Hoseya 6 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 6:1-11

Kusalapa kwa Israeli

1“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova.

Iye watikhadzula,

koma adzatichiritsa.

Iye wativulaza,

koma adzamanga mabala athu.

2Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa;

pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa

kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.

3Tiyeni timudziwe Yehova,

tiyeni tilimbike kumudziwa Iye.

Adzabwera kwa ife mosakayikira konse

ngati kutuluka kwa dzuwa;

adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe,

ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”

4Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani?

Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda?

Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa,

ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.

5Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga,

ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga;

chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.

6Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe,

ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.

7Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa,

iwo sanakhulupirike kwa Ine.

8Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa,

okhala ndi zizindikiro za kuphana.

9Monga momwe mbala zimadikirira anthu,

magulu a ansembe amachitanso motero;

iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu,

kupalamula milandu yochititsa manyazi.

10Ndaona chinthu choopsa kwambiri

mʼnyumba ya Israeli.

Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere,

ndipo Israeli wadzidetsa.

11“Kunenanso za iwe Yuda,

udzakolola chilango.

“Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”

New Russian Translation

Осия 6:1-11

Нераскаявшийся Израиль

1– В своем страдании они будут настойчиво искать Меня:

«Пойдем и вернемся к Господу.

Он поразил нас,

но Он же и исцелит нас.

Он поранил нас,

но Он же и перевяжет наши раны.

2Через два дня Он оживит нас,

а на третий день Он восстановит нас,

чтобы мы жили в Его присутствии.

3Узнаем же Господа,

будем стремиться узнать Его.

То, что Он придет,

верно как и то, что взойдет солнце.

Он придет к нам, как дождь,

подобно весенним дождям,

что орошают землю».

4– Что же Мне делать с тобой, Ефрем?

Что же Мне делать с тобой, Иудея?

Ваша верность – как утренний туман,

словно роса, что вскоре исчезает.

5Поэтому Я резал вас на куски через Моих пророков,

Я убивал вас словами Моих уст.

Словно молния, вспыхнул Мой суд над вами.

6Ведь Я милости хочу, а не жертвы,

и познания Бога более, нежели всесожжения.

7Подобно Адаму6:7 Или: «Как в городе Адаме»., вы нарушили завет;

там вы не были Мне верны.

8Галаад – город нечестивых людей,

запятнан кровью.

9Сборище священников подобно разбойникам,

которые сидят в засаде в ожидании человека.

Они убивают на пути в Шехем,

совершая гнусные преступления.

10В доме Израиля Я увидел ужасную вещь:

Там Ефрем предается распутству,

Израиль осквернил себя.

11И для тебя, Иудея,

назначена жатва.

Когда Я верну Мой народ из плена,