Levitiko 18 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 18:1-30

Kugonana Koletsedwa

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu. 3Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo. 4Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu. 5Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.

6“ ‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.

7“ ‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.

8“ ‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.

9“ ‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.

10“ ‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.

11“ ‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.

12“ ‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.

13“ ‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.

14“ ‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.

15“ ‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.

16“ ‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.

17“ ‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.

18“ ‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.

19“ ‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.

20“ ‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.

21“ ‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.

22“ ‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.

23“ ‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.

24“ ‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera. 25Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo. 26Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi, 27pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa. 28Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.

29“ ‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake. 30Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

Thai New Contemporary Bible

เลวีนิติ 18:1-30

ความสัมพันธ์ทางเพศที่ผิดธรรมบัญญัติ

1องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสว่า 2“ให้แจ้งชนอิสราเอลว่า ‘เราคือพระยาห์เวห์พระเจ้าของเจ้า 3เจ้าอย่าประพฤติตนตามอย่างชาวอียิปต์ซึ่งเจ้าทั้งหลายเคยอาศัยอยู่ด้วย และเจ้าอย่าทำอย่างชาวคานาอันในดินแดนซึ่งเรากำลังจะพาพวกเจ้าไป อย่าทำตามอย่างพวกเขา 4จงเชื่อฟังบทบัญญัติของเราและใส่ใจทำตามกฎหมายของเรา เราคือพระยาห์เวห์พระเจ้าของเจ้า 5จงทำตามกฎหมายและบทบัญญัติของเรา เพราะผู้ใดที่เชื่อฟังจะมีชีวิตอยู่โดยสิ่งเหล่านี้ เราคือพระยาห์เวห์

6“ ‘อย่าให้ผู้ใดในพวกเจ้าเข้าหาและมีเพศสัมพันธ์กับญาติสนิท เราคือพระยาห์เวห์

7“ ‘อย่าทำให้บิดาอับอายขายหน้าโดยมีเพศสัมพันธ์กับมารดาของเจ้า นางเป็นมารดาของเจ้า อย่ามีเพศสัมพันธ์กับนาง

8“ ‘อย่าทำให้บิดาอับอายขายหน้าโดยมีเพศสัมพันธ์กับภรรยาของบิดา

9“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับพี่สาวน้องสาวของเจ้า ไม่ว่าจะเป็นลูกสาวของบิดาหรือของมารดาเจ้า ไม่ว่าเกิดในบ้านเดียวกันหรือเกิดคนละที่

10“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับหลานสาวของเจ้าซึ่งทำให้ตัวเจ้าเองอับอายขายหน้า

11“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับลูกสาวของภรรยาของบิดาซึ่งเป็นเลือดเนื้อเชื้อไขของบิดาเจ้า เพราะนางคือพี่น้องของเจ้า

12“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับป้าหรืออาเพราะเป็นญาติสนิทของบิดาเจ้า

13“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับป้าหรือน้าเพราะเป็นญาติสนิทของมารดาเจ้า

14“ ‘อย่าทำให้พี่ชายหรือน้องชายของบิดาเจ้าอับอายขายหน้า โดยมีเพศสัมพันธ์กับภรรยาของเขา เพราะนางเป็นป้าสะใภ้หรืออาสะใภ้ของเจ้า

15“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับบุตรสะใภ้ของเจ้า นางเป็นภรรยาของบุตรชายของเจ้า อย่ามีเพศสัมพันธ์กับนาง

16“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับภรรยาของพี่ชายหรือของน้องชายเจ้าเพราะนั่นทำให้พี่น้องของเจ้าอับอายขายหน้า

17“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับหญิงคนใดและกับลูกสาวของนาง และอย่ามีเพศสัมพันธ์กับหลานสาวของนาง เพราะหญิงเหล่านั้นเป็นญาติสนิทของนาง การทำเช่นนั้นเป็นความชั่ว

18“ ‘อย่าเอาพี่สาวหรือน้องสาวของภรรยาของเจ้ามาเป็นคู่แข่งของนาง อย่ามีเพศสัมพันธ์กับพี่น้องของภรรยา ขณะที่ภรรยายังมีชีวิตอยู่

19“ ‘อย่าเข้าหาเพื่อมีเพศสัมพันธ์กับหญิงที่กำลังมีประจำเดือน

20“ ‘อย่ามีเพศสัมพันธ์กับภรรยาของเพื่อนบ้าน อันเป็นการสร้างมลทินแก่ตัวเองร่วมกับนาง

21“ ‘อย่าเอาลูกหลานลุยไฟเซ่นบูชาพระโมเลค อย่าหมิ่นประมาทพระนามพระเจ้าของเจ้า เราคือพระยาห์เวห์

22“ ‘อย่าสมสู่รักร่วมเพศอันเป็นสิ่งน่ารังเกียจเดียดฉันท์

23“ ‘อย่าสมสู่กับสัตว์ทำให้ตัวเองเป็นมลทิน ผู้หญิงก็ห้ามทอดกายให้สัตว์สมสู่ด้วย นั่นเป็นความวิปริต

24“ ‘อย่าทำตัวให้มีมลทินด้วยเหตุใดๆ ในข้อเหล่านี้ ซึ่งเป็นการกระทำของชนชาติต่างๆ ซึ่งเรากำลังจะขับไล่ออกไปให้พ้นหน้าเจ้า 25ทั่วดินแดนนั้นแปดเปื้อนมลทิน เราจึงลงโทษบาปของเขาเหล่านั้นและแผ่นดินกำลังสำรอกผู้ที่อาศัยอยู่ที่นั่นออกมา 26แต่เจ้าต้องถือรักษากฎหมายและบทบัญญัติของเรา ทั้งชนอิสราเอลโดยกำเนิดและคนต่างด้าวซึ่งอาศัยอยู่ในหมู่พวกเจ้า จะต้องไม่ทำสิ่งที่น่ารังเกียจเหล่านี้ 27เพราะประชาชนในดินแดนตรงหน้าเจ้าได้ทำสิ่งเหล่านี้ แผ่นดินนั้นจึงเป็นมลทิน 28และหากเจ้าทำให้แผ่นดินเป็นมลทิน แผ่นดินนั้นก็จะสำรอกพวกเจ้าออกมา เหมือนที่ได้สำรอกชนชาติต่างๆ ออกมาก่อนหน้าเจ้า

29“ ‘ทุกคนที่ทำสิ่งน่ารังเกียจอย่างใดอย่างหนึ่งเหล่านี้ จะต้องถูกตัดออกจากหมู่ประชากรของเขา 30ฉะนั้นจงปฏิบัติตามข้อกำหนดของเรา อย่าดำเนินตามเยี่ยงอย่างอันน่ารังเกียจเหล่านี้ ซึ่งทำกันอยู่ก่อนหน้าพวกเจ้าเข้ามา อย่าทำตัวแปดเปื้อนไปกับพวกเขา เราคือพระยาห์เวห์พระเจ้าของเจ้า’ ”