Levitiko 16 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 16:1-34

Tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo

1Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose. 2Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.

3“Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. 4Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi. 5Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.

6“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake. 7Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. 8Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele. 9Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo. 10Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.

11“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja. 12Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani. 13Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe. 14Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.

15“Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho. 16Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo. 17Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.

18“Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe. 19Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.

20“Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe. 21Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu. 22Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.

23“Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko. 24Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu. 25Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.

26“Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa. 27Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe. 28Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.

29“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu, 30chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova. 31Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya. 32Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika. 33Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.

34“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.”

Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.

New International Reader’s Version

Leviticus 16:1-34

The Day When Sin Is Paid For

1The Lord spoke to Moses after two of Aaron’s sons had died. They were the sons who died when they came near the Lord. 2The Lord said to Moses, “Speak to your brother Aaron. Tell him not to come into the Most Holy Room just anytime he wants to. Tell him not to come behind the curtain in front of the cover of the ark. The cover is the place where sin is paid for. If he comes behind the curtain, he will die. That is because I appear in the cloud over the cover.

3“Aaron must not enter the area of the Most Holy Room without bringing a sacrifice. He must bring a young bull for a sin offering. He must also bring a ram for a burnt offering. 4He must put on the sacred inner robe made out of linen. He must wear linen underwear next to his body. He must tie the linen belt around him. And he must put the linen turban on his head. Those are sacred clothes. So he must take a bath before he puts them on. 5The community of Israel must give him two male goats and a ram. The goats are for a sin offering. The ram is for a burnt offering.

6“Aaron must offer the bull for his own sin offering. It will pay for his own sin and the sin of his whole family. 7Then he must take the two goats and bring them to me at the entrance to the tent of meeting. 8He must cast lots for the two goats. One lot is for me. The other is for the goat that carries the people’s sins away. 9Aaron must bring the goat chosen for me by lot. He must sacrifice it for a sin offering. 10But the goat chosen by the other lot must remain alive. First, it must be brought in to me to pay for the people’s sins. Then, it must be sent into the desert as a goat that carries the people’s sins away.

11“Aaron must bring the bull for his own sin offering. It will pay for his own sin and the sin of his whole family. He must kill the bull for his own sin offering. 12He must take a shallow cup full of burning coals from the altar in my sight. He must get two handfuls of incense completely ground up. The incense must smell sweet. He must take the cup and the incense behind the curtain. 13He must put the incense on the fire in my sight. The smoke from the incense will hide the cover of the ark where the tablets of the covenant law are kept. The cover is the place where sin is paid for. Aaron must burn the incense so that he will not die. 14He must dip his finger in the bull’s blood. He must sprinkle it on the front of the cover of the ark. He must sprinkle some in front of the cover. He must do it seven times.

15“Then Aaron must kill the goat for the sin offering for the people. He must take its blood behind the curtain. There he must do the same thing with it as he did with the bull’s blood. He must sprinkle it on the cover of the ark. He must also sprinkle some in front of it. 16That is how he will make the Most Holy Room pure. He must do it because the Israelites are not ‘clean.’ They have not obeyed me. They have also committed other sins. Aaron must do the same for the tent of meeting because it stands in the middle of the camp. And the camp is ‘unclean.’ 17Aaron will go into the Most Holy Room to pay for the people’s sin. While Aaron is there, no one may be in the tent of meeting. No one may enter the tent until Aaron comes out. He will not come out until he has paid for his own sin and the sin of his whole family. He will not come out until he has also paid for the sin of the whole community of Israel.

18“Then he will come out to the altar for burnt offerings. It is in front of the tent where the ark of the Lord is. He will make the altar pure and clean. He will take some of the bull’s blood and some of the goat’s blood. Then he will put the blood on all the horns that stick out from the upper four corners of the altar. 19He will sprinkle some of the blood on it with his finger seven times. He will do it to make the altar pure. He will do it to set it apart from the Israelites. They are ‘unclean.’

20“Aaron will finish making the Most Holy Room pure and ‘clean.’ He will finish making the tent of meeting and the altar pure. Then he will bring out the live goat. 21He must place both of his hands on its head. While he does that, he must tell me about all the sins the Israelites have committed. He must tell me about all their evil acts and the times they did not obey me. In that way he puts their sins on the goat’s head. Then he will send the goat away into the desert. The goat will be led away by a man appointed to do it. 22The goat will carry all their sins on itself to a place where there are no people. And the man will set the goat free in the desert.

23“Then Aaron must go into the tent of meeting. He must take off the linen clothes he put on before he entered the Most Holy Room. He must leave them there. 24He must take a bath in the holy area. And he must put on his regular clothes. Then he will come out and sacrifice the burnt offering for himself. He will also sacrifice the burnt offering for the people. That will pay for his own sin and the people’s sin. 25He will also burn the fat of the sin offering on the altar.

26“The man who sets free the goat that carries the people’s sins away must wash his clothes. He must take a bath. After that, he can come back into the camp. 27The bull and the goat for the sin offerings must be taken outside the camp. Their blood was brought into the Most Holy Room. It paid for sin. The hides, meat and guts of the animals must be burned up. 28The man who burns them must wash his clothes. He must take a bath. After that, he can come back into the camp.

29“Here is a law for you that will last for all time to come. On the tenth day of the seventh month you must not eat anything. You must not do any work. It does not matter whether you are Israelites or outsiders. 30On that day your sin will be paid for. You will be made pure and clean. You will be clean from all your sins in my sight. 31That day is a sabbath for you. You must rest on it. You must not eat anything on that day. This is a law that will last for all time to come. 32The high priest must pay for sin. He must make everything pure and clean. He has been anointed and prepared to become the next high priest after his father. He must put on the sacred clothes that are made out of linen. 33He must make the Most Holy Room, the tent of meeting and the altar pure. And he must pay for the sin of the priests and all the members of the community.

34“Here is a law for you that will last for all time to come. Once a year you must pay for all the sin of the Israelites.”

So it was done, just as the Lord commanded Moses.