Levitiko 17 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 17:1-16

Za Kusadya Magazi

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi: 3Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa, 4mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake. 5Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano. 6Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova. 7Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’ ”

8“Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse 9popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’ ”

10“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake. 11Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo. 12Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’ ”

13“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi, 14chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.

15“ ‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa. 16Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’ ”

Священное Писание

Левит 17:1-16

Запрет приносить жертву вне святилища

1Вечный сказал Мусе:

2– Говори с Харуном, с его сыновьями и со всеми исраильтянами и скажи им: «Так повелел Вечный: 3всякий исраильтянин, который приносит в жертву вола17:3 Или: «корову»., ягнёнка или козлёнка в лагере или вне его, 4вместо того чтобы привести его к входу в шатёр встречи и принести его в жертву Вечному перед священным шатром Вечного, повинен в кровопролитии. Он пролил кровь и будет исторгнут из своего народа. 5Это установление велит, чтобы исраильтяне приносили Вечному те жертвы, которые они ныне совершают в открытом поле. Они должны приносить их к Вечному, к священнослужителю у входа в шатёр встречи, и приносить Вечному в жертву примирения. 6Пусть священнослужитель окропит кровью жертвенник Вечного у входа в шатёр встречи и сжигает жир для благоухания, приятного Вечному. 7Пусть они не приносят больше жертв демонам, с которыми они блудят, – демонам в образе козлов. Это установление для них и грядущих поколений будет вечным».

8Скажи им: «Любой исраильтянин или живущий у вас чужеземец, который приносит всесожжение или жертву, 9но не приносит её к входу в шатёр встречи, чтобы совершить жертву Вечному, будет исторгнут из своего народа».

Запрет употреблять в пищу кровь

10«Я обращу Моё лицо против любого исраильтянина или живущего у вас чужеземца, который будет есть кровь, и исторгну его из народа. 11Ведь жизнь всего живого – в его крови, и Я дал её вам, чтобы вы совершали очищение на жертвеннике. Это кровь, которая очищает вас. 12Поэтому Я и говорю исраильтянам: пусть никто из вас не ест кровь, и пусть живущий у вас чужеземец не ест кровь.

13Любой исраильтянин или живущий у вас чужеземец, который добудет на охоте животное или птицу, годную в пищу, должен выцедить кровь и прикрыть её землёй, 14потому что жизнь всего живого – в его крови. Поэтому Я и сказал исраильтянам: не ешьте крови никакого существа, ведь жизнь всего живого – в его крови. Любой, кто ест её, будет исторгнут.

15Пусть уроженец страны или поселенец, который поест падаль или растерзанное дикими зверями животное, выстирает одежду и вымоется сам, он будет нечист до вечера; после этого он будет чист. 16Но если он не выстирает одежду и не вымоется, он подлежит наказанию».