Hoseya 6 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 6:1-11

Kusalapa kwa Israeli

1“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova.

Iye watikhadzula,

koma adzatichiritsa.

Iye wativulaza,

koma adzamanga mabala athu.

2Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa;

pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa

kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.

3Tiyeni timudziwe Yehova,

tiyeni tilimbike kumudziwa Iye.

Adzabwera kwa ife mosakayikira konse

ngati kutuluka kwa dzuwa;

adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe,

ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”

4Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani?

Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda?

Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa,

ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.

5Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga,

ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga;

chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.

6Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe,

ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.

7Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa,

iwo sanakhulupirike kwa Ine.

8Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa,

okhala ndi zizindikiro za kuphana.

9Monga momwe mbala zimadikirira anthu,

magulu a ansembe amachitanso motero;

iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu,

kupalamula milandu yochititsa manyazi.

10Ndaona chinthu choopsa kwambiri

mʼnyumba ya Israeli.

Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere,

ndipo Israeli wadzidetsa.

11“Kunenanso za iwe Yuda,

udzakolola chilango.

“Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”

Het Boek

Hosea 6:1-11

Gods verlangen naar Israël

1‘Zij zullen zeggen: “Kom, laten we teruggaan naar de Here. Hij heeft ons verscheurd, Hij zal ons ook genezen. Hij heeft ons geslagen, Hij zal ook onze wonden verbinden. 2Hij zal ons na twee dagen weer overeind helpen en op de derde dag zullen wij, weer helemaal opgeknapt, met Hem leven. 3Ja, wij verlangen naar de Here en Hij zal daarop reageren, zo zeker als de komst van dauw of regen in het vroege voorjaar.”

4Wat zal Ik met u doen, Israël en Juda? Want uw liefde verdwijnt als wolken in de morgen en verdampt als dauw in de vroege ochtend. 5Ik stuurde mijn profeten om u te waarschuwen voor uw ondergang. Ik heb u harde klappen toegebracht met mijn woorden en met de dood bedreigd. Onverwacht werd u getroffen door mijn veroordeling, als door een plotseling doorbrekend licht. 6Ik wil uw offers niet, Ik wil uw liefde. Ik hoef uw brandoffers niet, Ik wil dat u Mij kent.

7Maar u bent net als Adam: u hebt mijn verbond verbroken en bent Mij zo ontrouw geworden. 8De bewoners van Gilead zijn misdadigers, de stad is vol bloedsporen. 9Zij zijn als een bende bandieten die loert op slachtoffers. Troepen priesters plegen moorden op de weg naar Sichem en bedrijven schandelijke misdaden. 10Ik heb in Israël iets afschuwelijks gezien: Israël liep afgoden achterna en werd zo verontreinigd. 11Ook u, Juda, zult uw straf nog oogsten. En Ik wilde u zo graag bevrijden!’