยาห์เวห์เป็นผู้บริสุทธิ์ และได้แยกเจ้าออกจากชาติอื่นๆ ทั้งปวง เพื่อเป็นกรรมสิทธิ์ของเรา

27“ ‘คนทรงทั้งหญิงและชายหรือพ่อมดหมอผีท่ามกลางพวกเจ้าจะต้องตาย เจ้าจะต้องเอาหินขว้างพวกเขา ที่พวกเขาต้องตายนั้นก็เพราะความผิดของพวกเขาเอง’ ”