Levitiko 12 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 12:1-8

Kudziyeretsa kwa Mkazi Atabala Mwana

1Yehova anayankhula ndi Mose kuti, 2“Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba. 3Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe. 4Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha. 5Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.

6“ ‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. 7Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake.

“ ‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi. 8Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

利未记 12:1-8

产妇洁净的条例

1耶和华对摩西说: 2“你把以下条例告诉以色列人。

“如果有妇人生了男婴,她就要不洁净七天,像在经期内不洁净一样。 3第八天,婴儿要接受割礼。 4妇人因产后流血,要等三十三天才能洁净。其间,不可接触任何圣物,也不可进入圣所。 5如果妇人生的是女婴,她就要不洁净十四天,像在经期内不洁净一样。她因产后流血,要等六十六天才能洁净。 6不论她生男生女,洁净期满后,都要预备一只一岁的羊羔作燔祭、一只雏鸽或斑鸠作赎罪祭,带到会幕门口交给祭司。 7祭司要在耶和华面前献祭,为她赎罪,她就洁净了。这是有关产妇的条例。 8她若负担不起一只羊羔,可以带两只斑鸠或雏鸽来,一只作燔祭,一只作赎罪祭。祭司为她赎罪后,她就洁净了。”